< Ezechiela 12 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie mówiąc:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Synu człowieczy! ty w pośrodku domu odpornego mieszkasz, którzy mają oczy, aby widzieli, a nie widzą, uszy mają, aby słyszeli, a nie słyszą; przeto, że domem odpornym są.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Ty tedy, synu człowieczy! spraw sobie sprzęt przeprowadzenia, a przeprowadzaj się we dnie przed oczyma ich, a przeprowadzaj się z miejsca swego na miejsce inne przed oczyma ich, aza wżdy obaczą, acz domem odpornym są.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 I wyniesiesz sprzęt swój, jako sprzęt przeprowadzenia, we dnie przed oczyma ich; a sam wynijdź w wieczór przed oczyma ich, jako wychodzą, którzy się przeprowadzają.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 Przed oczyma ich przekop sobie mur, a wynieś przezeń sprzęt twój.
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 Przed oczyma ich na ramionach nieś, z zmierzkiem wynieś, twarz swoję zakryj, a nie patrz na ziemię; bom cię dał za dziw domowi Izraelskiemu.
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 I uczyniłem tak, jako mi rozkazano; sprzęt mój wyniosłem jako sprzęt prowadzącego się we dnie, a w wieczór przekopałem sobie mur ręką; z zmierzkiem wyniosłem go na ramieniu niosąc przed oczyma ich.
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 Znowu stało się słowo Pańskie do mnie rano, mówiąc:
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 Synu człowieczy! Izali nie rzekł do ciebie dom Izraelski, dom ten odporny: Cóż to czynisz?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Rzeczże im, tak mówi panujący Pan: Na księcia, który jest w Jeruzalemie, ściąga się to brzemię, i na wszystek dom Izraelski, którzy są w pośród jego.
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 Rzeczże do nich: Jam jest dziwem waszym; jakom uczynił, tak się im stanie; przeprowadzą się, i w niewolę pójdą.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 A książę, który jest w pośrodku nich, na ramieniu poniesie sprzęt swój z zmierzkiem, i wynijdzie; mur przekopią, aby go wywiedli przezeń; twarz swoję zakryje, tak, że nie będzie widział ziemi okiem swojem.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 Bo rozciągnę nań sieć swoję, i pojmany będzie niewodem moim, i przywiodę go do Babilonu, do ziemi Chaldejskiej, a tej nie ogląda, i tam umrze.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 Także też wszystkich, którzy są około niego, pomoc jego, i wszystkie hufy jego rozproszę na wszystkie strony, i miecza dobędę za nimi;
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 I poznają, żem Ja Pan, gdy ich rozproszę między narody, i rozwieję ich po ziemiach.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 Jednak zostawię z nich trochę mężów po mieczu, po głodzie i po morze, aby opowiadali wszystkie obrzydliwości swe między narodami, do których wnijdą, i poznają, żem Ja Pan.
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 Znowu stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 Synu człowieczy! chleb swój z strachem jedz i wodę twoję ze drżeniem i z smutkiem pij,
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 A rzecz do ludu tej ziemi: Tak mówi panujący Pan o tych, którzy mieszkają w Jeruzalemie, o ziemi Izraelskiej: Chleb swój z smutkiem jeść, a wodę swą z trwogą pić będą, aby była ziemia jego złupiona z dostatków swoich dla bezprawia wszystkich mieszkających w niej;
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 Także miasta, w których mieszkają, spustoszone będą, i ziemia spustoszeje; i dowiecie się, żem Ja Pan.
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 Stało się zaś słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 Synu człowieczy! cóż to za przypowieść u was o ziemi Izraelskiej, iż mówicie: Przedłużąć się dni, a z tego widzenia nic nie będzie?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 Przetoż mów do nich: Tak mówi panujący Pan: Sprawię Ja to, iż ustanie ta przypowieść, a nie będą używać tej przypowieści więcej w Izraelu; powiedz im: I owszem, przybliżyły się te dni, i spełnienie wszelkiego widzenia.
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 Bo nie będzie więcej żadnego marnego widzenia, ani wieszczby pochlebcy w pośrodku domu Izraelskiego.
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 Przeto, że Ja Pan mówić będę, a którekolwiek słowo wyrzekę, stanie się; nie pójdzie w długą, ale za dni waszych, domie odporny! wyrzekę słowo, i wypełnię je, mówi panujący Pan.
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula nati:
27 Synu człowieczy! oto dom Izraelski mówią: To widzenie, które ten widzi, odwlecze się na wiele dni, a o dalekich czasach ten prorokuje;
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 Przeto im rzecz: Tak mówi panujący Pan: Nie pójdzieć w długą żadne słowo moje; ale słowo, które wyrzekę, stanie się, mówi panujący Pan.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”

< Ezechiela 12 >