< Powtórzonego 4 >

1 Teraz tedy, o Izraelu, słuchaj ustaw, i sądów, których ja was uczę, abyście je czyniąc żyli, a wszedłszy posiedli ziemię, którą Pan, Bóg ojców waszych, dawa wam.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 Nie przydacie do słowa, które ja wam rozkazuję, ani ujmiecie z niego, abyście strzegli przykazań Pana, Boga waszego, które ja wam rozkazuję.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 Oczy wasze widziały, co uczynił Pan dla Baal fegora, jako każdego męża, który się udawał za Baal fegorem, wytracił Pan, Bóg twój, z pośrodku was.
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 A wy, którzyście trwali przy Panu, Bogu waszym, żyjecie wszyscy aż do dnia dzisiejszego.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 Patrzcież, żem was nauczał ustaw i sądów, jako mi rozkazał Pan, Bóg mój, abyście tak czynili w ziemi tej, do której wchodzicie, abyście ją dziedzicznie posiedli.
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 Przestrzegajcież ich tedy, a czyńcie je; to bowiem jest mądrość wasza, i rozum wasz przed oczyma narodów; którzy usłyszawszy o tych wszystkich ustawach, rzeką: Tylko ten lud mądry, i rozumny, i naród wielki jest.
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Albowiem któryż naród tak wielki jest, coby mu byli bogowie tak bliscy, jako Pan, Bóg nasz, we wszystkiem, ilekroć go wzywamy?
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 Albo któryż naród tak wielki, któryby miał ustawy i sądy tak sprawiedliwe, jako wszystek ten zakon, który ja przedkładam wam dziś?
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 A wszakże miej się na pieczy, a strzeż duszy twej pilnie, byś snać nie zapomniał na te rzeczy, które widziały oczy twoje i aby snać nie odstąpiły od serca twego po wszystkie dni żywota twego; i oznajmisz je synom twym, i synom synów twoich.
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 Nie zapominaj, żeś onego dnia stał przed oblicznością Pana, Boga twego, na Horeb, gdy mówił Pan do mnie: Zgromadź mi lud, abym im powiedział słowa moje, których się uczyć będą, aby się mnie bali po wszystkie dni, pokąd żyć będą na ziemi, i synów swoich nauczając tego.
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 Tedyście przystąpili, a stanęliście pod górą, a ona góra pałała ogniem aż do samego nieba, a była na niej ciemność, obłok i mgła.
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 I mówił Pan do was z pośród ognia; głos słów słyszeliście, aleście podobieństwa żadnego nie widzieli oprócz głosu.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 I oznajmił wam przymierze swoje, które rozkazał wam, abyście je czynili, to jest dziesięć słów, które napisał na dwóch tablicach kamiennych.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 Mnie też rozkazał Pan na on czas, abym was nauczał ustaw i sądów, abyście je czynili w ziemi, do której idziecie, abyście ją dziedzicznie posiedli.
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 A tak strzeżcie pilnie dusz waszych, (gdyżeście nie widzieli żadnego podobieństwa, dnia, którego mówił Pan do was na Horebie z pośrodku ognia, )
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 Abyście się snać nie popsowali, i nie czynili sobie rytego bałwana, albo obrazu wszelkiego podobieństwa, kształtu mężczyzny albo niewiasty;
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 Albo kształtu jakiego zwierzęcia, które jest na ziemi, kształtu wszelkiego ptaka skrzydlastego, który lata po powietrzu;
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 Kształtu wszystkiego tego, co się płaza po ziemi, kształtu wszelkiej ryby, która jest w wodzie pod ziemią.
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 Ani podnoś oczu swych ku niebu, żebyś widząc słońce i miesiąc, i gwiazdy ze wszystkiemi zastępy niebieskiemi, nie dał się uwieść, abyś się im kłaniał, i służyłbyś im, ponieważ je oddał Pan, Bóg twój, na posługę wszystkim ludziom pod wszystkiem niebem.
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 Aleć was wziął Pan, i wywiódł was jako z żelaznego pieca, z Egiptu, abyście byli jego ludem dziedzicznym, jako dziś jesteście.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 A Pan rozgniewał się na mię dla was, a przysiągł, że nie przejdę przez Jordan, ani wnijdę do onej wybornej ziemi, którą Pan, Bóg twój, dawa tobie w dziedzictwo.
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 Bo ja umrę w tej ziemi, ja nie przejdę za Jordan; ale wy przejdziecie, i dziedzicznie osiądziecie tę dobrą ziemię.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Strzeżcież się, byście snać nie zapomnieli przymierza Pana, Boga waszego, które uczynił z wami, a nie czynili sobie rytego obrazu na kształt jakiejkolwiek rzeczy, jakoć rozkazał Pan, Bóg twój.
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 Albowiem Pan, Bóg twój, jest ogień trawiący, Bóg zawisny.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 Gdy spłodzisz syny i wnuki, a zstarzejecie się w ziemi onej, jeźlibyście się popsowali, a czynilibyście sobie ryte bałwany na kształt jakiejkolwiek rzeczy, i uczynilibyście co złego przed oczyma Pana, Boga waszego, drażniąc go:
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 Biorę na świadectwo przeciwko wam dziś niebo i ziemię, iż pewnie w rychle wyginiecie z ziemi, do której pójdziecie przez Jordan, abyście dziedzicznie ją posiedli; nie przedłużycie dni waszych w niej, bo pewnie wytraceni będziecie.
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 I rozproszy was Pan między narody, a zostanie was mało między narody, do których zaprowadzi was Pan.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 Tamże będziecie służyli bogom, robocie rąk ludzkich, drewnu i kamieniowi, które ani widzą, ani słyszą, ani wąchają.
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 A wszakże i tam jeźli szukać będziesz Pana, Boga twego, tedy znajdziesz, będzieszli go szukał całem sercem twojem, i całą duszą swoją.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 Gdy ucisk przyjdzie na cię, a najdą cię te wszystkie rzeczy w ostatnie dni, tedy, nawróciszli się do Pana, Boga twego, a posłusznym będziesz głosowi jego,
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 (Albowiem Bóg miłosierny Pan, Bóg twój jest) nie opuści cię, ani cię skazi, ani zapomni na przymierze ojców twoich, które im przysiągł.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 Pytaj się teraz na dni starodawne, które były przed tobą, ode dnia, którego stworzył Bóg człowieka na ziemi; a od jednego końca nieba aż do drugiego końca nieba stałali się kiedy rzecz podobna tej tak wielkiej? albo słuchanoli kiedy co takowego?
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 Słyszałli kiedy który naród głos Boga mówiącego z pośrodku ognia, jakoś ty słyszał, a żyw został?
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Albo kusiłli się który bóg przyjść a wziąć sobie naród z pośrodku innego narodu przez pokusy, przez znaki, i przez cuda, i przez wojny, i przez mocną rękę, i przez ramię wyciągnione, i w strachach wielkich, według wszystkiego, jako uczynił dla was Pan, Bóg wasz, w Egipcie przed oczyma twemi?
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 Tobie to ukazano, abyś wiedział, iż Pan jest Bóg, a nie masz innego oprócz niego.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 Dał ci z nieba słyszeć głos swój, aby cię wyćwiczył, a na ziemi ukazał ci ogień swój wielki, a słowa jego słyszałeś z pośrodku ognia.
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 A iż umiłował ojce twoje, obrał nasienie ich po nich, i wywiódł cię przed sobą mocą swoją wielką z Egiptu,
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 Aby wygnał narody wielkie i możniejsze nad cię przed twarzą twoją, i wprowadził cię, a dał ci ziemię ich w dziedzictwo, jako to dziś widzisz.
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 Wiedzże tedy dziś, a wspomnij na to w sercu twojem, iż Pan jest Bogiem na niebie wysoko, i na ziemi nisko nie masz innego.
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 A tak przestrzegaj ustaw jego, i przykazań jego, które ja dziś rozkazuję tobie, abyć się dobrze wodziło, i synom twoim po tobie; abyś też przedłużył dni na ziemi, którą Pan, Bóg twój, da tobie, po wszystkie dni.
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 Tedy oddzielił Mojżesz trzy miasta z tej strony Jordanu na wschód słońca.
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 Aby tam uciekał mężobójca, któryby zabił bliźniego swego z nieobaczenia, nie mając go w nienawiści przedtem, aby uciekłszy do jednego z tych miast, żyw został;
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 Beser na puszczy, w równinie w ziemi Rubenitów, i Ramot w Galaad między Gadyty, i Golam w Bazan między Manassytami.
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 Tenci jest zakon, który przedłożył Mojżesz synom Izraelskim.
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 Te są świadectwa, i ustawy, i sądy, które mówił Mojżesz do synów Izraelskich, gdy wyszli z Egiptu;
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 Z tej strony Jordanu, w dolinie przeciw Betfegor, w ziemi Sehona, króla Amorejskiego, który mieszkał w Hesebon, którego poraził Mojżesz, i synowie Izraelscy, gdy szli z Egiptu;
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 I osiedli ziemię jego, i ziemię Oga, króla Basańskiego, dwóch królów Amorejskich, którzy byli z tej strony Jordanu na wschód słońca;
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 Od Aroer, które jest nad brzegiem potoku Arnon, i aż do góry Syon, która jest Hermon;
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 I wszystkie pola nad Jordanem na wschód słońca, i aż do morza pustego, pod górą Fazga.
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.

< Powtórzonego 4 >