< Kaznodziei 2 >
1 Rzekłem ja do serca mego: Nuże teraz doświadczę cię w weselu, używajże dobrych rzeczy; ale i toć marność.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake.
2 Śmiechowi rzekłem: Szalejesz, a weselu: Cóż to czynisz?
“Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?”
3 Przemyślałem w sercu swem, abym pozwolił wina ciału memu, (serce jednak swoje sprawując mądrością) i abym się trzymał głupstwa dotąd, ażbym obaczył, coby lepszego było synom ludzkim czynić pod niebem, przez wszystkie dni żywota ich.
Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.
4 Wielkiem sprawy wykonał; pobudowałem sobie domy, nasadziłem sobie winnic;
Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa.
5 Naczyniłem sobie ogrodów, i sadów, i naszczepiłem w nich drzew wszelakiego owocu;
Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse.
6 Pobudowałem sobie stawy ku odwilżaniu przez nie lasu, w którym rośnie drzewo;
Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija.
7 Nabyłem sobie sług i dziewek, i miałem czeladź w domu moim; do tego i stada wołów, i wielkie trzody owiec miałem nad wszystkich, którzy byli przedemną w Jeruzalemie.
Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe.
8 Zgromadziłem też sobie srebro i złoto, i klejnoty od królów i krain. Sporządziłem też sobie śpiewaków i śpiewaczki, i inne rozkosze synów ludzkich, i muzyczne naczynia rozliczne.
Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu.
9 A tak stałem się wielkim i możniejszym nad wszystkich, którzy byli przede mną w Jeruzalemie; nadto mądrość moja zostawała przy mnie.
Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.
10 A wszystkiego, czego pożądały oczy moje, nie zabraniałem im, anim odmawiał sercu memu żadnego wesela; ale serce moje weseliło się ze wszystkiej pracy mojej. A toć był dział mój ze wszystkiej pracy mojej.
Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna; mtima wanga sindinawumane zokondweretsa. Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse, ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.
11 Lecz gdym się obejrzał na wszystkie sprawy swoje, które czyniły ręce moje, i na prace, którem podejmował pracując: oto wszystko marność, i utrapienie ducha, i niemasz nic pożytecznego pod słońcem.
Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga, ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze, zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe, palibe chomwe ndinapindula pansi pano.
12 Przetoż obróciłem się do tego, abym się przypatrywał mądrośći, i szaleństwu, i głupstwu; (bo cóżby człowiek czynił ten, który nastanie po królu? to, co już inni czynili.)
Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani, komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani. Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani choposa chimene chinachitidwa kale?
13 I obaczyłem, iż jest pożyteczniejsza mądrość niżeli głupstwo, tak jako jest pożyteczniejsza światłość, niżeli ciemność.
Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru, monga momwe kuwala kumapambanira mdima.
14 Mądry ma oczy w głowie swej, ale głupi w ciemnościach chodzi; a wszakżem poznał, że jednakie przygody na wszystkich przychdzą.
Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo, pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli; koma ndinazindikira kuti chomwe chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.
15 Dlategom rzekł w sercu mojem: Mali mi się tak dziać, jako się głupiemu dzieje, przeczżem go ja tedy mądrośćią przeszedł? Przetożem rzekł w sercu mojem: I toć jest marność.
Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga, “Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine. Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?” Ndinati mu mtima mwanga, “Ichinso ndi chopandapake.”
16 Albowiem nie na wieki będzie pamiątki mądrego i głupiego, dlatego, iż to, co teraz jest, we dni przyszłe wszystkiego zapomną; a jako umiera mądry, tak i głupi.
Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali; mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika. Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!
17 Przetoż mi żywot omierzł; bo mi się nie podoba żadna rzecz, która się dzieje pod słońcem; albowiem wszystkie są marnością, i utrapieniem ducha.
Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
18 Nawet omierzła mi i wszystka praca moja, którąm podejmował pod słońcem, przeto, że ją zostawić muszę człowiekowi, który nastanie po mnie.
Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga.
19 A kto wie, będzieli mądrym, czyli głupim? a wszakże będzie panował nad wszystką pracą moją, którąm prowadził, i w którejm był mądry pod słońcem. Aleć i to marność.
Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake.
20 I przypadłem na to, abym zwątpił w sercu mojem o wszystkiej pracy, którąm się mądrze bawił pod słońcem.
Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano.
21 Nie jeden zaiste człowiek pracuje mądrze, i umiejętnie, i sprawiedliwie; a wszakże to innemu, który nie robił na to, za dział zostawi. I toć marność i wielka bieda.
Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu.
22 Bo cóż ma człowiek ze wszystkiej pracy swej, i z usiłowania serca swego, które podejmuje pod słońcem?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano?
23 Ponieważ wszystkie dni jego są bolesne, a zabawa jego jest frasunek, tak iż i w nocy nie odpoczywa serce jego. I toć jest marność.
Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.
24 Izali nie lepsza człowiekowi, aby jadł i pił, i dobrze uczynił duszy swojej z pracy swojej? alemci widział, że i to z ręki Bożej pochodzi.
Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu,
25 Albowiem któżby słuszniej miał jeść, i pożywać tego nad mię?
pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo?
26 Bo człowiekowi, który mu się podoba, daje mądrość, umiejętność, i wesele; ale grzesznikowi daje frasunek, aby zbierał i zgromadzał, coby zostawił temu, który się podoba Bogu. I toć jest marność, a utrapienie ducha.
Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.