< Ezechiela 10 >
1 I widziałem; a oto na rozpostarciu, które było nad głową Cherubinów, jakoby kamień szafirowy, na wejrzeniu jako podobieństwo stolicy, ukazało się nad nimi.
Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
2 Tedy rzekł do onego męża odzianego szatą lnianą, mówiąc: Wnijdź między koła pod Cherubinów, a napełń ręce swe węglem ognistym z pośród Cherubinów, i rozrzuć po mieście. I wszedł przed oczyma memi.
Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
3 (A Cherubowie stali po prawej stronie domu, gdy wchodził on mąż, a obłok napełnił sień wnętrzną.
Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
4 Bo gdy się była podniosła chwała Pańska z Cherubinów, ku progowi domu, tedy napełniony był dom obłokiem, a sień napełniona była jasnością chwały Pańskiej;
Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
5 A szum skrzydeł Cherubinów słyszany był aż do sieni zewnętrznej, jako głos Boga wszechmocnego, gdy mówi.)
Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
6 Gdy tedy rozkazał onemu mężowi odzianemu w szatę lnianą, mówiąc: Weźmij ognia z pośrodku kół, z pośrodku Cherubinów: wszedł i stanął podle kół.
Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
7 Tedy wyciągnął Cherubin jeden rękę swą w pośród Cherubinów do onego ognia, który był w pośrodku Cherubinów, a wziąwszy podał go w rękę onego odzianego szatą lnianą, który wziąwszy go wyszedł.
Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
8 Bo się ukazało na onych Cherubinach podobieństwo ręki człowieczej pod skrzydłami ich.
Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
9 Potemem wejrzał, a oto cztery koła podle Cherubinów, koło jedno podle jednego Cherubina, a tak każde koło podle każdego Cherubina, a podobieństwo kół jako barwa kanienia Tarsys;
Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
10 A na wejrzeniu miały jednakie podobieństwa one koła, jakoby było koło w pośrodku koła.
Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
11 Gdy chodziły, na cztery strony swoje chodziły; nie uchylały się, gdy szły, ale do onego miejsca, do którego się wódź obracał, za nim szły; nie uchylały się, gdy szły.
Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
12 A wszytko ciało ich, i grzbiety ich, i ręce ich, i skrzydła ich, także i koła pełne były oczów około onych samych czterech, i kół ich.
Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
13 A koła one nazwał okręgiem, gdziem ja słyszał.
Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
14 A każde zwierzę miało cztery twarze; twarz pierwsza była twarz Cherubinowa, druga twarz była twarz człowiecza, trzecia była twarz lwia, a czwarta była twarz orla.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
15 I podnieśli się Cherubinowie. Toć są one zwierzęta, którem widział nad rzeką Chebar.
Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
16 A gdy chodzili Cherubinowie, chodziły i koła podle nich; a gdy ponosili Cherubinowie skrzydła swoje, aby się wzbili od ziemi, nie odwracały się też koła od nich.
Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
17 Gdy oni stali, stały, a gdy się ponosili, podnosiły się też z nimi; bo duch zwierząt był w nich.
Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
18 I odeszła chwała Pańska od progu domu, i stanęła nad Cherubinami.
Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
19 Gdy podnieśli Cherubinowie skrzydła swoje, a wzbili się od ziemi przed oczyma mojemi odchodząc, a koła przeciwko nim, i stanęli w wejściu bramy domu Pańskiego wschodniej, tedy chwała Boga Izraelskiego z wierzchu nad nimi była.
Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
20 Toć są one zwierzęta, którem widział pod Bogiem Izraelskim nad rzeką Chebar; i poznałem, iż to byli Cherubinowie.
Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
21 Po cztery twarze miał każdy z nich, i po cztery skrzydła każdy z nich, a podobieństwo rąk ludzkich pod skrzydłami ich.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
22 A podobieństwo twarzy ich było jako twarzy, którem widział u rzeki Chebar; także i oblicze ich takież było, i oni sami; każdy z nich prosto ku swej stronie chodził.
Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.