< Wyjścia 35 >

1 Potem zebrał Mojżesz wszystko zgromadzenie synów Izraelskich, i mówił do nich: Te są rzeczy, które rozkazał Pan, abyście je czynili.
Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
2 Przez sześć dni odprawowana będzie robota; ale dzień siódmy będzie wam święty, sabbat odpocznienia Pańskiego; kto by weń robił robotę, umrze.
Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
3 Nie rozniecicie ognia we wszystkich mieszkaniach waszych w dzień sabbatu.
Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
4 Rzekł też Mojżesz do wszystkiego zgromadzenia synów Izraelskich, mówiąc: Tać jest rzecz, którą przykazał Pan mówiąc:
Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
5 Złóżcie od siebie podarek Panu: każdy, kto jest ochotnego serca, przyniesie ten podarek Panu, złoto, i srebro, i miedź.
Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
6 I hijacynt, i szarłat, i karmazyn dwa kroć farbowany, i biały jedwab, i sierść kozią;
nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
7 Skóry też baranie czerwono farbowane i skóry borsukowe, i drzewo sytym;
zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
8 I oliwę do świecenia, i rzeczy wonne na olejek pomazywania, i dla kadzenia wonnego;
mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
9 Kamienie też onychiny, i kamienie do osadzania naramiennika i napierśnika.
miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
10 A wszyscy dowcipnego serca między wami przyjdą, i robić będą, cokolwiek rozkazał Pan:
“Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
11 Przybytek, namiot jego, i przykrycie jego, haczyki jego, i deski jego, drągi jego, słupy jego, i podstawki jego;
Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
12 Skrzynie i drążki jej, ubłagalnią, i oponę do zasłony,
Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
13 Stół i drążki jego, ze wszystkiem naczyniem jego, i chleby pokładne;
tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
14 I świecznik do świecenia z naczyniem jego, i lampy jego, i oliwę do świecenia.
choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
15 Ołtarz także do kadzenia z drążkami jego, i olejek pomazywania, i kadzenia wonne, i zasłonę do drzwi przybytku;
guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
16 Ołtarz do całopalenia, i kratę jego miedzianą, drążki jego, i wszystkie naczynia jego, wannę z stolcem jej.
guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
17 Opony do sieni, słupy jej, i podstawki jej, i zasłony do drzwi u sieni.
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
18 Kołki do przybytku i kołki do sieni z sznurami jej.
zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
19 Szaty służebne do usługiwania w świątnicy, szaty święte Aaronowi kapłanowi, i szaty synom jego, dla sprawowania urzędu kapłańskiego
zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
20 Wyszło tedy wszystko zgromadzenie synów Izraelskich od obliczności Mojżeszowej.
Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
21 I przyszedł każdy mąż, którego pobudziło serce jego, i każdy, w którym dobrowolny był duch jego, przynieśli podarek Panu do robienia namiotu zgromadzenia, i do wszelkiej potrzeby jego, i na szaty święte.
ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
22 Przychodzili tedy mężowie z niewiastami, każdy, kto był ochotnego serca, przynosili zapony, i nausznice, i pierścienie, i manele, i wszelakie naczynia złote, i ktokolwiek przynosił ofiarę złotą Panu.
Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
23 Każdy też co miał hijacynt, i szarłat, i karmazyn dwa kroć farbowany, i biały jedwab, i sierść kozią, i skóry baranie czerwono farbowane, i skóry borsukowe, przynosili.
Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
24 Ktokolwiek ofiarował podarek srebra i miedzi, przynosili na ofiarę Panu, każdy też, co miał drzewo sytym, na wszelaką potrzebę ku usłudze przynosili.
Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
25 I wszystkie niewiasty dowcipnego serca rękami swemi przędły, a przynosiły co naprzędły, hijacynt, i szarłat, karmazyn dwa kroć farbowany, i biały jedwab.
Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
26 A wszystkie niewiasty których pobudziło serce ich umiejętne, przędły sierść kozią.
Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
27 Przełożeni zasię przynosili kamienie onychiny, i kamienie do osadzania naramiennika i napierśnika.
Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
28 Także rzeczy wonne i oliwę do świecenia, i na olejek pomazywania i na wonne kadzenia.
Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
29 Każdy mąż i niewiasta, w których ochotne serce było do ofiarowania, na każdą robotę, którą rozkazał Pan czynić przez Mojżesza, przynosili synowie Izraelscy ofiarę dobrowolną Panu.
Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
30 Zatem rzekł Mojżesz do synów Izraelskich: Oto, wezwał Pan z imienia Besaleela, syna Urowego, syna Churowego, z pokolenia Judy,
Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
31 I napełnił go Duchem Bożym, mądrością, i umiejętnością wszelkiego rzemiosła;
ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
32 I ku dowcipnemu wymyślaniu, cokolwiek może być urobione ze złota, i z srebra, i z miedzi;
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
33 Do rzezania kamienia ku osadzeniu, i na wyrobienie drzewa, do czynienia wszelakiej roboty zmyślnej.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
34 Dał nadto do serca jego, aby uczyć mógł inszych, on, i Acholijab, syn Achysamechów z pokolenia Dan.
Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
35 Napełnił je mądrością serca, aby robili wszelakie rzemiosło ciesielskie, i haftarskie, i tkackie z hijacyntu, i z szarłatu, z karmazynu dwa kroć farbowanego, i z białego jedwabiu tkacką robotą, aby robili każdą robotę dowcipnie wymyślając.
Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.

< Wyjścia 35 >