< Ezechiela 26 >

1 I stało się roku jedenastego, pierwszego dnia miesiąca, stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Synu człowieczy! przeto, iż Tyr mówił o Jeruzalemie wykrzykając: Hej, hej! zniszczone jest miasto bram bardzo ludnych, obraca się do mnie, teraz napełniony będę, gdyż to jest spustoszone;
“Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
3 Dlatego tak mówi panujący Pan: Otom Ja powstał przeciwko tobie, o Tyrze! a przywiodę na cię wiele narodów, jakobym przywiódł morze z nawałnościami jego;
Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
4 I zburzą mury Tyrskie, i rozwalą wieże jego; i wymiotę z niego proch jego, i uczynię go wierzchołkiem skały gładkiej,
Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
5 Tak, że będą wysuszać sieci w pośród morza; bom Ja rzekł, mówi panujący Pan, przeto będzie na rozchwycenie narodom.
Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
6 A córki jego, które będą na polu, mieczem pobite będą, a dowiedzą się, żem Ja Pan.
Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
7 Bo tak mówi panujący Pan: Oto Ja przywiodę przeciwko Tyrowi Nabuchodonozora, króla Babilońskiego, od północy, króla nad królmi, z końmi i z wozami, i z jezdnymi i z zgrają, i z ludem wielkim.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
8 Córki twoje na polu mieczem pomorduje, i przeciwko tobie porobi baszty, i usypie wał przeciwko tobie, i postawi przeciwko tobie tarcz;
Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
9 I tarany zasadzi przeciwko murom twoim, a wieże twoje potłucze młotami swemi.
Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
10 Od mnóstwa koni jego okryje cię proch ich; od grzmotu jezdnych i kar i wozów poruszą się mury twoje, gdy wchodzić będzie w bramy twoje, jako wchodzą do miasta zburzonego.
Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
11 Kopytami koni swoich zdepcze wszystkie ulice twoje, lud twój mieczem pobije, a mocne słupy twoje upadną na ziemię;
Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
12 I robiorą majętność twoję, a rozchwycą towary twoje, i rozwalą mury twoje, i domy twoje rozkoszne poburzą, a kamienie twoje, i drzewo twoje, i proch twój do wody wrzucą.
Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
13 I uczynię. że ustanie głos pieśni twoich, a dźwięk harf twoich nie będzie więcej słyszany.
Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
14 I uczynię cię wierzchołkiem gładkiej skały; staniesz się miejscem ku wysuszaniu sieci, nie będziesz więcj zbudowany; bom Ja Pan powiedział, mówi panujący Pan.
Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
15 Tak mówi panujący Pan do Tyru: Izali się od trzasku upadku twego, gdy ranni wołać będą, gdy okrutne morderstwo będzie w pośrodku ciebie, wyspy się nie poruszą?
“Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
16 I powstaną z stolic swoich wszyscy książęta pomorscy, i złożą z siebie płaszcze swoje, a szaty swe haftowane zewleką, strachem będą przyodziani, na ziemi usiądą, a wzdrygając się co chwila zdumiewać się będą nad tobą,
Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
17 I podniosą nad tobą lament i rzekną do ciebie: Jakoś zginęło, o miasto! w którem mieszkano dla przyległości morza, miasto sławne, które było mocne na morzu, ono i z obywatelami swymi, którzy byli straszni wszystkim obywatelom jego.
Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
18 Tedy się zatrwożą wyspy w dzień upadku twego; zatrwożą się mówię wyspy morskie nad zginieniem twojem.
Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
19 Bo tak mówi panujący Pan: Gdy cię uczynię miastem spustoszonem, jako miasta, w których nie mieszkają, gdy na cię przepaść przywiodę, tak, że cię wody wielkie przykryją;
“Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
20 Gdy uczynię, że zstąpisz z tymi, którzy zstępują do dołu, do ludu dawnego, a położę cię w najniższych stronach ziemi, na pustyniach dawnych, z tymi, co zstępują do dołu, aby nie mieszkano w tobie, tedy dokażę sławy w ziemi żyjących.
Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
21 Bo uczynię to, że będziesz na wielki postrach, gdy cię nie stanie; a choćby cię szukano, nie znajdą cię na wieki, mówi panujący Pan.
Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”

< Ezechiela 26 >