< Powtórzonego 32 >

1 Słuchajcie niebiosa, a mówić będę; niech słucha i ziemia wymowy ust moich.
Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
2 Kropić będzie jako deszcz nauka moja, popłynie jako rosa wymowa moja, jako drobny deszcz na zioła, a jako krople na trawę.
Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
3 Albowiem imienia Pańskiego będę wzywał; dajcież wielmożność Bogu naszemu,
Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
4 Skale, której sprawy są doskonałe; bo wszystkie drogi jego są sprawiedliwe. Boć jest Bóg prawdziwy, a nie masz w nim nieprawości, sprawiedliwy i prawy jest.
Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
5 Pokazili mu się, jakoby nie byli synami jego, sprosnością swoją, naród zły, a przewrotny.
Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
6 I także to oddawacie Panu, ludu głupi i szalony? izali nie on jest ojcem twoim, który cię sobie nabył? on cię uczynił, i stworzył cię.
Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
7 Wspomnij na dni dawne, uważajcie lata każdego wieku; spytaj ojca twego, a oznajmi tobie; starszych twoich, a powiedząć.
Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 Gdy rozdzielił dziedzictwa Najwyższy narodom, a rozsadził syny Adamowe, położył granice narodom według liczby synów Izraelskich;
Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 Albowiem działem Pańskim jest lud jego, Jakób sznurem dziedzictwa jego.
Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
10 Znalazł go w ziemi pustej, i na puszczy wielkiej i strasznej; obwodził go, uczył go, strzegł go, jako źrenicy oka swego.
Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 Jako orzeł wybawia orlęta swoje, nad orlętami swojemi latając, rozszerza skrzydła swoje, bierze je i nosi je na skrzydłach swoich;
ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Tak Pan sam prowadził go, a żaden obcy bóg nie był z nim.
Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 Wyniósł go na wysokie miejsca ziemi, aby używał urodzajów polnych, i uczynił, aby ssał miód z skały i oliwę z opoki twardej;
Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 Aby jadł masło od krów, i mleko od owiec, z tłustością jagniąt, i barany odchowane w Basan, i kozły z tłustością ziarn pszenicznych, a pił czerwone wino wyborne.
pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
15 I roztył Izrael, i wierzgał (otyłeś, stłuściałeś, zgrubiałeś, i opuściłeś Boga, który cię uczynił, ) i lekce poważył Boga, opokę zbawienia swego.
Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 Ku zapalczywości pobudzili go przez cudze bogi, i przez obrzydliwości rozdraźnili go.
Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 Ofiarowali dyjabłom, nie Bogu, bogom, których nie znali, nowym, którzy z bliska przyszli, których się nie bali ojcowie wasi.
Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Opoki, która cię spłodziła, zapomniałeś, zapomniałeś Boga, Stworzyciela twego.
Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
19 Co widząc Pan poruszył się gniewem na syny swoje, i na córki swoje.
Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
20 I rzekł: Skryję oblicze moje przed nimi, obaczę, jaki będzie koniec ich; albowiem są narodem przewrotnym, synami, w których wiary nie masz.
Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
21 Oni mię wzruszyli ku zapalczywości przez to, co nie jest Bogiem; pobudzili mię próżnościami swemi. Ja też do zazdrości pobudzę je przez te, którzy nie są ludem, przez naród głupi rozdraźnię je.
Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
22 Albowiem ogień rozpalił się w popędliwości mojej, i będzie gorzał aż do najgłębszego piekła, i pożre ziemię, i urodzaj jej, i wypali grunty gór. (Sheol h7585)
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
23 Zgromadzę na nie złe rzeczy, strzały moje na nie wystrzelam.
“Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
24 Zniszczeją od głodu, i będą strawieni gorączką, i śmiercią gorzką; zęby też bestyi poślę na nie, z jadem gadzin ziemskich.
Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
25 Zewnątrz osieroci je miecz, a w pokojach będzie strach, tak na młodzieńca, jako na pannę, na ssącego piersi, i na męża sędziwego.
Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
26 Rzekłem: Rozproszę je po kątach, i wygubię między ludźmi pamiątkę ich.
Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
27 Gdybym się na pychę nieprzyjaciół nie oglądał, by się snać nie podnieśli nieprzyjaciele ich, a nie rzekli: Ręka nasza wyniosła, a nie Pan, sprawiła to wszystko.
koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
28 Albowiem ten naród ginie przez rady swe, i nie ma rozumu.
Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
29 O by mądrymi byli! wyrozumieliby to, i oglądaliby się na ostatnie rzeczy swoje.
Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
30 Jakoby uganiał jeden z nich tysiąc, a dwaj goniliby dziesięć tysięcy! gdyby ich Bóg, opoka ich, nie zaprzedał, i Pan ich nie wydał:
Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
31 Albowiem nie jako skała nasza skała ich, co nieprzyjaciele nasi sami osądzą.
Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
32 Albowiem z macicy Sodomskiej macica ich, i z latorośli Gomorskich jagody ich, jagody jadowite, grona ich gorzkie.
Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
33 Jad smoczy wino ich, i trucizną żmij okrutną.
Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
34 Izali to nie jest skryto u mnie; zapieczętowano w skarbie moim?
“Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
35 Mojać jest pomsta i nagroda; czasu swego powinie się noga ich, ponieważ bliski jest dzień zginienia ich, a spieszą się przyszłe rzeczy do nich.
Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
36 Albowiem sądzić będzie Pan lud swój, a sług swoich użali się, gdy ujrzy, że ustała siła, a iż tak pojmany, jako zostawiony, nic nie mogą.
Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
37 I rzecze: Gdzież bogowie ich? Ona opoka, w której ufali?
Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
38 Którzy tłustość ofiar ich jadali, i pijali wino ofiar ich mokrych? Niechże wstaną, i ratują was, i niechaj będą ucieczką waszą.
milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
39 Obaczcież teraz, żem Ja, Jam jest sam, a że nie masz bogów oprócz Mnie; Ja zabijam i ożywiam, zranię, i Ja uleczę, a nie masz kto by z ręki mojej wyrwał.
“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
40 Albowiem podniosę ku niebu rękę moję, i rzekę: Żyję Ja na wieki.
Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
41 Jeźli zaostrzę błyszczący się miecz swój, i porwie sąd ręka moja, oddam pomstę nieprzyjaciołom moim, i tym, którzy mię nienawidzą, nagrodzę.
pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
42 Opoję strzały moje krwią, a miecz mój naje się mięsa ze krwi pobitych i pojmanych, skoro zacznę mścić się nad nieprzyjacioły.
Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
43 Weselcie się narodowie z ludem jego; albowiem krwi sług swoich pomści się, i pomstę odda nieprzyjaciołom swoim, a miłościw będzie ziemi swojej, i ludowi swemu.
Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
44 Tedy przyszedł Mojżesz, i mówił wszystkie słowa pieśni tej w uszach ludu tego, on i Jozue, syn Nunów.
Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
45 A gdy dokonał Mojżesz mówić tych wszystkich słów do wszystkiego Izraela,
Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
46 Rzekł do nich: Przyłóżcie serca wasze do wszystkich słów, któremi się ja oświadczam przeciwko wam dziś, abyście je przykazywali synom waszym, żeby strzegli i pełnili wszystkie słowa zakonu tego;
iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
47 Albowiem to słowo nie ma być próżne u was, gdyż jest żywotem waszym; i w tem słowie przedłużycie dni na ziemi, do której się przeprawiacie przez Jordan, abyście ją osiedli.
Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
48 I rzekł Pan do Mojżesza tegoż dnia, mówiąc:
Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
49 Wstąp na tę górę Abarym, na górę Nebo, która jest w ziemi Moabskiej przeciw Jerychu, a oglądaj ziemię Chananejską, którą Ja dawam synom Izraelskim w osiadłość.
“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
50 I umrzesz na tej górze, na którą wstąpisz, i będziesz przyłączony do ludu twego, jako umarł Aaron, brat twój, na górze Hor, i przyłączon jest do ludu swego;
Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
51 Dla tego żeście wystąpili przeciwko mnie w pośród synów Izraelskich przy wodach w poswarku w Kades na puszczy Syn, i żeście mię nie poświęcili w pośród synów Izraelskich.
Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
52 Bo przed sobą oglądasz ziemię; ale tam nie wnijdziesz, do tej ziemi, którą ja daję synom Izraelskim.
Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

< Powtórzonego 32 >