< II Samuela 24 >

1 Tedy się znowu popędliwość Pańska zapaliła na Izraela, gdy pobudził szatan Dawida przeciwko nim mówiąc: Idź, policz Izraela i Judę.
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 I rzekł król do Joaba, hetmana wojska swego: Przbież zaraz wszystkie pokolenia Izraelskie od Dan aż do Beerseba, a policzcie lud, abym wiedział poczet ludu.
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Lecz Joab rzekł do króla: Niech przymnoży Pan, Bóg twój, ludu, jako teraz jest tyle stokroć, aby na to oczy króla, pana mego patrzały; ale król, pan mój, przeczże się tego napiera?
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Wszakże przemogło słowo królewskie Joaba i hetmany wojska. Przetoż wyszedł Joab, i hetmani wojska od oblicza królewskiego, aby policzyli lud Izraelski.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 A przeprawiwszy się przez Jordan, położyli się obozem przy Aroer, po prawej stronie miasta, które jest w pośród potoku Gad i przy Jazer.
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Potem przyszli do Galaad, i do ziemi dolnej Hadsy, a stamtąd przyszli do Dan Jaan i w okół Sydonu.
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 Potem przyszli ku twierdzy Tyrskiej, i do wszystkich miast Hewejskich i Chananejskich, skąd wyszli na południe Judy do Beerseba.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 A obszedłszy wszystkę ziemię, przyszli po dziewięciu miesiącach, i po dwudziestu dniach do Jeruzalemu.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 I oddał Joab poczet obliczonego ludu królowi. A było w Izraelu ośm kroć sto tysięcy mężów rycerskich, godnych ku bojowi, a mężów Juda pięć kroć sto tysięcy mężów.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Potem uderzyło Dawida serce jego, gdy obliczył lud, i rzekł Dawid do Pana: Zgrzeszyłem bardzo, żem to uczynił: ale teraz o Panie! przenieś proszę nieprawość sługi twego, bomci bardzo głupio uczynił.
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 A gdy wstał Dawid rano, oto słowo Pańskie stało się do Gada proroka, Widzącego Dawidowego, mówiąc:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 Idź, a powiedz Dawidowi: Tak mówi Pan: Trzyć rzeczy podawam, obierz sobie jednę z tych, abym ci uczynił.
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 A tak przyszedł Gad do Dawida, i oznajmił mu, a rzekł mu: Albo przyjdzie na cię głód przez siedm lat w ziemi twojej, albo przez trzy miesiące będziesz uciekał przed nieprzyjacioły twymi, a oni cię gonić będą, albo więc przez trzy dni będzie morowe powietrze w ziemi twojej; rozmyśl że się prędko, a obacz, co mam odpowiedzieć temu, który mię posłał.
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 I rzekł Dawid do Gada: Jestem bardzo ściśniony. Niech proszę raczej wpadniemy w rękę Pańską, gdyż wielkie są zlitowania jego; ale w rękę ludzką niech nie wpadam.
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 Tedy przepuścił Pan powietrze morowe na Izraela od poranku aż do czasu naznaczonego, i umarło z ludu od Dan aż do Beerseba siedmdziesiąt tysięcy mężów.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 A gdy wyciągnął Anioł rękę swą na Jeruzalem, aby je wytracił, tedy się użalił Pan onego złego, i rzekł do Anioła, który tracił lud: Dosyć teraz; zawściągnij rękę twą. A Anioł Pański był podle bojewiska Arawny Jebuzejczyka.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 I rzekł Dawid do Pana, gdy ujrzał Anioła bijącego lud, mówiąc: Otom ja zgrzeszył, jam źle uczynił; ale te owce cóż uczyniły? niech się proszę obróci ręka twoja na mię i na dom ojca mego.
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 Tedy przyszedł Gad do Dawida onegoż dnia, i rzekł mu: Idź, a zbuduj ołtarz Panu na bojewisku Arawy Jebuzejczyka.
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 I szedł Dawid podług słowa Gadowego, jako był rozkazał Pan.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 Tedy spojrzawszy Arawna, ujrzał króla, i sługi jego, przychodzące do siebie: i wyszedł Arawna, a pokłonił się królowi twarzą swą ku ziemi.
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 I rzekł Arawna: Przeczże przyszedł król, pan mój, do sługi swego? I odpowiedział Dawid: Abym kupił u ciebie to bojewisko, i zbudował na niem ołtarz Panu, żeby zahamowana była ta plaga między ludem.
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Tedy rzekł Arawna do Dawida: Niech weźmie, a ofiaruje król, pan mój, co mu się dobrego widzi: oto woły na całopalenie, i wozy, i jarzma wołów na drwa.
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Wszystko to dawał król Arawna królowi Dawidowi. I mówił Arawna do króla: Pan, Bóg twój, niech cię sobie upodoba.
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Lecz król rzekł do Arawny: Nie tak, ale raczej kupię u ciebie i zapłacę; ani będę ofiarował Panu, Bogu memu, całopalenia darmo danego. A tak kupił Dawid ono bojewisko i woły za pięćdziesiąt syklów srebra.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 Tamże zbudował Dawid ołtarz Panu, i sprawował całopalenia, i spokojne ofiary. I ubłagany był Pan ziemi, a zahamowana jest ona plaga od Izraela.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.

< II Samuela 24 >