< Wyjścia 8 >

1 I rzekł Pan do Mojżesza: Wnijdź do Faraona, a mów do niego: Tak mówi Pan: Wypuść lud mój, aby mi służył.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Ale jeźli ty nie będziesz chciał puścić, oto, Ja zarażę wszystkie granice twoje żabami.
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 I wyda rzeka żaby, które wylezą i wnijdą do domu twego, i do komory łoża twego, i na pościel twoję, i do domu sług twoich, i między lud twój, i do pieców twoich, i w dzieże twoje.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 Tak na cię, jako na lud twój, i na wszystkie sługi twoje polezą żaby.
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 Tedy rzekł Pan do Mojżesza: Rzecz do Aarona: Wyciągnij rękę twoję z laską twą na rzeki, na strugi, i na jeziora, a wywiedź żaby na ziemię Egipską.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 Tedy wyciągnął Aaron rękę swą na wody Egipskie, i wylazły żaby, które okryły ziemię Egipską.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 I uczynili także czarownicy czarami swemi, i wywiedli żaby na ziemię Egipską.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Zatem Farao wezwał Mojżesza i Aarona, mówiąc: Módlcie się Panu, aby oddalił żaby ode mnie, i od ludu mego; a wypuszczę lud, aby ofiarowali Panu.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 I rzekł Mojżesz do Faraona: Poczczę cię tem, a powiedz, kiedy się modlić mam za cię, i za sługi twoje, i za lud twój, aby wytracone były żaby od ciebie, i z domów twoich, a tylko w rzece zostały.
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 A on rzekł: Jutro. Tedy rzekł Mojżesz: Uczynię według słowa twego, abyś wiedział, że nie masz, jako Pan Bóg nasz.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 I odejdą żaby od ciebie, i od domów twoich, i od sług twoich, i od ludu twego, tylko w rzece zostaną.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Wyszedł tedy Mojżesz i Aaron od Faraona. I zawołał Mojżesz do Pana, aby odjął żaby, które był przepuścił na Faraona.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 I uczynił Pan według słowa Mojżeszowego, że wyzdychały żaby z domów, ze wsi, i z pól.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 I zgromadzali je na kupy, i zśmierdła się ziemia.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 A widząc Farao, że miał wytchnienie, obciążył serce swoje, i nie usłuchał ich, jako był powiedział Pan.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 I rzekł Pan do Mojżesza: Mów do Aarona: Wyciągnij laskę twoję, a uderz w proch ziemi, aby się obrócił we wszy po wszystkiej ziemi Egipskiej.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 I uczynili tak; bo wyciągnął Aaron rękę swoję z laską swoją, i uderzył w proch ziemi; i były wszy na ludziach, i na bydle; wszystek proch ziemi obrócił się we wszy po wszystkiej ziemi Egipskiej.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 Czynili też także czarownicy, przez czary swoje, aby wywiedli wszy, ale nie mogli; i były wszy na ludziach i na bydle.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Tedy rzekli czarownicy do Faraona: Palec to Boży jest. I zatwardziało serce Faraonowe, i nie usłuchał ich, jako powiedział Pan.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 I rzekł Pan do Mojżesza: Wstań rano, a stań przed Faraonem, (oto, wynijdzie do wody, ) i rzeczesz do niego: Tak mówi Pan: Wypuść lud mój, aby mi służył;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Bo jeźli ty nie wypuścisz ludu mego, oto, Ja posyłam na cię, i na sługi twe, i na lud twój, i na domy twoje rozmaite robactwo; a będą napełnione domy Egipskie rozmaitem robactwem, nadto i ziemia, na której oni są.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 A oddzielę dnia onego ziemię Gosen, w której lud mój mieszka, aby tam nie było rozmaitego robactwa, abyś poznał, żem Ja Pan w pośrodku ziemi.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 I położę znak odkupienia między ludem moim i między ludem twoim; jutro będzie znak ten.
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 Tedy uczynił tak Pan. I przyszło rozmaite robactwo ciężkie na dom Faraonów, i na dom sług jego, i na wszystkę ziemię Egipską; i psowała się ziemia od rozmaitego robactwa.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Zatem wezwał Farao Mojżesza i Aarona, i rzekł: Idźcie, ofiarujcie Bogu waszemu w tej ziemi.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 I odpowiedział Mojżesz: Nie godzi się tak czynić; bo byśmy obrzydliwość Egipską ofiarowali Panu Bogu naszemu; a gdybyśmy ofiarowali obrzydliwość Egipską przed oczyma ich, zażby nas nie ukamionowali?
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 Drogę trzech dni pójdziemy na puszczą, i ofiarować będziemy Panu Bogu naszemu, jako nam rozkaże.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 I rzekł Farao: Jać wypuszczę was, abyście ofiarowali Panu Bogu waszemu na puszczy, wszakże daleko nie odchodźcie, i módlcie się za mną.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 I odpowiedział Mojżesz: Ja wychodzę od ciebie, i będę się modlił Panu, a odejdzie rozmaite robactwo od Faraona, od sług jego, i od ludu jego jutro; tylko niech więcej Farao nie kłamie, aby nie miał wypuścić ludu dla ofiarowania Panu.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 Wyszedłszy tedy Mojżesz od Faraona, modlił się Panu.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 I uczynił Pan według słowa Mojżeszowego, i oddalił ono rozmaite robactwo od Faraona, i od sług jego, i od ludu jego, a nie zostało i jednego.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Jednak Farao obciążył serce swe i tym razem, a nie wypuścił ludu.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

< Wyjścia 8 >