< II Samuela 4 >

1 A usłyszawszy Izboset, syn Saula, że poległ Abner w Hebronie, zemdlały ręce jego, i wszystek Izrael był przestraszony.
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 Miał też syn Saula dwóch mężów hetmanów nad hufcami, imię jednego Baana, a imię drugiego Rechab, synowie Remmona Berotczyka z synów Benjaminowych; bo też Berot policzon był w Benjaminie.
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 Uciekli tedy Berotczykowie do Gietaim, i byli tam przychodniami aż do onego dnia.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 A Jonatan, syn Saula, miał jednego syna chromego na nogi, (bo gdy miał pięć lat, a przyszła wieść o śmierci Saulowej, i Jonatanowej z Jezreel, a wziąwszy go mamka jego uciekła, a gdy prędko uciekała, upadł i ochromiał, ) a imię jego Mefiboset.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 Poszli tedy synowie Remmona Berotczyka, Rechab i Baana, i weszli, gdy był najgorętszy dzień, do domu Izboseta, który spał na łóżku w południe.
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 Ci tedy weszli w dom jego, jakoby kupować zboża; tamże go przebili pod piąte żebro Rechab i Baana, brat jego, i uciekli.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 Bo gdy byli weszli w dom, a on spał na łóżku swem w pokoju, kędy legał, tedy go przebili, i zabili go, a uciąwszy głowę jego, wzięli ją, i poszli drogą puszczy przez całą onę noc.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 I przynieśli głowę Izbosetowę do Dawida do Hebronu, i rzekli do króla; Oto, głowa Izboseta, syna Saulowego, nieprzyjaciela twego, który szukał duszy twojej; a dał Pan królowi, panu memu, pomstę dzisiaj nad Saulem i nad nasieniem jego.
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 Tedy odpowiedział Dawid Rechabowi i Baanie, bratu jego, synom Remmona Berotczyka, i rzekł do nich: Jako żyw Pan, który wybawił duszę moję od wszelkiego ucisku:
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 Jeźlim onego, który mi oznajmił, mówiąc: Oto umarł Saul, (choć mu się zdało, że wesołą nowinę przyniósł, ) pojmawszy zabił w Syclegu, który rozumiał, żem mu miał dać zapłatę za poselstwo jego:
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 Jako daleko więcej ludzie niepobożne, gdyż zabili męża sprawiedliwego w domu jego, na łożu jego? A teraz, izali nie mam szukać krwi jego z ręki waszej, i wygładzić was z ziemi?
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 A tak rozkazał Dawid sługom, i zabili je, a obciążywszy ręce ich, i nogi ich, zawiesili je nad stawem w Hebronie; ale głowę Izbosetową wziąwszy pogrzebali w grobie Abnerowym w Hebronie.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< II Samuela 4 >