< Ezechiela 25 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Synu człowieczy! obróć twarz twoję przeciwko synom Ammonowym, a prorokuj przeciwko nim.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
3 I rzecz synom Ammonowym: Słuchajcie słowa panującego Pana. Tak mówi panujący Pan: Przeto, żeś wykrzykał mówiąc: Hej, hej! nad świątnicą moją, gdy była splugawiona, i nad ziemią Izraelską, i gdy była spustoszona, i nad domem Judzkim, i gdy szedł w niewolę;
Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
4 Przetoż oto Ja cię też podam narodom wschodnim w dziedzictwo i pobudują pałace swoje w tobie, a wystawią mieszkanie swoje w tobie, one będą jeść urodzaje twoje, oni też będą pić mleko twoje.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
5 I dam Rabbę na mieszkanie wielbłądom, a miasta synów Ammonowych na legowisko trzodom; i dowiecie się, żem Ja Pan.
Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 Bo tak mówi panujacy Pan: Przeto, iżeś klaskał ręką, a tąpał nogą, i weseliłeś się z serca, żeś cale spustoszył ziemię Izraelską:
Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
7 Przetoż oto Ja wyciągnę rękę swą przeciwko tobie, a dam cię w rozchwycenie narodom, i wytnę cię z narodów, a wytracę cię z ziem, i wygładzę cię, a dowiesz się, żem Ja Pan.
Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
8 Tak mówi panujący Pan: Dlatego, że Moab i Seir mówił: Oto dom Judzki podobny jest wszystkim innym narodom.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
9 Dlatego oto Ja otworzę stronę Moabczyków od miast, od miast mówię ich, i od granic ich, ozdobę ziemi Betiesymot, Baalmeon, i Karyjataim,
Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
10 Narodom wschodnim z ziemią synów Ammonowych; bom ją dał w dziedzictwo, aby nie było pamiątki synów Ammonowych między narodami.
Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
11 A tak nad Moabem sądy wykonam, iż poznają, żem Ja Pan.
Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
12 Tak mówi panujący Pan: Przetoż, iż się Edomczycy srodze mścili nad domem Judzkim, i przywiedli na się winę wielką, mszcząc się nad nimi;
“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
13 Przetoż tak mówi panujący Pan: Wyciągnę też rękę moję na ziemię Edomczyków, a wytrcę z niej ludzi i bydło, i uczynię ją pustynią; od Teman aż do Dedan od miecza polegną.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
14 A tak wykonam pomstę moję nad Edomczykami przez ręce ludu mojego Izraelskiego, a obejdą się z Edomczykami według popędliwości mojej, i według gniewu mego; i poznają pomstę moję, mówi panujacy Pan.
Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
15 Tak mówi panujący Pan: Przeto, iż się Filistyńczycy mścili, i pomstę wykonywali, pustosząc ich z serca, a do zginienia przywodząc z nieprzyjaźni starodawnej;
“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
16 Dlatego tak mówi panujący Pan: Oto Ja wyciągnę rękę moję na Filistyńczyków, i wykorzenię Cheretejczyków, i wytracę ostatek krainy pomorskiej.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
17 A tak uczynię nad nimi pomsty wielkie, karząc ich w zapalczywości; i dowiedzą się, żem Ja Pan, gdy wykonam pomstę moję nad nimi.
Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezechiela 25 >