< Wyjścia 32 >

1 A widząc lud, iż omieszkiwał Mojżesz zejść z góry, tedy zebrał się lud przeciw Aaronowi, i mówili do niego: Wstań, uczyń nam bogi, którzy by szli przed nami; bo Mojżeszowi, mężowi temu, który nas wywiódł z ziemi Egipskiej, nie wiemy co się stało.
Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
2 Tedy im rzekł Aaron: Odejmijcie nausznice złote, które są na uszach żon waszych, synów waszych, i córek waszych, a przynieście do mnie.
Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
3 I poodrywał wszystek lud nausznice złote, które były na uszach ich, a przynieśli do Aarona.
Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
4 Które gdy odebrał z ręku ich, wykształtował je rylcem i uczynił z nich cielca odlewanego. I rzekli: Ci są bogowie twoi, Izraelu, którzy cię wywiedli z ziemi Egipskiej.
Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
5 Co ujrzawszy Aaron, zbudował ołtarz przed nim; a wołając Aaron mówił: Święto Pańskie jutro będzie.
Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
6 A wstawszy bardzo rano nazajutrz, ofiarowali całopalenia, i przywiedli ofiary spokojne; i siadł lud, aby jadł i pił, i wstali grać.
Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
7 Tedy rzekł Pan do Mojżesza: Idź zstąp; bo się popsował lud twój, któryś wywiódł z ziemi Egipskiej.
Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
8 Ustąpili prędko z drogi, którąm im przykazał; uczynili sobie cielca odlewanego, i kłaniali się mu, i ofiarowali mu mówiąc: Ci są bogowie twoi, Izraelu, którzy cię wywiedli z ziemi Egipskiej.
Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
9 Rzekł zasię Pan do Mojżesza: Widziałem lud ten, a oto, jest lud twardego karku.
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
10 Przetoż teraz puść mię, że się rozpali popędliwość moja na nie i wygładzę je; a ciebie uczynię w naród wielki.
Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
11 I modlił się Mojżesz Panu Bogu swemu, a rzekł: Przeczże o Panie, rozpala się popędliwość twoja przeciwko ludowi twemu, któryś wywiódł z ziemi Egipskiej mocą wielką i ręką możną?
Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
12 A przeczżeby Egipczanie rzec mieli, mówiąc: Na ich złe wywiódł je, aby je pobił na górach, i aby je wygładził z wierzchu ziemi? Odwróć się od gniewu zapalczywości twojej, a ulituj się nad złem ludu twego.
Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
13 Wspomnij na Abrahama, Izaaka, i Izraela, sługi twoje, którymeś przysiągł sam przez się i mówiłeś do nich: Rozmnożę nasienie wasze jako gwiazdy niebieskie, i wszystkę tę ziemię, o którejm mówił. Dam ją nasieniu waszemu, i odziedziczą ją na wieki.
Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
14 I użalił się Pan nad złem, które mówił, że uczynić miał ludowi swemu.
Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
15 A obróciwszy się Mojżesz zstąpił z góry, dwie tablice świadectwa mając w ręku swych, tablice pisane po obu stronach; i na tej, i na owej stronie były pisane.
Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
16 A one tablice robotą Bożą były; pismo także pismo Boże było, wyryte na tablicach.
Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
17 A usłyszawszy Jozue głos ludu wołającego, rzekł do Mojżesza: Głos bitwy w obozie.
Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
18 Który odpowiedział: Nie jest to głos zwyciężających, ani głos porażonych: głos śpiewających ja słyszę.
Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
19 I stało się, gdy się przybliżył do obozu, że ujrzał cielca i tańce; a rozgniewawszy się bardzo Mojżesz, porzucił z ręku swoich tablice, i stłukł je pod górą.
Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
20 Wziął też cielca, którego byli uczynili, i spalił go w ogniu, i skruszył go aż na proch, a wysypawszy na wodę, dał pić synom Izraelskim.
Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
21 I rzekł Mojżesz do Aarona: Cóż ci ten lud uczynił, żeś wprowadził nań grzech wielki?
Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
22 Odpowiedział Aaron: Niech się nie rozpala gniew pana mego; ty znasz ten lud, jako do złego skłonny jest.
Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
23 Bo mi mówili: Uczyń nam bogi, którzy by szli przed nami, gdyż Mojżeszowi, mężowi temu, który nas wywiódł z ziemi Egipskiej, nie wiemy, co się stało.
Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
24 I odpowiedziałem im: Kto ma złoto, odrywajcie je z siebie. I dali mi, i wrzuciłem je w ogień, i ulał się ten cielec.
Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
25 Widząc tedy Mojżesz lud obnażony, (bo go był złupił Aaron na zelżenie przed nieprzyjaciołmi ich).
Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
26 Stanął Mojżesz w bramie obozu, i rzekł: Kto Pański, przystąp do mnie. I zebrali się do niego wszyscy synowie Lewiego.
Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
27 I rzekł do nich: Tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Przypasz każdy miecz swój do biodry swojej; przychodźcie a wracajcie się od bramy do bramy w obozie, a zabijajcie każdy brata swego, i każdy przyjaciela swego, i każdy bliźniego swego.
Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
28 I uczynili synowie Lewiego według słowa Mojżeszowego; i poległo z ludu dnia onego około trzech tysięcy mężów.
Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
29 Bo był rzekł Mojżesz: Poświęćcie ręce swoje dziś Panu, każdy na synu swym, i na bratu swym, aby wam dane było dziś błogosławieństwo.
Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
30 A gdy było nazajutrz, mówił Mojżesz do ludu: Wyście zgrzeszyli grzechem wielkim; przetoż teraz wstąpię do Pana, aza go ubłagam za grzech wasz.
Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
31 Wróciwszy się tedy Mojżesz do Pana, mówił: Proszę, zgrzeszył ten lud grzechem wielkim; bo sobie uczynili bogi złote.
Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
32 Teraz tedy, albo odpuść grzech ich, albo jeźli nie, wymaż mię proszę z ksiąg twoich, któreś napisał.
Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
33 I rzekł Pan do Mojżesza: Kto mi zgrzeszył, tego wymażę z ksiąg moich.
Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
34 A teraz idź, prowadź ten lud, gdziem ci rozkazał. Oto, Anioł mój pójdzie przed tobą; ale w dzień nawiedzenia mego nawiedzę też i na nich ten grzech ich.
Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
35 Skarał tedy Pan lud, przeto, że uczynili byli cielca, którego był uczynił Aaron.
Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.

< Wyjścia 32 >