< Amosa 1 >

1 Słowa Amosa, który był między pasterzami z Tekua, które widział o Izraelu za dni Uzyjasza, króla Judzkiego, i za dni Jeroboama, syna Joazowego, króla Izraelskiego, dwa lata przed trzęsieniem ziemi.
Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
2 i rzekł: Zaryczy Pan z Syonu, z Jeruzalemu wyda głos swój; i będą płakały mieszkania pasterzy, a wyschną pola najwyborniejsze.
Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
3 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Damaszku, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, że młócili wozami żelaznemi Galaada;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
4 Ale poślę ogień na dom Hazaela, który pożre pałace Benadadowe.
Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
5 Połamię też zaworę w Damaszku, a wykorzenię obywatela z doliny Awen, i tego, który trzyma sceptr z domu Heden; i pójdzie w niewolę lud Syryjski do Kir, mówi Pan.
Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
6 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Gazy, owszem, dla czterech, nie przepuszczę im, przeto, że ich pojmawszy, w więzienie wieczne podawali Edomczykom;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
7 Ale poślę ogień na mur Gazy, który pożre pałace jej.
ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
8 Wykorzenię też obywatela z Azotu, i tego, który trzyma sceptr z Aszkalonu, i obrócę rękę moję przeciwko Akkaronowi, że zginie ostatek Filistynów, mówi panujący Pan.
Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
9 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Tyru, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, że ich w więzienie wieczne podali Edomczykom, a nie wspomnieli na przymierze braterskie;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
10 Ale poślę ogień na mur Tyrski, który pożre pałace jego.
Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
11 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Edoma, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, że zepsowawszy w sobie wszelaką litość swoję prześladuje mieczem brata swego, a gniewem swym ustawicznie pała, owszem, zapalczywość jego rozsila się bez przestania;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
12 Ale poślę ogień na Teman, i pożre pałace w Bocra.
Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
13 Tak mówi Pan: Dla trzech występków synów Amonowych, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, iż rozcinali brzemienne w Galaad, tylko aby rozszerzali granice swoje;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
14 Ale rozniecę ogień na murze Rabby, który pożre pałace jego z krzykiem w dzień wojny, i z wichrem w dzień niepogody.
Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
15 I pójdzie król ich w niewolę, on i książęta jego z nim, mówi Pan.
Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.

< Amosa 1 >