< Ezechiela 27 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 A ty, synu człowieczy! podnieś nad Tyrem lament,
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 A rzecz do Tyru, który leży nad portami morskiemi i handluje z narodami na wielu wyspach: Tak mówi panujący Pan: O Tyrze! tyś mówił: Jam jest doskonały w piękności.
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 W pośrodku morza były granice twoje, budownicy twoi doskonałą uczynili piękność twoję.
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 Z jedliny z Sanir pobudowalić wszystkie piętra twoje, cedry z Libanu brali, aby czynili maszty twoje.
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 Z dębów Basańskich czynili wiosła twoje, ławy twoje urobili z kości słoniowych i z bukszpanu z wysep Cytymskich.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Bisior haftowany egipski bywał płótnem twojem, z któregoś żagle miewał; hijacynt i szarłat z wysep Elisa był nakryciem twojem.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 Obywatele Sydonu, i Arwadczycy bywali żeglarzami twymi; mędrcy twoi, Tyrze! którzy bywali w tobie, ci byli sternikami twymi.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 Starcy z Giebal, i mędrcy jego oprawiali w tobie rozpadliny twoje; wszystkie okręty morskie i żeglarze ich bywali w tobie, handlując z tobą.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 Persowie, i Ludczycy, i Putejczycy bywali w wojsku twojem, mężowie waleczni twoi; tarcz i przyłbicę zawieszali w tobie, ci przydawali tobie ozdoby.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 Synowie Arwad z wojskiem twojem na murach twoich w około, także Gamadczycy na wieżach twoich bywali, tarcze twoje zawieszali na murach twoich w około; cić są, którzy doskonałą uczynili piękność twoję.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 Zamorscy kupcy twoi dla wielkości wszelakich dostatków, srebrem, żelazem, cyną i ołowiem kupczyli na jarmarkach twoich.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 Jawan, Tubal, i Mesech, kupcy twoi, ludzi i naczynie miedziane dawali na zamianę tobie.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 Z domu Togorma końmi, i jezdnymi, i mułami kupczyli na jarmarkach twoich.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 Synowie Dedanowi, kupcy twoi, i wiele wysep przekupowali towary ręki twojej, rogi, kości słoniowe, i drzewo hebanowe dawali na zamianę za zapłatę twoję.
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 Syryjczycy kupcy twoi dla mnóstwa przemyślnych robót twoich, karbunkułami, szarłatem, i haftarskiemi rzeczami, płótnem subtelnem, i koralami, i kryształami handlowali na jarmarkach twoich.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 Juda i ziemia Izraelska, i ci kupcy twoi, pszenicę z Minnit i z Pannag, i miód, i oliwę. i kadzidło na zamianęć dawali.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 Damaszczanie, kupcy twoi dla mnóstwa przemyślnych robót twoich, i dla mnóstwa wszelkich dostatków, winem z Helbonu i wełnę białą kupczyli.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 Także Dan i Jawan, kramarze na jarmarkach twoich, sprzedawali żelazo polerowane, kassyję, i Tatarskie ziela na zamianęć dawali.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 Dedan kupczył w tobie suknami kosztownemi na wozy.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 Arabczycy, i wszyscy książęta Kedarscy, i ci kupczyli z tobą skopami i baranami, i kozłami, tem handlowali w tobie.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 Kupcy Sabejscy i z Ramy kupczyli z tobą wszelakiemi przedniejszemi wonnemi rzeczami, i wszelakim kamieniem drogim i złotem kupczyli na jarmarkach twoich;
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 Haran, i Kanne, i Eden kupcy z Saby; Assur i Kilmad kupczył w tobie.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 Ci kupcy twoi, sztukami hijacyntu, i rzeczami haftowanemi, i skrzyniami dla kosztownych szat, także towarami, które powrozami obwiązują albo w skrzyniach cedrowych zawierają, kupczyli w tobie.
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 Okręty morskie przodkowały w kupiectwie twojem; i byłoś napełnione i uwielbione bardzo w pośród morza.
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Na wody wielkie zaprowadzili cię żeglarze twoi; wiatr wschodni rozbije cię w pośród morza.
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Bogactwa twoje, i jarmarki twoje, kupiectwo twoje, żeglarze twoi, i sternicy twoi, i ci, którzy zaprawiali rozpadliny twoje, i kupcy towarów twoich, i wszyscy mężowie waleczni twoi, którzy byli w tobie, i wszystko mnóstwo twoje, które jest w pośród ciebie, wpadną w pośród morza w dzień upadku twego.
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 Na głos krzyku sterników twoich zadrżą wały morskie;
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 I wystąpią z okrętów swoich wszyscy robiący wiosłem, żeglarze, i wszyscy sternicy morscy na ziemi staną.
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 I będą narzekali nad tobą głosem wielkim, i będą gorzko wołali, a sypiąc proch na głowy swoje, w popiele się walać będą.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 Nadto poczynią sobie dla ciebie łysiny, a opaszą się worami; i będą płakać nad tobą w gorzkości duszy swej płaczem gorzkim.
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Uczynią, mówię, nad tobą lament żałośny, a będą narzekali nad tobą, mówiąc: Któreż miasto podobne jest Tyrowi, wyciętemu w pośrodku morza?
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 Gdy wychodziły towary twoje z morza, nasycałoś wiele narodów; mnóstwem bogactw twoich i handlów twoich bogaciłoś królów ziemskich.
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 Ale gdy będziesz podruzgotane od morza w głębokościach wód, kupiectwo twoje i wszystko mnóstwo twoje w pośrodku ciebie upadnie.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 Wszyscy na wyspach mieszkający zdumieją się nad tobą, a królowie ich strachem zdjęci będąc, bardzo się zatrwożą.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 Kupcy między narodami zaświsną nad tobą; na postrach im będziesz, a nie będzie cię na wieki.
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

< Ezechiela 27 >