< Kaznodziei 5 >
1 Strzeż nogi twojej, gdy idziesz do domu Bożego, a bądź skłonniejszym ku słuchaniu, niżeli ku dawaniu ofiar ludzi głupich; boć oni nie wiedzą, że źle czynią.
Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.
2 Nie bywaj porywczy do mówienia, ani serce twoje prędkie na wymówienie słowa przed obliczem Bożem, albowiem Bóg jest na niebie, a ty na ziemi; przeto niech słów twoich mało będzie.
Usamafulumire kuyankhula, usafulumire mu mtima mwako kunena chilichonse pamaso pa Mulungu. Mulungu ali kumwamba ndipo iwe uli pa dziko lapansi, choncho mawu ako akhale ochepa.
3 Bo jako sen przychodzi z wielkiej pracy, tak głos głupiego z wielu słów.
Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa, ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.
4 Gdy co Bogu poślubisz, nie omieszkiwaj tego oddać, boć mu się głupi nie podobają; cokolwiek poślubisz, oddaj.
Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako.
5 Lepiej jest nie ślubować, niżeli poślubiwszy co, nie oddać.
Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo.
6 Nie dopuszczaj ustom twoim, aby do grzechu przywodziły ciało twoje, ani mów przed aniołem, że to jest błąd. Przeczże masz Boga gniewać mową swą, któryby wniwecz obrócił sprawę rąk twoich?
Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako?
7 Bo gdzie jest wiele snów, tam i marności i słów wiele; ale się ty Boga bój.
Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.
8 Jeźli ucisk ubogiego, i zatrzymanie sądu i sprawiedliwości ujrzysz w której krainie, nie dziwuj się temu; bo wyższy wysokiego upatruje, a jeszcze wyżsi są nad nimi.
Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa.
9 Zabawa koło ziemi ma pierwsze miejsce u wszystkich; i król roli służy.
Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.
10 Kto miłuje pieniądze, nie nasyci się pieniędzy, a kto miłuje bogactwa, nie będzie miał pożytku. I toć jest marność.
Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo; aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza. Izinso ndi zopandapake.
11 Gdzie wiele majętności, wiele bywa tych, co ją jedzą. Cóż tedy za pożytek Panu z tego? jedno że na nie patrzy oczyma swemi.
Chuma chikachuluka akudya nawo chumacho amachulukanso. Nanga mwini wake amapindulapo chiyani kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?
12 Słodki jest sen pracowitemu, chociaż mało, chociaż wiele jadł; ale nasycenie bogatego spać mu nie dopuści.
Wantchito amagona tulo tabwino ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri, koma munthu wolemera, chuma sichimulola kuti agone.
13 Jest ciężka bieda, którąm widział pod słońcem; bogactwa zachowane na złe pana swego.
Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano: chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,
14 Bo takowe bogactwo złą sprawą giną, a syn, którego spłodzi, nie będzie miał nic w rękach swych.
kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka, kotero kuti pamene wabereka mwana alibe kanthu koti amusiyire.
15 Jako nagi wyszedł z żywota matki swojej, tak się wraca, jako był przyszedł, a nie odnosi nic z pracy swojej, coby miał wziąć w rękę swoję.
Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake, ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho. Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.
16 A tak i toć jest ciężka bieda, że jako przyszedł, tak odejdzie. Cóż tedy za pożytek, że na wiatr pracował?
Izinso ndi zoyipa kwambiri: munthu adzapita monga momwe anabwerera, ndipo iye amapindula chiyani, pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?
17 Dotego, że po wszystkie dni swoje w ciemności jadał z wielkim kłopotem, z boleścią i z gniewem.
Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima, kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.
18 Toć jest, com ja obaczył, że dobra i osobliwa rzecz jest, jeść i pić, i używać dobrego ze wszystkiej pracy swej, którą człowiek podejmuje pod słońcem po wszystkie dni żywota swego, które mu dał Bóg; albowiem to jest dział jego.
Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake.
19 A któremukolwiek człowiekowi dał Bóg majętność i bogactwo, i dał mu w moc, aby ich używał, i odbierał dział swój, a weselił się z pracy swojej: to jest dar Boży.
Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.
20 Bo nie będzie wiele pamiętał na dni żywota swego; przeto, że mu Bóg życzy wesela serca jego.
Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.