< Kaznodziei 7 >

1 Lepsze jest imię dobre, niżeli maść wyborna; a dzień śmierci, niż dzień narodzenia.
Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
2 Lepiej iść do domu żałoby, niż iść do domu biesiady, przeto, iż tam widzimy koniec każdego człowieka, a żyjący składa to do serca swego.
Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
3 Lepszy jest smutek, niżeli śmiech; bo przez smutek twarzy naprawia się serce.
Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
4 Serce mądrych w domu żałoby; ale serce głupich w domu wesela.
Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
5 Lepiej jest słuchać gromienia mądrego, niżeli słuchać pieśni głupich.
Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
6 Bo jaki jest trzask ciernia pod garncem, tak jest śmiech głupiego; i toć jest marność.
Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
7 Zaiste ucisk przywodzi mądrego do szaleństwa, a dar zaślepia serce.
Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
8 Lepsze jest dokończenie rzeczy, niżeli początek jej; lepszy jest człowiek cierpliwego ducha, niż ducha wyniosłego.
Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
9 Nie bądź porywczy w duchu twym do gniewu; bo gniew w zanadrzyu głupich odpoczywa.
Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
10 Nie mów: Cóż to jest, że dni pierwsze lepsze były, niż teraźniejsze? Bobyś się o tem nie mądrze pytał.
Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
11 Dobra jest mądrość przy majętności, i jest pożteczna tym, którzy widzą słońce.
Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Albowiem pod cieniem mądrości, i pod cieniem srebra odpoczywa człowiek, a wszakże przedniejsza jest umiejętność mądrości; bo przynosi żywot tym, którzy ją mają.
Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
13 Przypatrz się sprawie Bożej; bo któż może wyprostować, co on skrzywi?
Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
14 W dzień dobry zażywaj dobra, w dzień zły miej się na pieczy: boć ten uczynił Bóg przeciwko owemu, dlatego, aby nie doszedł człowiek tego, co nastanie po nim.
Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
15 Tom wszystko widział za dni marności mojej: Bywa sprawiedliwy, który ginie z sprawiedliwością swoją; także bywa niezbożnik, który długo żyje we złości swojej.
Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 Nie bądź nazbyt sprawiedliwym, ani nazbyt mądrym; przeczżebyś miał do zguby przychodzić?
Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
17 Nie bądź nader niepobożnym, ani nazbyt głupim; przeczżebyś miał umrzeć przed czasem swoim?
Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Dobra jest, abyś się owego trzymał, a tego się nie puszczał; kto się boi Boga, uchodzi tego wszystkiego.
Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
19 Mądrość umacnia mądrego więcej, niżeli dziesięć książąt, którzy są w mieście.
Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
20 Zaiste niemasz człowieka sprawiedliwego na ziemi, któryby czynił dobrze, a nie grzeszył.
Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
21 Nie do wszystkich też słów, które mówią ludzie przykładaj serca twego; i niech cię to nie obchodzi, choćciby i sługa twój złorzeczył.
Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 Boć wie serce twoje, żeś i ty częstokroć drugim złorzeczył.
pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
23 Wszystkiegom tego doświadczył mądrością, i rzekłem: Będę mądrym; aleć się mądrość oddaliła odemnie.
Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
24 A co dalekiego, i co bardzo głębokiego jest, któż to znajdzie?
Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
25 Wszystkom ja przeszedł myślą swoją, abym poznał i wybadał się, i wynalazł mądrość i rozum, a żebym poznał niezbożność, głupstwo, i błąd, i szaleństwo.
Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
26 I znalazłem rzecz gorzciejszą nad śmierć, to jest, taką niewiastę, której serce jest jako sieci i sidło, a ręce jej jako pęta. Kto się Bogu podoba, wolny będzie od niej; ale grzesznik będzie od niej pojmany.
Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
27 Otom to znalazł, (mówi kaznodzieja, ) stosując jedno z drugiem, abym doszedł umiejętności.
Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28 Czego zaś nad to szukała dusza moja, tedym nie znalazł. Męża jednego z tysiąca znalazłem; alem niewiasty między temi wszystkiemi nie znalazł.
pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 To tylko obacz, com znalazł, że stworzył Bóg człowieka dobrego; ale oni udali się za rozmaitemi myślami. Któż może z mądrym porównać? a kto może wyłożyć każdą rzecz?
Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”

< Kaznodziei 7 >