< Kaznodziei 6 >

1 Jest złe, którem widział pod słońcem, a jest ludziom zwyczajne.
Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri:
2 Gdy któremu człowiekowi Bóg dał bogactwa, i majętność, i sławę, tak że na niczem nie schodzi duszy jego, czegokolwiek żąda, jednak nie daje mu Bóg mocy pożywać tego: ale obcy człowiek pożera je. Toć jest marność i bieda ciężka.
Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.
3 Jeźli kto spłodził sto synów, a żyłby wiele lat, i przedłużyłyby się dni lat jego, a jeźliby dusza jego nie była nasycona dobrem, a nie miałby ani pogrzebu: powiadam, że lepszy jest martwy płód, niżeli on.
Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo.
4 Bo ten próżno przyszedłszy do ciemności odchodzi, a ciemnościami imię jego okryte bywa.
Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika.
5 Owszem, słońca nie widział, i nic nie poznaje; a tak odpocznienie lepsze ma, niżeli ów.
Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja,
6 A choćby też żył przez dwa tysiące lat, a dobregoby nie użył, azaż do jednego miejsca wszyscy nie idą?
ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?
7 Wszystka praca człowiecza jest dla gęby jego, a wszakże dusza jego nie może się nasycić.
Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake, komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.
8 Albowiem co ma więcej mądry nad głupiego? albo co ma więcej ubogi, który sobie umie poczynać między ludźmi?
Kodi munthu wanzeru amaposa motani chitsiru? Kodi munthu wosauka amapindula chiyani podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?
9 Lepiej jest co oczyma widzieć, niżeli tego żądać; aleć i to marność i utrapienie ducha.
Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
10 Czemkolwiek kto jest, już tak nazwano imię jego; i wiadomo było, że człowiekiem być miał, i że się nie może sądzić z mocniejszym nad się.
Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina, za mmene munthu alili nʼzodziwika; sangathe kutsutsana ndi munthu amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.
11 Ponieważ tedy wiele rzeczy jest, które rozmnażają marność, cóż z nich za pożytek ma człowiek?
Mawu akachuluka zopandapake zimachulukanso, nanga munthu zimamupindulira chiyani?
12 Albowiem któż wie, co jest dobrego człowiekowi w tym żywocie po wszystkie dni żywota marności jego, które jako cień pomijają? Albo kto oznajmi człowiekowi, co po nim będzie pod słońcem?
Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?

< Kaznodziei 6 >