< Ezechiela 35 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Synu człowieczy! obróć twarz swoję przeciwko górze Seir, a prorokuj przeciwko niej,
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 I mów do niej: Tak mówi panujący Pan: Otom Ja przeciwko tobie, góro Seir! a wyciągnę rękę moję na cię, i podam cię na wielkie spustoszenie.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Miasta twoje w spustoszenie obrócę, że będziesz spustoszona, i dowiesz się, żem Ja Pan.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Przeto, iż wieczną nieprzyjaźń wiedziesz, i rozpraszasz synów Izraelskich ostrzem miecza czasu utrapienia ich, czasu wykonywania kaźni ich;
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 Dlatego, jako żyję Ja, mówi panujący pan, że cię podam na zabicie, a krew cię ścigać będzie; ponieważ krwi rozlewania w nienawiści nie masz, przetoż cię krew ścigać będzie.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 I obrócę górę Seir w wielkie spustoszenie, a wygubię z niej przechodzącego, i wracającego się;
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 I napełnię góry jej pobitymi jej; na pagórkach twoich, i na dolinach twoich, i przy wszystkich strumieniach twoich pobici mieczem polegną na nich;
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Na pustynie wieczne podam cię, i w miastach twoich mieszkać nie będą; a dowiecie się, żem Ja Pan.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Przetoż iż mówisz: Te dwa narody, i te dwie ziemie moje będą a posiądziemy tę, w której Pan mieszkał;
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 Dlategoż, jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że uczynię według gniewu twego i według zawiści twojej, którąś czyniła w nienawiści swej przeciwko nim; i będę poznany od nich, gdy cię sądzić będę;
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 I dowiesz się, żem Ja Pan słyszał wszystkie urągania twoje, któreś wyrzekła przeciw górom Izraelskim, mówiąc: Spustoszone są, a nam podane są ku pożarciu.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 Boście się przeciwko mnie wynosili usty waszemi, a rozmnożyliście słowa swoje przeciwko mnie, com Ja słyszał.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Tak mówi panujący Pan: Jako się ta wszystka ziemia weseli, tak cię obrócę w pustnię.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 Jako się ty weselisz nad dziedzictwem domu Izraelskiego, przeto, że jest spustoszone, tak uczynię i tobie; będziesz spustoszona, o góro Seir! a zgoła wszystka ziemia Edomska; i dowiedzą się żem Ja Pan.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezechiela 35 >