< Ezechiela 3 >

1 I rzekł do mnie: Synu człowieczy! co przed tobą jest, zjedz; zjedz te księgi, a idź i mów do domu Izraelskiego.
Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
2 Otworzyłem tedy usta swe, i dał mi zjeść one księgi,
Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
3 A mówił do mnie: Synu człowieczy! nakarm brzuch twój, a wnętrzności twoje napełnij temi księgami, któreć daję. I zjadłem je, i były w ustach moich słodkie jako miód.
Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
4 Zatem rzekł do mnie: Synu człowieczy! idź a wnijdź do domu Izraelskiego, i mów słowy mojemi do nich.
Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
5 Bo cię nie do ludu nieznajomej mowy, albo trudnego języka posyłam, ale do domu Izraelskiego;
Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
6 Nie do wielu narodów nieznajomej mowy, i trudnego języka, którychbyś słów nie zrozumiał, którzy jednak, gdybym cię do nich posłał, usłuchaliby cię.
Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
7 Lecz dom Izraelski nie będzie cię chciał usłuchać, ponieważ mnie samego usłuchać nie chcą; bo wszystek dom Izraelski jest twardego czoła i zatwardzonego serca.
Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
8 Ale otom uczynił twarz twoję twardą przeciwko twarzy ich, a czoło twe twarde przeciwko czołu ich.
Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
9 Uczyniłem czoło twe jako dyjament, i twardsze nad skałę; nie bójże się ich, ani się lękaj twarzy ich, przeto, że są domem odpornym.
Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
10 I rzekł do mnie: Synu człowieczy! wszystkie słowa moje, które mówić będę do ciebie, przyjmij do serca twego, a słuchaj uszyma twemi.
Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
11 Idź a wnijdź do pojmanych, do synów ludu twego, i mów do nich, a powiedz im: Tak mówi panujący Pan, niech oni słuchają, albo nie.
Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
12 Tedy mię duch podniósł, i słyszałem za sobą głos grzmotu wielkiego: Błogosławiona niech będzie chwała Pańska z miejsca swego;
Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
13 I szum skrzydeł onych zwierząt, które się naspół dotykały, i głos kół naprzeciwko nim, i głos grzmotu wielkiego.
Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
14 A duch podniósł mię i wziął mię. I odszedłem z gorzkością w rozgniewaniu ducha mego; ale ręka Pańska nademną mocna była.
Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
15 I przyszedłem do pojmanych do Telabib, którzy mieszkali przy rzece Chebar, i siadłem gdzie oni mieszkali, a siedziałem tam siedm dni w pośrodku ich, zdumiawszy się.
Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
16 A gdy minęło siedm dni, było słowo Pańskie do mnie mówiące:
Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
17 Synu człowieczy! Dałem cię stróżem domowi Izraelskiemu, abyś słysząc słowo z ust moich napomniał ich odemnie.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
18 Gdybym Ja rzekł niepobożnemu: Śmiercią umrzesz, a nie napomniałbyś go, i nie mówiłbyś, abyś go odwiódł od niezbożnej drogi jego, tak, żebyś go przy żywocie zachował, tedy onci niezbożny w nieprawości swojej umrze; ale krwi jego z ręki twojej szukać będę.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
19 Lecz jeźlibyś ty napomniał niezbożnego, a nie odwróciłby się od niezbożności swej, i od drogi swej niezbożnej, tedy onci w nieprawości swojej umrze; ale ty duszę swoję wybawisz.
Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
20 Także jeźliby się odwrócił sprawiedliwy od sprawiedliwości swojej, a czyniłby nieprawość, a Jabym położył zawadę przed nim, i takby umarł, a tybyś go nie napomniał: w grzechu swym umrze, a nie przyjdą na pamięć sprawiedliwości jego, które czynił, lecz krwi jego z ręki twojej szukać będę.
“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
21 Ale jeźlibyś ty napomniał sprawiedliwego, aby nie zgrzeszył ten sprawiedliwy, i nie grzeszyłby, zaiste żyć będzie, bo napomnienie przyjął, a ty duszę swoję wybawisz.
Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
22 I była tam nademną ręka Pańska, i rzekł do mnie: Wstawszy wyjdź w pole, a tam się z tobą rozmówię.
Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
23 A tak wstawszy szedłem w pole, a oto chwała Pańska stała tam, jako chwała, którąm widział u rzeki Chebar, i upadłem na oblicze moje.
Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
24 Tedy duch wstąpił w mię, a postawiwszy mię na nogi moje mówił do mnie, i rzekł mi: Wnijdź, zamknij się w domu swym.
Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
25 Bo oto na cię, synu człowieczy! włożą powrozy, i zwiążą cię niemi, a nie będziesz mógł wynijść między nich.
Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
26 A Ja uczynię, że język twój przylgnie do podniebienia twego, i będziesz niemy, a nie będziesz im mężem strofującym, przeto, że są domem odpornym.
Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
27 Ale gdy z tobą mówić będę, otworzę usta twoje; tedy rzeczesz do nich: Tak mówi panujący Pan: Kto chce słuchać, niech słucha, a kto nie chce, niech nie słucha, gdyż domem odpornym są.
Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

< Ezechiela 3 >