< Ezechiela 23 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Synu człowieczy! były dwie niewiasty, córki jednej matki;
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 Te nierząd płodziły w Egipcie, w młodości swojej nierząd płodziły; tam są omacane piersi ich, i tam są zgniecione piersi panieństwa ich.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Imiona ich te są: Większej Ahola, a siostry jej Aholiba. Teć były moje, i zrodziły synów i córki; imiona, mówię, ich są, Samaryja Ahola, a Jeruzalem Aholiba.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Ale Ahola płodziła wszeteczeństwo przy mnie, a nierządu pilnowała z miłośnikami swojemi, z Assyryjkczykami bliskimi,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 Którzy byli obleczeni w hijacynt, z książętami, i panami, i ze wszystkimi młodzieńcami udatnymi, i z jezdnymi jeżdżącymi na koniach;
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 Udała się, mówię, na wszeteczeństwo swoje z nimi, ze wszystkimi najprzedniejszymi synami Assyryjskimi, i ze wszystkimi, za którymi miłością pałała, a splugawiała się wszystkiemi plugawemi bałwanami ich.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 A tak wszeteczeństw swoich egipskich nie zaniechała: bo z nią sypiali w młodości jej, a oni omacali piersi panieństwa jej, i wylali wszeteczeństwo swe na nią.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 Dlatego podałem ją w rękę zalotników jej, w rękę synów Assyryjskich, za którymi miłością pałała.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Oni odkryli nagość jej, synów jej i córki jej zabrali, a samę mieczem zabili; i stała się osławioną między niewiastami, gdy sądy wykonali przy niej.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 To widząc siostra jej Aholiba, bardziej się niż ona zapaliła miłością, a wszeteczeństwo jej większe było niżeli siostry jej.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 Za synami Assyryjskimi pałała miłością, za książętami, i panami bliskimi, ubranymi w szaty kosztowne, za jezdnymi jeżdżącymi na koniach, i za wszystkimi młodzieńcami urodziwymi.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 I widziałem, że się splugawiła, a iż jednaka droga obu była.
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 Ale ta jeszcze to przydała do wszeteczeństw swoich, że widząc mężów wymalowanych na ścianie, obrazy Chaldejczyków malowane farbami,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 Opasane pasami na biodrach ich, i kołpaki farbowane na gowach ich, a że wszyscy na wejrzeniu byli jako hetmani, podobni synom Babilońskim, w ziemi Chaldejskiej zrodzonym;
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 I pałała miłością ku nim, ujrzawszy ich oczyma swemi, a wyprawiła posłów do nich do ziemi Chaldejskiej.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 Tedy weszli do niej synowie Babilońscy do komory nierządu, i zmazali ją wszeteczeństwem swojem; a gdy się splugawiła z nimi, odstąpiła dusza jej od nich.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 I gdy odkryła wszeteczeństwa swe, odkryła i nagość swoję; odstąpiła dusza moja od niej, jako była odstąpiła dusza moja od siostry jej.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 Bo rozmnożyła wszeteczeństwa swoje, wspominając na dni młodości swojej, których nierządu patrzyła w ziemi Egipskiej.
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 I pałała miłością przeciwko nierządnikom ich, których ciała są jako ciała osłów, a przyrodzenie ich jako przyrodzenie końskie.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 A takeś się zaś nawróciła do sprośności młodości twojej, gdy macali Egipczanie piersi twoje dla piersi młodości twojej.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 Przetoż, o Aholibo! tak mówi panujący Pan: Oto ja pobudzę zalotników twoich przeciwko tobie, tych, od których odstąpiła dusza twoja, i przywiodę ich na cię zewsząd;
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 Synów Babilońskich, i wszystkich Chaldejczyków z Pekot, i z Soby, i z Kohy, i wszystkich synów Assyryjskich z nimi, młodzieńców udatnych, książąt i panów wszystkich, hetmanów i ludzi zacnych, wszystkich jeżdżących na koniach;
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 I przyjadą przeciwko tobie na wozach żelaznych, i na rydwanach, i na karach, a to z zgrają narodów, z tarczami, i z pancerzami, i z przyłbicami, położą się przeciwko tobie zewsząd; i dam im prawo, aby cię sądzili według praw swoich.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 I wyleję gorliwość moję na cię, i obejdą się z tobą zapalczywie, nos twój i uszy twoje oberżną, a ostatek twój od miecza polegnie; oni synów twoich i córki twoje pojmają, a ostatek twój ogniem pożarty będzie;
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 I zewloką cię z szat twoich, a pobiorą strój ozdoby twojej.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 A tak uczynię koniec sprośności twojej przy tobie, i wszeteczeństwu twemu, któreś przyniosła z ziemi Egipskiej, a nie podniesiesz oczów twych do nich, ani na Egipt nie wspomnisz więcej.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 Bo tak mówi panujący Pan: Oto cię Ja podaję w ręce tych, których masz w nienawiści, w ręce tych, od których odstąpiła dusza twoja;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 I obejdą się z tobą według nienawiści, i zabiorą wszystkę pracę twoję, a zostawią cię nagą i obnażoną, i będzie jawna nagość wszeteczeństw twoich, i sprośności twojej, i nierządów twoich.
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 Toć się stanie przeto, żeś nierząd płodziła naśladując pogan, przeto, żeś się zmazała plugawemi bałwanami ich;
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Chodziłaś drogą siostry swej, dlatego dam kubek jej w rękę twoję.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Tak mówi panujący Pan: Kubek siostry twojej głęboki i szeroki pić będziesz, spory będzie; pośmiech także i igrzysko będą mieli z ciebie.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Pijaństwem i boleścią napełniona będziesz, kubkiem spustoszenia i smutku, kubkiem siostry swej Samaryi!
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 I wypijesz go i wysączysz, potem go pokruszysz, a piersi swe poobrywasz; bom Ja rzekł, mówi panujący Pan.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 Dlatego tak mówi panujący Pan: Ponieważeś zapomniała na mię, a zarzuciłaś mię za tył swój, i ty też ponoś niecnotę, swoję, i wszeteczeństwa swoje.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 I rzekł Pan do mnie: Synu człowieczy! izali się będziesz zastawiał za Aholę albo za Aholibę? Oznajmij im raczej obrzydliwości ich:
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 Że cudzołożyły, a krew jest na rękach ich, i z plugawemi bałwanami swemi cudzołożyły; nadto i synów swych, których mi narodziły, przez ogień przeporowadzały im na pożarcie.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Więc i to mi uczyniły, że świątnicę moję splugawiły dnia onego, a sabaty moje pogwałciły.
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 Bo gdy ofiarowały synów swych plugawym bałwanom swoich, wchodziły do świątnicy mojej onegoż dnia, aby ją zmazały; oto takci czyniły w pośrodku domu mego.
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Nadto posyłały też do mężów, aby przyszli z daleka; którzy zaraz przychodzili, kiedy poseł do nich wysłany był. Tymeś kwoli się ty umywała, farbowałaś twarz swoję, i zdobiłaś się ochędóstwem swojem.
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 Siadałaś na łożu zacnem, przed którym był stół przygotowany, na któremeś i kadzeniw moje i olejek mój pokładała.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 A gdy głos onego mnóstwa ucichł, tedy i do mężów ludu pospolitego posyłały, których przywodzono ożartych z puszczy, i kładli manele na ręce ich, i korony ozdobne ne ręce ich.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 A chociażem przymawiał onej cudzołożnicy zastarzałej, a iż oni raz z jedną, raz z drugą nierząd płodzą,
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 I że każdy z nich wchodzi do niej, jako wchodzą do niewiasty wszetecznej: przecie jednak wchodzili do Aholi i do Aholiby, niewiast niecnotliwych.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Przetoż sprawiedliwi mężowie, ci je osądzą sądem cudzołożnic, i sądem wylewających krew, przeto, że cudzołożyły, a krew jest na rękach ich.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 Bo tak mówi panujący Pan: Przywiodę na nie wojsko, a poddam je na potłukanie i na łup;
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 I ukamionuje je ono zgromadzenie kamieniem, i rozsieką je mieczami swemi, synów ich i córki ich pobiją, a domy ich ogniem spalą.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 A tak uprzątnę sprośność z tej ziemi, i będą się tem karać wszystkie niewiasty, a nie uczynią według niecnoty waszej.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 Bo włożona będzie na was niecnota wasza, a grzechy plugawych bałwanów waszych poniesiecie, i poznacie, żem Ja panujący Pan.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

< Ezechiela 23 >