< Estery 1 >

1 I stało się za dni Aswerusa, (który Aswerus królował od Indyi aż do Murzyńskiej ziemi, nad stem i dwudziestą i siedmią krain.)
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2 Że za onych dni, gdy siedział król Aswerus na stolicy królestwa swego, która była w Susan, mieście stołecznem,
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3 Roku trzeciego królowania swego sprawił u siebie ucztę na wszystkich książąt swoich, i sług swoich, na hetmanów z Persów i z Medów, na przełożonych i na starostów onych krain,
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
4 Pokazując bogactwa, i chwałę królestwa swego, i zacność a ozdobę wielmożności swojej przez wiele dni, mianowicie przez sto i ośmdziesiąt dni.
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
5 (A gdy się dokończyły dni one, uczynił król na wszystek lud, co go kolwiek było w Susan, w mieście stołecznem, od największego aż do najmniejszego, ucztę przez siedm dni na sali w ogrodzie przy pałacu królewskim.)
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
6 Opony białe, zielone i hijacyntowe zawieszono na sznurach bisiorowych i szarłatnych, na kolcach srebrnych i na słupach marmurowych; łoża złote i srebrne na tle kryształowem, i marmurowem, i paryjowem, i socharowem.
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
7 A napój dawano w naczyniu złotem, a to w naczyniu co raz innem, i wina królewskiego dostatkiem, jako przystało na króla.
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
8 Ale do picia, według ustawy, nikt nie przymuszał. Albowiem tak był rozkazał król wszystkim rządcom domu swego, aby czynili według woli każdego.
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
9 Wasty też królowa sprawiła ucztę na białegłowy w domu królewskim króla Aswerusa.
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
10 A dnia siódmego, gdy sobie król podweselił winem, rzekł do Mechumana, Bysyta, Herbona, Bygta, i Abagta, Zetara, i Charchasa, do siedmiu komorników, którzy służyli przed obliczem króla Aswerusa,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
11 Aby przywiedli Wasty królowę przed oblicze królewskie w koronie królewskiej, chcąc pokazać narodom i książętom piękność jej; bo bardzo piękna była.
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
12 Ale nie chciała królowa Wasty przyjść na rozkazanie królewskie, opowiedziane przez komorników. Przetoż rozgniewał się król bardzo, a gniew jego zapalił się w nim.
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
13 Tedy rzekł król do mędrców, rozumiejących czasy: (bo taki był zwyczaj przedkładać sprawy królewskie wszystkim biegłym w prawach i w sądach;
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14 A najbliższymi jego byli Charsena, Setar, Admata, Tarsys, Meres, Marsena, Memuchan, siedm książąt Perskich i Medskich, którzy patrzali na oblicze królewskie, i siadali na pierwszem miejscu w królestwie.)
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
15 Co czynić podług prawa z królową Wasty, przeto, iż nie uczyniła rozkazania króla Aswerusa, opowiedzianego przez komorników?
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
16 Tedy odpowiedział Memuchan przed królem i książętami: Nie przeciwko królowi samemu wystąpiła Wasty królowa, ale przeciwko wszystkim książętom, i przeciwko wszystkim narodom, którzy są po wszystkich krainach króla Aswerusa.
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
17 Albowiem gdy się ta sprawa królowej doniesie do wszystkich niewiast, znieważą sobie mężów swoich w oczach swoich, i rzeką: Król Aswerus rozkazał przywieść Wasty królowę przed oblicze swoje, a nie przyszła.
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
18 Owszem dzisiaj toż rzeką księżny Perskie i Medskie, (które słyszały postępek królowej) wszystkim książętom królewskim, a będzie dosyć wzgardy i waśni.
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
19 Przetoż, jeśli się za dobre widzi królowi, niech wynijdzie wyrok królewski od oblicza jego, a niech będzie wpisan między prawa Perskie i Medskie, których się przestępować nie godzi: Że nie chciała przyjść Wasty przed obliczność króla Aswerusa, przetoż królestwo jej da król innej, lepszej niż ona.
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
20 A gdy usłyszą ten wyrok królewski, który wydasz po wszystkiem królestwie swojem, jako wielkie jest, tedy wszystkie żony będą wyrządzały uczciwość małżonkom swoim od wielkiego aż do małego.
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
21 I podobała się ta rada królowi i książętom. I uczynił król według rady Memuchanowej;
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
22 A rozesłał listy do wszystkich krain królewskich, do każdej krainy pismem jej własnem, i do każdego narodu językiem jego, aby każdy mąż był panem w domu swoim. A to obwołano językiem każdego narodu.
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

< Estery 1 >