< Wyjścia 11 >
1 I rzekł Pan do Mojżesza: Jeszcze jednę plagę przywiodę na Faraona, i na Egipt, potem wypuści was stąd; wypuści cale, owszem wypędzi was stąd.
Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
2 Mówże teraz do uszu ludu, aby wypożyczył każdy od bliźniego swego, i każda u sąsiadki swej naczynia srebrnego, i naczynia złotego.
Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
3 A dał Pan łaskę ludowi w oczach Egipczan, i był Mojżesz mąż bardzo wielki w ziemi Egipskiej, w oczach sług Faraonowych, i w oczach ludu.
Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
4 Tedy rzekł Mojżesz: Tak mówi Pan: O północy Ja pójdę przez pośrodek Egiptu.
Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
5 A umrze każde pierworodne w ziemi Egipskiej, od pierworodnego Faraonowego, który miał siedzieć na stolicy jego, aż do pierworodnego niewolnicy, która jest przy żarnach, i każde pierworodne z bydląt.
Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
6 A będzie krzyk wielki po wszystkiej ziemi Egipskiej, jaki przedtem nie był, i jaki potem nie będzie.
Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
7 Ale u wszystkich synów Izraelskich nie ruszy językiem swym, ani pies, ani człowiek, ani bydlę, abyście wiedzieli, że Pan uczynił rozdział między Egipczany i między Izraelem.
Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
8 I przyjdą ci wszyscy słudzy twoi do mnie, a kłaniać mi się będą, mówiąc: Wynijdź ty, i wszystek lud, który jest pod sprawą twoją; a potem wynijdę. I wyszedł od Faraona z wielkim gniewem.
Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
9 I rzekł Pan do Mojżesza: Nie usłucha was Farao, abym rozmnożył cuda moje w ziemi Egipskiej.
Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
10 Tedy Mojżesz i Aaron czynili te wszystkie cuda przed Faraonem; ale Pan zatwardził serce Faraonowe, i nie wypuścił synów Izraelskich z ziemi swojej.
Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.