< II Samuela 21 >

1 I był głód za dni Dawidowych przez trzy lata, jednego roku po drugim. Tedy szukał Dawid oblicza Pańskiego, któremu rzekł Pan: Dla Saula, i dla domu jego krwawego, przeto iż pomordował Gabaonity.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide kunali njala kwa zaka zitatu zotsatana. Kotero Davide anapemphera kwa Yehova. Yehova anati, “Izi zachitika chifukwa chakuti Sauli ndi banja lake akanali ndi mlandu wakupha Agibiyoni.”
2 Przyzwał tedy król Gabaonitów, i rzekł do nich: (A ci Gabaonitowie nie byli z synów Izraelskich, ale z ostatków Amorejczyków, którym acz byli synowie Izraelscy przysięgli, wszakże je usiłował Saul wyplenić z gorliwości swej dla synów Izraelskich i Judzkich.)
Mfumu inayitanitsa Agibiyoni ndipo inayankhula nawo. (Tsono Agibiyoni sanali Aisraeli, koma otsala mwa Aamori. Aisraeli analumbira kuwasiya ndi moyo, koma Sauli chifukwa cha chikondi cha pa Israeli ndi Yuda, anafuna kuwawonongeratu).
3 I rzekł Dawid do Gabaonitów: Cóż wam mam uczynić? a czem was ubłagać, abyście błogosławili dziedzictwu Pańskiemu?
Davide anafunsa Agibiyoni kuti, “Kodi ine ndikuchitireni chiyani? Ndipepese bwanji kuti inu mudalitse cholowa cha Yehova?”
4 I odpowiedzieli mu Gabaonitowie: Nie idzie nam o srebro ani o złoto z Saulem, i z domem jego, ani o to, żebyśmy zabili kogo w Izraelu. A on rzekł: Cokolwiek rzeczecie, uczynię wam.
Agibiyoni anamuyankha kuti, “Ife tilibe ufulu woti nʼkulamula Sauli ndi banja lake kuti atipatse siliva kapena golide, tilibenso ufulu woti nʼkupha wina aliyense mu Israeli.” Davide anafunsa, “Mukufuna ine ndikuchitireni chiyani?”
5 Którzy rzekli do króla: Męża, który nas wygubił, i na tem był, aby nas do szczętu wytracił, żeby nas nic nie zostało we wszystkich granicach Izraelskich.
Iwo anayankha mfumu kuti, “Tsono za munthu amene anatiwononga ndi kukonza chiwembu choti titheretu ndi kukhala wopanda malo mu Israeli,
6 Wydajcie nam siedmiu mężów z synów jego, a powiesimy je Panu w Gabaa Saula, niekiedy wybranego Pańskiego. Tedy rzekł: Wydam.
mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.” Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”
7 Lecz sfolgował król Mefibosetowi, synowi Jonatana, syna Saulowego, dla przysięgi Pańskiej, która była między nimi, między Dawidem i między Jonatanem, synem Saulowym.
Koma mfumu inasunga Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli, chifukwa cha kulumbira kumene mfumu Davide ndi Yonatani mwana wa Sauli anachita pamaso pa Yehova.
8 Ale wziął król dwóch synów Resfy, córki Ai, które porodziła Saulowi, Armoniego i Mefiboseta, i pięciu synów Micholi, córki Saulowej, które porodziła Adryjelowi, synowi Barsyla Meholatyckiego,
Ndipo mfumu inatenga Arimoni ndi Mefiboseti, ana aamuna awiri a Rizipa, mwana wamkazi wa Ayiwa, amene anaberekera Sauli pamodzi ndi ana asanu a Merabi mwana wamkazi wa Sauli, amene anabereka Adirieli mwana wa Barizilai Mmeholati.
9 I wydał je w ręce Gabaonitów, i powiesili je na górze przed Panem. I umarli oni siedmiu pospołu, a pobici są w pierwsze dni żniwa, na początku żniwa jęczmiennego.
Iye anawapereka kwa anthu a ku Gibiyoni, amene anawapha nawayika pa phiri la Yehova. Onse asanu ndi awiri anafera limodzi. Iwo anaphedwa masiku oyamba kukolola barele.
10 A wziąwszy Resfa, córka Ai, wór, ropostarła go na skale, na początku żniwa, ażby na nie kropił deszcz z nieba, i nie dopuszczała ptastwu powietrznemu, padać na nie we dnie, ani zwierzowi polnemu w nocy.
Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa anatenga chiguduli ndi kudziyalira pa mwala (pamene panali mitemboyo). Kuyambira nthawi yoyamba kukolola mpaka pamene mvula inayambanso kugwa, iye sanalole kuti mbalame zikhudze mitemboyo masana kapena nyama zakuthengo usiku.
11 Tedy oznajmiono Dawidowi, co uczyniła Resfa, córka Ai, założnica Saulowa.
Davide atawuzidwa zimene Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa, mzikazi wa Sauli anachita,
12 Przetoż szedłszy Dawid wziął kości Saulowe, i kości Jonatana, syna jego od starszych Jabez Galaadskiego, którzy je byli ukradli z ulicy Betsańskiej, kędy je byli zawiesili Filistynowie onegoż dnia, gdy porazili Filistynowie Saula w Gielboe.
anapita kukatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi (iwo anawatenga mwamseri kuchoka pabwalo la ku Beti-Sani, kumene Afilisti anawapachika atapha Sauli ku Gilibowa).
13 A tak wziął stamtąd kości Saulowe i kości Jonatana, syna jego; zebrano też kości powieszonych,
Davide anakatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kumeneko ndiponso mafupa otayidwa a amene anaphedwa nawasonkhanitsa pamodzi.
14 I pogrzebli kości Saulowe i Jonatana, syna jego, w ziemi Benjamina w Sela, grobie Cysa, ojca jego, a uczynili wszystko, co był rozkazał król; a tak potem ubłagany był Bóg ziemi.
Iwo anayika mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani mʼmanda a Kisi abambo ake a Sauli ku Zera mʼdziko la Benjamini, ndipo anachita zonse zimene mfumu inalamula. Atachita zimenezi, Mulungu anayankha pemphero lopempherera dzikolo.
15 I była zasię wojna między Filistynami i Izraelem; i ciągnął Dawid i słudzy jego z nim, a walczył przeciwko Filistynom, tak, że ustał Dawid.
Nthawi inanso panali nkhondo pakati pa Afilisti ndi Aisraeli, Davide anapita ndi ankhondo ake kukamenyana ndi Afilisti ndipo iye anatopa kwambiri.
16 Tedy Jesbibenob, który był z synów jednego olbrzyma, (a grot drzewca jego ważył trzy sta syklów miedzi, a miał przepasany miecz nowy) umyślił był zabić Dawida.
Ndipo Isibi-Benobi, mmodzi mwa zidzukulu za Rafa, amene mkondo wake unkalemera makilogalamu atatu ndi theka ndipo analinso ndi lupanga latsopano, anati adzapha Davide.
17 Ale go ratował Abisaj, syn Sarwii, a raniwszy Filistyna zabił go. Przetoż przysięgli mężowie Dawidowi, mówiąc mu: Nie pójdziesz więcej z nami na wojnę, abyś nie zgasił pochodni Izraelskiej.
Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”
18 I stało się potem, że była znowu wojna w Gob z Filistynami, i zabił Sobochaj Husatycki Safa, który był z synów tegoż olbrzyma.
Patapita nthawi, panali nkhondo ina ndi Afilisti ku Gobu. Pa nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Safu, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai.
19 Była też jeszcze inna wojna w Gob z Filistynami, kędy zabił Elhana, syna Jaara Oregim, Betlehemczyk, brata Golijatowego z Giet, którego drzewce u włóczni było jako nawój tkacki.
Pa nkhondo inanso ndi Afilisti ku Gobu, Elihanani mwana wa Yaare-Oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliati Mgiti, amene anali ndi mkondo ngati ndodo yowombera nsalu.
20 Nadto jeszcze była wojna w Giet, kędy był mąż wielkiego wzrostu, mając po sześć palców u rąk swoich, i po sześć palców u nóg swoich, wszystkich dwadzieścia i cztery; a ten też był synem tegoż olbrzyma.
Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati panali munthu wina wamtali kwambiri wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
21 Ten gdy urągał Izraelowi, zabił go Jonatan, syn Samaa, brata Dawidowego.
Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
22 Ci czterej byli synowie jednego olbrzyma z Giet, a ci polegli od ręki Dawidowej, i od ręki sług jego.
Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

< II Samuela 21 >