< II Samuela 9 >

1 Tedy rzekł Dawid: Jestże jeszcze kto, coby pozostał z domu Saulowego, abym uczynił nad nim miłosierdzie dla Jonatana?
Davide anafunsa kuti, “Kodi alipo amene watsala mʼbanja la Sauli kuti ndimuchitire chifundo chifukwa cha Yonatani?”
2 I był z domu Saulowego sługa, którego zwano Syba: tego zawołano do Dawida. I rzekł król do niego: Tyżeś jest Syba? A on odpowiedział: Jam jest, sługa twój.
Tsono panali mtumiki wina wa banja la Sauli wotchedwa Ziba. Iwo anamuyitana kuti aonekere pamaso pa Davide, ndipo mfumu inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe Ziba?” Iyeyo anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
3 Potem rzekł król: Jestże jeszcze kto z domu Saulowego, abym nad nim uczynił miłosierdzie Boże? Odpowiedział Syba królowi: Jest jeszcze syn Jonatana, chromy na nogi.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi palibe amene watsala wa banja la Sauli amene ndingamuchitire chifundo cha Mulungu?” Ziba anayankha mfumu kuti, “Alipo mwana wa Yonatani, koma ndi wolumala mapazi ake onse.”
4 I rzekł do niego król: Gdzieli jest? A Syba odpowiedział królowi: Oto, jest w domu Machira, syna Ammijelowego, w Lodebarze.
Mfumu inafunsa kuti, “Ali kuti?” Ziba anayankha kuti, “Iye ali ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli ku Lodebara.”
5 Przetoż posłał król Dawid, i wziął go z domu Machira, syna Ammijelowego z Lodebaru.
Kotero mfumu inamubweretsa kuchokera ku Lodebara, ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli.
6 A gdy przyszedł Mefiboset, syn Jonatana, syna Saulowego, do Dawida, upadł na oblicze swe, i pokłonił się. I rzekł Dawid: Mefibosecie! Który odpowiedział: Oto, sługa twój.
Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli atafika kwa Davide, anawerama pansi kupereka ulemu kwa iye. Davide anati, “Mefiboseti!” Iye anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
7 I rzekł do nigo Dawid: Nie bój się: bo zapewne uczynię z tobą miłosierdzie dla Jonatana, ojca twego, i przywrócęć wszystkę rolą Saula, dziada twego. a ty będziesz jadł chleb u stołu mego zawżdy.
Davide anati kwa iye, “Usachite mantha, pakuti ndidzakuchitira ndithu chifundo chifukwa cha abambo ako Yonatani. Ine ndidzakubwezera iwe dziko lonse limene linali la agogo ako Sauli, ndipo iweyo udzadya ndi ine nthawi zonse.”
8 Tedy ukłoniwszy się, rzekł: Coż jest sługa twój, żeś się obejrzał na psa zdechłego, jakom ja jest?
Mefiboseti anawerama pansi ndipo anati, “Mtumiki wanu ndine yani kuti musamale galu wakufa ngati ine?”
9 Zatem wezwał król Syby, sługi Saulowego i rzekł mu: Cokolwiek miał Saul, i wszystek dom jego, dałem synowi pana twego.
Kenaka Davide anayitanitsa Ziba, mtumiki wa Sauli, ndipo anati, “Ine ndapereka kwa chidzukulu cha mbuye wako chilichonse chimene chinali cha Sauli ndi banja lake.
10 Będziesz tedy sprawował rolą jego, ty, synowie twoi, i słudzy twoi, a będziesz dodawał, aby miał chleb syn pana twego, któryby jadł; ale Mefiboset, syn pana twego, będzie zawżdy jadał chleb u stołu mego. A Syba miał piętnaście synów i dwadzieścia sług.
Iwe ndi ana ndi antchito anu muzimulimira mʼdziko lake ndipo muzibweretsa zokololazo kuti chidzukulu cha mbuye wako chikhale ndi chakudya. Ndipo Mefiboseti, chidzukulu cha mbuye wako adzadya ndi ine nthawi zonse.” (Tsono Ziba anali ndi ana aamuna khumi ndi asanu ndi antchito makumi awiri).
11 I odpowiedział Syba królowi: Wszystko, co rozkazał król, pan mój, słudze swemu, tak uczyni sługa twój, aczkolwiek Mefiboset mógłby jadać u stołu mego, jako jeden z synów królewskich.
Ndipo Ziba anati kwa mfumu, “Mtumiki wanu adzachita chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mudzalamulire wantchito wanu kuti achite.” Kotero Mefiboseti ankadya ndi Davide monga mmodzi wa ana a mfumu.
12 Miał też Mefiboset syna małego, imieniem Micha; a wszyscy, którzy mieszkali w domu Sybowym, byli sługami Mefibosetowymi.
Mefiboseti anali ndi mwana wamngʼono wamwamuna wotchedwa Mika, ndipo onse a banja la Ziba anali antchito a Mefiboseti.
13 A tak Mefiboset mieszkał w Jeruzalemie, bo on u stołu królewskiego zawżdy jadał; a był chromy na obie nogi.
Ndipo Mefiboseti anakhala mu Yerusalemu chifukwa nthawi zonse amadya ndi mfumu. Iye anali wolumala mapazi ake onse.

< II Samuela 9 >