< Amosa 2 >
1 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Moaba, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, iż spalił kości króla Edomskiego na popiół;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Ale poślę ogień na Moaba, który pożre pałace Karyjot; i umrze Moab w huku, w krzyku i w głosie trąby.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 I wygładzę sędziów z pośrodku jego, i wszystkich książąt jego pobiję z nim, mówi Pan.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Judzkich, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, że odrzucają zakon Pański, i ustaw jego nie przestrzegają, a dadzą się zwodzić kłamstwom swoim, których naśladowali ojcowie ich;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Ale poślę ogień na Judę, który pożre pałace Jeruzalemskie.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Tak mówi Pan: Dla trzech występków Izraelskich, owszem, dla czterech, nie przepuszczę mu, przeto, że sprawiedliwego za pieniądze sprzedawają, a ubogiego za parę trzewików;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 Którzy usiłują, aby na proch potarli głowy ubogich, a drogę pokornych podwracają; nadto syn i ojciec jego wchodzą do jednejże dziewki, aby splugawili imię świętobliwości mojej;
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 I na szatach zastawionych kłaniają się przy każdym ołtarzu, a wino tych, co podpadli pod kaźń, piją w domu bogów swoich.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Chociażem Ja wytracił Amorejczyka od oblicza ich, którego wysokość była jako wysokość cedrów, aczkolwiek warownie stał jako dąb, wszakżem skaził owoc jego z wierzchu, a korzenie jego ze spodku.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 A was wywiodłem z ziemi Egipskiej, i prowadziłem was po puszczy czterdzieści lat, żebyście posiedli ziemię Amorejczyka.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Nadto wzbudzałem z synów waszych proroków, a z młodzieńców waszych Nazarejczyków; izali nie tak jest, o synowie Izraelowi? mówi Pan.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 Aleście wy napawali Nazarejczyków winem, a prorokom zakazywaliście, mówiąc: Nie prorokujcie.
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Oto Ja ścisnę ziemię waszę, tak jako ciśnie wóz napełniony snopami.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 I zginie ucieczka od prędkiego, a mocarz nie pokrzepi mocy swojej, i duży nie wybawi duszy swojej;
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 A ten, który trzyma łuk, nie ostoi się, i prędki na nogi swe nie uciecze, a ten, który jeździ na koniu, nie zachowa duszy swej,
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Ale i rycerz serca zmężałego między mocarzami nago uciecze w on dzień, mówi Pan.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.