< II Tymoteusza 1 >
1 Paweł, Apostoł Jezusa Chrystusa przez wolę Bożą, według obietnicy żywota onego, który jest w Chrystusie Jezusie;
Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
2 Tymoteuszowi, miłemu synowi, niech będzie łaska, miłosierdzie i pokój od Boga Ojca i Chrystusa Jezusa, Pana naszego.
Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
3 Dziękuję Bogu, któremu służę z przodków w czystem sumieniu, że cię bez przestanku wspominam w prośbach moich, w nocy i we dnie,
Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga.
4 Żądając cię widzieć, wspominając na twoje łzy, abym był radością napełniony,
Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe.
5 Przywodząc sobie na pamięć onę, która w tobie jest, nieobłudną wiarę, która pierwej mieszkała w babce twojej Loidzie i w matce twojej Eunice, a pewienem, że i w tobie mieszka.
Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.
6 Dla której przyczyny przypominam ci, abyś wzniecał dar Boży, który w tobie jest przez włożenie rąk moich.
Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja.
7 Albowiem nie dał nam Bóg Ducha bojaźni, ale mocy i miłości, i zdrowego zmysłu.
Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.
8 Przetoż nie wstydź się za świadectwo Pana naszego, ani za mię, więźnia jego, ale cierp złe z Ewangieliją według mocy Bożej.
Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu.
9 Który nas zbawił i powołał powołaniem świętem, nie według uczynków naszych, ale według postanowienia swego i łaski, która nam jest dana w Chrystusie Jezusie przed czasy wiecznemi. (aiōnios )
Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios )
10 A teraz objawiona jest przez okazanie się zbawiciela naszego, Jezusa Chrystusa, który i śmierć zgładził, i żywot na jaśnię wywiódł, i nieśmiertelność przez Ewangieliję,
Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe.
11 Której jam jest postanowiony kaznodzieją i Apostołem, i nauczycielem pogan.
Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu.
12 Dla której też przyczyny te rzeczy cierpię; aleć się nie wstydzę, gdyż wiem, komum uwierzył i pewienem, iż on mocen jest tego, czego mi się powierzył, strzec aż do onego dnia.
Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.
13 Zatrzymaj wzór zdrowych słów, któreś ode mnie usłyszał, w wierze i w miłości, która jest w Chrystusie Jezusie.
Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.
14 Strzeż dobrego pokładu przez Ducha Świętego, który w nas mieszka.
Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.
15 Wiesz to, iż mię odstąpili wszyscy, którzy są w Azyi, z których jest Fygellus i Hermogenes.
Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.
16 Niech da Pan miłosierdzie swoje Onezyforowemu domowi, iż mię często ochłodził i za łańcuch mój się nie wstydził;
Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo.
17 Ale będąc w Rzymie, bardzo mię pilno szukał i znalazł.
Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza.
18 Niech mu Pan da, aby znalazł miłosierdzie u Pana w on dzień; a ty lepiej wiesz, jako mi wiele usługiwał w Efezie.
Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.