< Amosa 5 >

1 Słuchajcie słowa tego, które Ja wydaję przeciwko wam, to jest narzekania, o domie Izraelski!
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 Upadnie, a nie powstanie więcej panna Izraelska; opuszczona będzie w ziemi swej, a nie będzie, ktoby ją podniósł.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Bo tak mówi panujący Pan: W mieście, z którego wychodziło tysiąc, zostanie sto, a w tem, z którego wychodziło sto, zostanie dziesięć domowi Izraelskiemu.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Bo tak mówi Pan domowi Izraelskiemu: Szukajcie mię, a żyć będziecie;
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 A nie szukajcie Betela, ani chodźcie do Galgal, i do Beerseby nie udawajcie się; bo Galgal w niewolę zawiedzione będzie, a Betel się wniwecz obróci.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Szukajcie Pana, a żyć będziecie, by snać domu Józefowego nie przeniknął jako ogień, i nie pochłonął Betel, a nie byłby, ktoby ugasił;
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 Którzy obracacie sąd w piołun, a sprawiedliwość na ziemi opuszczacie: Szukajcie, mówię.
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 Tego, który uczynił Baby na niebie i Oriona, który cień śmierci w poranek odmienia i dzień w ciemności nocne; który przywołuje wody morskie, a wylewa je na oblicze ziemi, Pan jest imię jego;
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Który pokrzepia słabego przeciwko mocarzowi, tak że ten osłabiały do twierdzy uchodzi.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Mają w nienawiści tego, który ich w bramie karze; a tym, co mówi rzeczy dobre, brzydzą się.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Przetoż, iż uciskacie ubogiego, a brzemię zboża bierzecie od niego, domuweście wprawdzie z ciosanego kamienia nabudowali, ale nie będziecie w nich mieszkać; winnic rozkosznych nasadziliście, ale wina z nich pić nie będziecie.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 Bo wiem o wielkich przestępstwach waszych, i srogich grzechach waszych, że ciemiężycie sprawiedliwego, biorąc poczty, a ubogich sprawy w bramie podwracacie.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Przetoż roztropny czasu onego milczeć musi; bo czas zły jest.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Szukajcie dobrego a nie złego, abyście żyli; a będzie tak Pan Bóg zastępów z wami, jako mówicie.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Miejcie w nienawiści złe, a miłujcie dobre, a sąd postanówcie w bramie; owa się snać Pan, Bóg zastępów, nad ostatkiem Józefa zmiłuje.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Przetoż tak mówi panujący Pan, Bóg zastępów: Po wszystkich ulicach będzie narzekanie, a po wszystkich stronach zakrzykną: Biada, biada! i zawołają oracza do płaczu i do kwilenia z tymi, którzy narzekać umieją.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Owszem, i po wszystkich winnicach będzie narzekanie, gdy przejdę przez pośrodek ciebie, mówi Pan.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Biada tym, którzy żądają dnia Pańskiego! cóż wam po tym dniu Pańskim, ponieważ jest ciemnością, a nie światłością?
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Jako gdyby kto uciekał przede lwem, a zabieżał mu niedźwiedź; albo gdyby wszedł do domu, a podparł się ręką swą na ścianie, ukąsiłby go wąż.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Izali dzień Pański nie jest dzień ciemności, a nie światłości, w którym niemasz jasności, ale chmura?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Mam w nienawiści i odrzuciłem uroczyste święta wasze, ani się kocham w ofiarach zgromadzenia waszego.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Bo jeźli mi ofiarować będziecie całopalenia, i śniedne ofiary wasze, nie przyjmę ich, a na spokojne ofiary tłustych bydeł waszych nie wejrzę.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Odejmij odemnie wrzask pieśni swoich; bo ich i dźwięku harf waszych słuchać nie chcę.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Ale sąd nawalnie popłynie, jako woda, a sprawiedliwość jako strumień gwałtowny.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Izaliście mi ofiary i dar ofiarowali na puszczy przez czterdzieści lat, domie Izraelski?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Owszem, nosiliście namiot Molocha waszego i Kijuna, obrazy wasze, gwiazdę bogów waszych, którycheście sobie naczynili.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Przetoż was zaprowadzę za Damaszek, mówi Pan, Bóg zastępów imię jego.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amosa 5 >