< II Samuela 3 >

1 I była długa wojna między domem Saulowym i między domem Dawidowym. Wszakże Dawid postępował, i zmacniał się; ale dom Saulów schodził i niszczał.
Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
2 I narodziło się Dawidowi w Hebronie synów. A był pierworodny jego Amnon z Achinoamy Jezreelitki;
Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
3 Wtóry po nim był Helijab z Abigaili, żony przedtem Nabalowej z Karmelu, a trzeci Absalom, syn Moachy, córki Tolmaja króla Giessur;
Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
4 A czwarty Adonijasz, syn Hagity, a piąty Sefatyjasz, syn Abitali;
wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
5 A szósty Jetraam z Egli, żony Dawidowej. Cić się urodzili Dawidowi w Hebronie.
ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
6 I stało się, gdy była wojna między domem Saulowym i między domem Dawidowym, a Abner się mężnie zastawiał o dom Saulowy.
Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
7 (A Saul miał założnicę, której imię było Resfa, córka Aje, ) że rzekł Izboset do Abnera: Czemuś wszedł do założnicy ojca mojego?
Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
8 I rozgniewał się Abner bardzo o one słowa Izbosetowe, i rzekł: Izalim ja psia głowa, którym przeciw Judzie dziś uczynił miłosierdzie nad domem Saula, ojca twego, i nad bracią jego, i nad przyjaciółmi jego, i nie wydałem cię w rękę Dawidowę, a ty d ziś szukasz na mnie nieprawości tej niewiasty?
Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
9 To niech uczyni Bóg Abnerowi, i to niech mu przyczyni, jeźliże, jako przysiągł Pan Dawidowi, nie pomogę do tego.
Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
10 Aby przeniesione było królestwo od domu Saulowego, a wystawiona stolica Dawidowa nad Izraelem, i nad Judą od Dan aż do Beerseba.
Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
11 I nie mógł nic więcej odpowiedzieć Abnerowi, przeto że się go bał.
Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
12 A tak wyprawił Abner posły do Dawida od siebie, mówiąc: Czyjaż jest ziemia? i żeby mówili: Uczyń przymierze twoje ze mną, a oto ręka moja będzie z tobą, aby obrócon był do ciebie wszystek Izrael.
Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
13 Któremu odpowiedział: Dobrze, uczynię z tobą przymierze. A wszakże o jedno cię proszę, mianowicie, abyś nie przychodził przed oblicze moje, aż mi pierwej przywiedziesz Michol, córkę Saulowę, gdy będziesz chciał przyjść, abyś widział twarz moję.
Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
14 I wyprawił Dawid posły do Izboseta syn Saulowego, mówiąc: Wydaj mi żonę moję Michol, którąm sobie poślubił stem nieobrzezek Filistyńskich.
Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
15 Przetoż posłał Izboset, i wziął ją od męża, od Faltejela, syna Laisowego.
Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
16 Tedy szedł z nią mąż jej, a idąc za nią, płakał jej aż do Bachurym; i rzekł do niego Abner: Idź, a wróć się; i wrócił się.
Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
17 Uczynił potem Abner rzecz do starszych Izraelskich mówiąc: Przeszłych czasów szukaliście Dawida, aby był królem nad wami.
Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
18 Przetoż teraz uczyńcie tak; bo Pan rzekł o Dawidzie, mówiąc: Przez rękę Dawida, sługi mego, wybawię lud mój Izraelski z ręki Filistyńskiej, i z ręki wszystkich nieprzyjaciół jego.
Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
19 To też mówił Abner i do Benjamińczyków. Potem odszedł Abner, aby mówił z Dawidem w Hebronie wszystko, co dobrego było w oczach Izraela, i w oczach wszystkiego domu Benjaminowego.
Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
20 Gdy tedy przeszedł Abner do Dawida do Hebronu, a z nim dwadzieścia mężów, sprawił Dawid na Abnera, i na męże, którzy z nim byli, ucztę.
Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
21 I rzekł Abner do Dawida: Wstanę, a pójdę, abym zebrał do króla, pana mego, wszystkiego Izraela, którzy z tobą uczynią przymierze; a będziesz królował nad wszystkimi, jako żąda dusza twoja. A tak odprawił Dawid Abnera, który odszedł w pokoju.
Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
22 A oto, słudzy Dawidowi i Joab wracali się z wojny, korzyści wielkie z sobą prowadząc, ale Abnera już nie było u Dawida w Hebronie: bo go był odprawił, i odszedł był w pokoju.
Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
23 Joab tedy i wszystko wojsko, które z nim było, przyszli tam; i dano znać Joabowi, mówiąc: Był tu Abner, syn Nera, u króla; ale go odprawił, i odszedł w pokoju.
Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
24 Przetoż wszedłszy Joab do króla, rzekł: Cóżeś uczynił? Oto, przyszedł był Abner do ciebie; przeczżeś go puścił, aby zaś odszedł.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
25 Znasz Abnera, syna Nerowego, gdyż przyszedł, aby cię zdradził, i żeby wiedział wyjście twoje, i wejście twoje, aby się wywiedział o wszystkiem, co ty czynisz.
Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
26 Tedy odszedłszy Joab od Dawida, wyprawił posły za Abnerem, którzy go wrócili od studni Syra, o czem Dawid nie wiedział.
Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
27 A gdy się wrócił Abner do Hebronu, odwiódł go Joab w pośród bramy, aby z nim po cichu (osobno) mówił, i przebił go tam pod piąte żebro, że umarł dla krwi Asaela, brata swego.
Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
28 Co gdy potem usłyszał Dawid, rzekł: Nie jestem winien, ani królestwo moje, przed Panem aż na wieki krwi Abnera, syna Nerowego.
Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
29 Niechaj przyjdzie na głowę Joabowę, i na wszystek dom ojca jego, i niech nie ustaje z domu Joabowego płynienie nasienia cierpiący, i trędowaty, i o kiju chodzący, i od miecza upadający, i nie mający chleba.
Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
30 A tak Joab i Abisaj, brat jego, zabili Abnera, przeto iż on też był zabił Asaela, brata ich, w bitwie u Gabaona.
(Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
31 Rzekł potem Dawid do Joaba i do wszystkiego ludu, który był z nim: Porozdzierajcie odzienia wasze a opaszcie się w wory, i płaczcie nad Abnerem. A król Dawid szedł za marami.
Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
32 A gdy pogrzebli Abnera w Hebronie, podniósł król głos swój, i płakał nad grobem Abnerowym; płakał też wszystek lud.
Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
33 A tak lamentując król nad Abnerem, rzekł: Izali tak miał umrzeć Abner, jako umiera nikczemnik?
Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
34 Ręce twoje nie były związane, a nogi twoje nie były pętami obciążone; poległeś jako ten, który pada przed synami niezbożnymi. Tedy tem więcej wszystek lud płakał nad nim.
Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
35 Potem przyszedł wszystek lud prosić Dawida, aby jadł chleb, gdy jeszcze był jasny dzień: ale przysiągł Dawid, mówiąc: To mi niech uczyni Bóg, i to niech przyczyni, jeźli przed zajściem słońca skosztuję chleba, albo czego innego.
Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
36 Co gdy wszystek lud obaczył, podobało się im to; a wszystko cokolwiek czynił król, podobało się w oczach wszystkiego ludu.
Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
37 I poznał wszystek Izrael dnia onego, że nie z naprawy królewskiej zabity był Abner, syn Nera.
Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
38 I rzekł król do sług swoich: Azaż nie wiecie, że hetman, a bardzo wielki, poległ dziś w Izraelu?
Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
39 A ja dziś jako nowy, i dopiero pomazany król; ci zasię mężowie, synowie Sarwii, srożsi są niżli ja; niechże odda Pan czyniącemu złe według złości jego.
Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”

< II Samuela 3 >