< Ezechiela 32 >

1 A dwunastego roku, miesiąca dwunastego, pierwszego dnia tegoż miesiąca, stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Synu człowieczy! podnieś lament nad Faraonem, królem Egipskim, a powiedz mu: Podobnyś ty lwowi młodemu między narodami, tyś jest jako wieloryb w morzu, gdyż bujając po rzekach twoich mącisz wodę nogami twemi, i mięszasz rzeki jego.
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 Tak mówi panujący Pan: Rozciągnę też na cię sieć moję przez zebranie wielu narodów, którzy cię wyciągną niewodem moim;
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 I zostawię cię na ziemi, na polu porzucę cię, i sprawię, że mieszkać będzie na tobie wszelkie ptastwo niebieskie, i nakarmię tobą zwierza wszystkiej ziemi;
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 I rozrzucę mięso twoje po górach, i napełnię doliny wysokością twoją,
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 I napoję ziemię twoję, w której pływasz, krwią twoją aż do gór, tak, że i rzeki będą napełnione tobą.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 A gdy cię zgaszę, zakryję niebiosa, i ciemne uczynię gwiazdy ich, słońce obłokiem zasłonię, a księżyc nie da światła swego.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 Wszystkie światła jasne na niebiosach zaćmię dla ciebie, i przywiodę ciemność na ziemię twoję, mówi panujący Pan.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 Nadto zasmucę serce wielu narodów, gdy za sprawą moją przyjdzie wieść o starciu twojem między narody, do ziem, którycheś nie znał.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Uczynię, mówię, że się zdumieje nad tobą wiele narodów, a królowie ich zatrwożą się bardzo dla ciebie, gdy szermować będę mieczem swoim przed twarzą ich; będą się zaiste lękać co chwila każdy o duszę swoję w dzień upadku twego.
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 Bo tak mówi panujący Pan: Miecz króla Babilońskiego przyjdzie na cię.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 Mieczami mocarzów porażę zgraję twoję; najokrutniejsi ze wszystkich narodów, ci skażą pychę Egipską, i będzie zgładzone wszystko mnóstwo jego.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 Zagładzę i wszystko bydło jego, które jest przy wodach wielkich, tak, że ich więcej nie zmąci noga człowiecza, ani kopyta bydlęce mącić ich będą.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Tedy uczynię, że się wody ich ustoją, a rzeki ich jako oliwa pójdą, mówi panujący Pan.
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 Gdyż obrócę ziemię Egipską w spustoszenie, a ziemia będzie wypróżniona z pełności swojej, gdy pobiję wszystkich mieszkających w niej; i dowiedzą się, żem Ja Pan.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 Toć jest lament, którym nad nią lamentować będą; córki narodów narzekać będą nad nią, nad Egiptem i nad wszystkiem mnóstwem jego narzekać będą, mówi panujący Pan.
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 Potem dwunastego roku, piętnastego dnia tegoż miesiąca, stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc;
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 Synu człowieczy! narzekaj nad mnóstwem Egipskiem, a zepchnij je, i córki tych narodów sławnych aż do najniższych miejsc ziemi, do tych, co zstępują do dołu,
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 I mów: Nad kogożeś wdzięczniejszy? Zstąp, a połóż się z nieobrzezańcami.
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 W pośród pobitych mieczem upadną; pod miecz podany jest, wywleczcież go ze wszystką zgrają jego.
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 Mówić do niego będą najmocniejsi z mocarzów z pośrodku grobu z pomocnikami jego, którzy tam zstąpiwszy, leżą z nieobrzezańcami pobitymi mieczem. (Sheol h7585)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
22 Tam jest Assur, i wszystka zgraja jego, w około niego są groby jego; wszyscy ci pobici upadli od miecza.
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 Którego groby położone są przy stronach dołu, aby była zgraja jego w około grobu jego; ci wszyscy pobici polegli od miecza, którzy puszczali strach w ziemi żyjacych.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 Tam Elam i wszystka zgraja jego około grobu jego, ci wszyscy pobici upadli od miecza, którzy zstąpili w nieobrzezce do niskości ziemi, którzy puszczali strach swój w ziemi żyjących; jużci odnoszą hańbę swoją z tymi, którzy zstępują do dołu.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 W pośrodku pobitych postawili mu łoże, i wszystkiej zgrai jego, w około niego są groby jego; wszyscy ci nieobrzezańcy pobici są mieczem, przychodził strach ich na ziemię żyjących, jużci odnoszą hańbę swoję z tymi, którzy zstąpili do grobu, a w poś rodku pobitych położeni są.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 Tam Mesech, Tubal i wszystka zgraja jego, i w około niego groby jego, ci wszyscy nieobrzezańcy pobici mieczem, choć puszczali strach swój w ziemi żyjących.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 Aczkolwiekci jeszcze nie polegli z mocarzami, którzy upadli z nieobrzezańców, co zstąpili do grobu z wojennym orężem swoim, i położyli miecze swe pod głowy swe; a wszakże przyjdzie nieprawość ich na kości ich, chociaż strach tych mocarzów był w ziemi żyjących. (Sheol h7585)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
28 I ty w pośrodku nieobrzezańców starty będziesz, i będziesz leżał między pobitymi mieczem.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 Tam Edom, i królowie jego, i wszyscy książęta jego, którzy położeni są, z mocą swoją i z pobitymi mieczem; i ci z nieobrzezańcami leżeć będą, i z tymi, którzy zstępują do dołu.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 Tam wszyscy zgoła książęta północnej strony, i wszyscy Sydończycy, którzy zstępują do pobitych z strachem swoim, za moc swoję wstydzić się będą, i leżeć będą ci nieobrzezańcy z pobitymi mieczem, a odniosą hańbę swoję z tymi, którzy zstępują do dołu.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 Tych ujrzawszy Farao ucieszy się nad wszystką zgrają swoją, która jest mieczem pobita, Farao i wszystko wojsko jego, mówi panujący Pan.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 Bo puszczę strach mój w ziemi żyjących, i położony będzie między nieobrzezańcami z pobitymi mieczem Farao i wszystka zgraja jego, mówi panujący Pan.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezechiela 32 >