< Wyjścia 36 >

1 Tedy robił Besaleel, i Acholijab, i każdy mąż dowcipny, którym dał Bóg mądrość i rozum, aby umieli urobić każdą robotę ku usłudze świątnicy, wszystko, co rozkazał Pan.
Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”
2 I wezwał Mojżesz Besaleela, i Acholijaba, i każdego męża dowcipnego, któremu dał Pan mądrość w serce jego; każdego też, którego pobudziło serce jego, aby przystąpił do czynienia tej roboty.
Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito.
3 I wzięli od Mojżesza wszystkie podarki, które byli przynieśli synowie Izraelscy na robotę ku usłudze świątnicy, aby ją wykonali; ale oni przynaszali do niego jeszcze dobrowolne dary na każdy poranek.
Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse.
4 Tedy się zeszli wszyscy dowcipni, którzy robili wszelaką robotę świątnicy, każdy opuściwszy robotę swoję, którą czynili.
Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo
5 I rzekli do Mojżesza, mówiąc: Daleko więcej lud przynosi, niż potrzeba do wyrobienia tej usługi, którą rozkazał Pan uczynić.
ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”
6 Rozkazał tedy Mojżesz, aby obwołano w obozie mówiąc: Ani mąż, ani niewiasta niech więcej ni przynoszą ofiar na robienie świątnicy. I zabroniono ludowi, aby nie nosili.
Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri,
7 Bo mieli potrzeb dostatek do wszystkiej roboty, aby ją wyrobili, i zbywało.
chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.
8 I urobili każdy dowcipny z rzemieślników tę robotę: przybytek z dziesięciu opon z białego jedwabiu kręconego, i z hijacyntu, i szarłatu i z karmazynu dwa kroć farbowanego; z Cherubiny, robotą misterną robili je.
Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi.
9 Długość opony jednej dwadzieścia i osiem łokci, a szerokość opony jednej na cztery łokcie; pod jedną miarą były wszystkie opony.
Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
10 I spoił pięć opon jednę z drugą, także drugie pięć opon spoił jednę z drugą.
Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
11 Naczynił też pętlic hijacyntowych po kraju opony jednej, na końcu, gdzie się spinać mają; także uczynił po kraju opony drugiej, na końcu, gdzie się spinać mają.
Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
12 Pięćdziesiąt pętlic uczynił na oponie jednej, a pięćdziesiąt pętlic uczynił po kraju opony, któremi spojona była do drugiej; pętlica jedna przeciw drugiej była.
Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
13 Uczynił też pięćdziesiąt haczyków złotych, a spiął opony jednę ku drugiej haczykami; i tak uczyniony jest przybytek jeden.
Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.
14 Urobił też opony z sierści koziej na namiot ku zakrywaniu przybytku z wierzchu, jedenaście opon urobił.
Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi.
15 Długość opony jednej trzydzieści łokci, a cztery łokcie szerokość opony jednej; jednaż miara była tych jedenaście opon.
Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri.
16 I spoił pięć opon osobno, a sześć opon osobno.
Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso.
17 Uczynił też pętlic pięćdziesiąt po kraju jednej opony na końcu, gdzie się ma spinać; i pięćdziesiąt pętlic uczynił po kraju opony drugiej ku spinaniu.
Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
18 Uczynił też haczyków miedzianych pięćdziesiąt, do spięcia namiotu, aby był jeden.
Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
19 Nad to uczynił przykrycie na namiot z skór baranich czerwono farbowanych, i przykrycie z skór borsukowych na wierzch.
Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
20 Naczynił też desek do przybytku z drzewa sytym stojących.
Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
21 Dziesięć łokci długość deski, a półtora łokcia szerokość deski jednej.
Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69.
22 Dwa czopy miała deska jedna, sporządzone jeden przeciwko drugiemu; tak uczynił u wszystkich desek przybytku.
Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
23 Zgotował też i deski do przybytku, dwadzieścia desek ku stronie południowej, ku wiatrowi południowemu.
Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho,
24 I czterdzieści podstawków urobił ze srebra pod dwadzieścia desek: dwa podstawki pod deskę jednę do dwóch czopów jej, także dwa podstawki pod deskę drugą do dwu czopów jej.
ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
25 Także na drugiej stronie przybytku ku stronie północnej, uczynił dwadzieścia desek.
Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho,
26 I czterdzieści podstawków ich srebrnych: dwa podstawki pod deskę jednę, i dwa podstawki pod deskę drugą.
ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
27 Lecz na stronie przybytku ku zachodowi, uczynił sześć desek.
Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo,
28 Dwie deski uczynił na węgłach po obu stronach przybytku;
ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
29 A były spojone od spodku, także spojone były od wierzchu do jednegoż kolca; tak uczynił po obu stronach na dwu węgłach.
Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana.
30 A tak było osiem desek, i podstawków ich srebrnych szesnaście podstawków, po dwu podstawkach pod każdą deską.
Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.
31 Naczynił i drągów z drzewa sytym; pięć do desek przybytku na jednę stronę;
Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
32 Pięć także drągów do desek przybytku na drugą stronę, pięć też drągów do desek przybytku do obu węgłów, na zachód.
mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
33 A uczynił też drąg pośredni, aby przechodził przez pośrodek desek od końca do końca.
Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
34 A deski one powlókł złotem, i kolce do nich porobił ze złota, aby w nich drągi były, i powlókł drągi złotem.
Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.
35 Uczynił zaś zasłonę z hijacyntu, i z szarłatu, i z karmazynu dwa kroć farbowanego, i z białego jedwabiu kręconego; robotą misterną uczynił to z Cherubiny.
Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi.
36 A do niej nagotował cztery słupy z drzewa sytym, i powlókł je złotem, haki też ich były złote, i ulał do nich cztery podstawki srebrne.
Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi.
37 Uczynił też zasłonę do drzwi namiotu z hijacyntu, i z szarłatu, i z karmazynu dwa kroć farbowanego, i z białego jedwabiu kręconego, robotą haftarską.
Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
38 A słupów do niej pięć z haczykami ich; i powlókł wierzchy ich i przepasania ich złotem, a podstawków ich było pięć miedzianych.
Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.

< Wyjścia 36 >