< Amosa 4 >

1 Słuchajcie słowa tego, o krowy Basańskie! któreście na górach Samaryi, które uciskacie nędzników a niszczycie ubogich, które mówicie panom ich: Przynieście, abyśmy piły.
Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
2 Przysiągł panujący Pan przez świętobliwość swoję, iż oto dni idą na was, których nieprzyjaciel weźmie was na haki, a potomki wasze na wędy rybackie, i wyjdziecie przerwami, każda tak jako stoi;
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
3 I będziecie rozrzucać cokolwiek było w pałacach waszych, mówi Pan.
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
4 Idźcież do Betel a bądzcie tułaczami w Galgal; rozmnóżcie przestępstwa, a przynoście na każdy poranek ofiary wasze, i trzeciego roku dziesięciny wasze;
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
5 A paląc ofiarę chwały z kwaszonych rzeczy, obwołajcie ofiary dobrowolne, i rozgłoście, ponieważ się wam tak podoba, o synowie Izraelscy! mówi panujący Pan.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
6 A chociażem Ja wam dał czystość zębów we wszystkich miastach waszych, to jest, niedostatek chleba po wszystkich miejscach waszych, wszakżeście się nie nawrócili do mnie, mówi Pan.
“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
7 Jam też zahamował od was deszcz, gdy jeszcze były trzy miesięce do żniwa, a spuściłem deszcz na jedne miasto, a na drugiem miasto nie spuścił; jedna dziedzina była deszczem odwilżona, a druga dziedzina, na którą deszcz nie padał, uschła.
“Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 I chodziły dwa i trzy miasta do jednego miasta, aby piły wodę, a nie mogły się napić; a wszakżeście się nie nawrócili do mnie, mówi Pan.
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
9 Uderzyłem was suszą i rdzą; obfitość, którą przynosiły ogrody wasze, i winnice wasze, i figowe sady wasze, i oliwnice wasze, gąsienice pożarły, a wszakżeście się nie nawrócili do mnie, mówi Pan.
“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
10 Posłałem na was mór, tak jako na Egipt, pobiłem mieczem młodzieńców waszych, w pojmaniem podał konie wasze, i sprawiłem, że smród wojsk waszych występował w nozdrza wasze; a wszakżeście się nie nawrócili do mnie, mówi Pan.
“Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
11 Wywróciłem was, jako Bóg wywrócił Sodomę i Gomorę, tak, żeście byli jako głownia wyrwana z ognia; a wszakżeście się nie nawrócili do mnie, mówi Pan.
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
12 Przetoż tak ci uczynię, o Izraelu! a iż ci tak uczynić chcę, bądźże gotowym na zabieżenie Bogu swemu, o Izraelu!
“Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 Albowiem oto on jest, który kształtuje góry, a tworzy wiatry, i który oznajmuje człowiekowi, jaka jest myśl jego; on z rannej zorzy ciemność czyni, a depcze wysokości ziemi; Pan Bóg zastępów jest imię jego.
Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amosa 4 >