< II Samuela 2 >

1 I stało się potem, że pytał Dawid Pana, mówiąc: Mamże iść do któregokolwiek miasta Judzkiego? Któremu Pan odpowiedział: Idź. I rzekł Dawid: Dokądże pójdę? I odpowiedział: Do Hebronu.
Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
2 Tedy tam jechał Dawid, także i dwie żony jego, Achinoam Jezreelitka, i Abigail żona przedtem Nabalowa z Karmelu.
Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
3 Także męże swe, którzy z nim byli, zabrał Dawid, każdego z domem jego, i mieszkali w miastach Hebrońskich.
Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
4 Przyszli potem mężowie Juda, i pomazali tam Dawida za króla nad domem Juda; tedy opowiadano Dawidowi, mówiąc: Mężowie z Jabes Galaad ci pogrzebli Saula.
Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
5 Tedy wyprawił Dawid posły do mężów z Jabes Galaad, i rzekł do nich: Błogosławieniście wy od Pana, którzyście ucznili to miłosierdzie nad Panem waszym Saulem, żeście go pogrzebli.
iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
6 Przetoż teraz niech uczyni Pan z wami miłosierdzie, i prawdę, a ja też oddam wam to dobrodziejstwo, żeście uczynili tę rzecz.
Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
7 Teraz tedy niech się zmacniają ręce wasze, a bądźcie mężnymi; bo choć umarł Saul, pan wasz, wszakże mnie pomazał dom Juda za króla nad sobą.
Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
8 A Abner, syn Nera, hetman nad wojskiem Saulowem, wziął Izboseta syna Saulowego, i przyprowadził go do Machanaim,
Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
9 I uczynił go królem nad Gaaladem, i nad Assury, i nad Jezreelem, i nad Efraimem, i nad Benjaminem, i nad wszystkim Izraelem.
Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
10 Czterdzieści lat miał Izboset, syn Saula, gdy począł królować nad Izraelem, a dwa lata królował; tylko dom Juda stał przy Dawidzie.
Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
11 I była liczba dni, których był Dawid królem w Hebronie nad domem Judzkim, siedm lat i sześć miesięcy.
Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
12 Potem wyszedł Abner, syn Nera, i słudzy Izboseta, syna Saulowego, z Machanaim do Gabaonu.
Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
13 Joab także, syn Sarwii, z sługami Dawidowymi wyszli, i spotkali się z sobą prawie u stawu Gabaońskiego, i zostali jedni na jednej stronie stawu, a drudzy na drugiej stronie stawu.
Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
14 Tedy rzekł Abner do Joaba: Niech teraz wstaną młodzieńcy, a poigrają przed nami. I rzekł Joab: Niech wstaną.
Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
15 Wstali tedy; i wyszło w liczbie dwanaście z Benjamińczyków ze strony Izboseta, syna Saulowego, a dwanaście z sług Dawidowych.
Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
16 Którzy uchwyciwszy się, każdy za głowę przeciwnika swego, utopił miecz swój w boku jeden drugiego, i polegli pospołu. Przetoż nazwano miejsce ono Helkatassurym, które jest w Gabaonie.
Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
17 I była bitwa bardzo sroga dnia onego, a porażon jest Abner i mężowie Izraelscy od sług Dawidowych.
Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
18 I byli też tam trzej synowie Sarwii: Joab, Abisaj, i Asael; ale Asael był prędkich nóg, jako dzika koza.
Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
19 I gonił Asael Abnera, a nie ustąpił idąc ani na prawo ani na lewo, ścigając Abnera.
Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
20 A obejrzawszy się Abner nazad, rzekł: Tyżeś jest Asael? A on mu odpowiedział: Ja.
Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
21 Tedy mu rzekł Abner: Uchyl się na prawą stronę twoję, albo na lewą stronę twoję, a pojmij sobie jednego z młodzieńców, i weźmij sobie łupy z niego; ale Asael nie chciał od niego ustąpić.
Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
22 Tedy po wtóre rzekł Abner do Asaela: Idź precz ode mnie, bym cię snać nie przebił ku ziemi; bo jakoże bym śmiał podnieść twarz moję na Joaba, brata twego?
Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
23 A gdy nie chciał ustąpić, uderzył go Abner końcem włóczni pod piąte żebro, tak iż wyszła włócznia na drugą stronę. Tamże padł, i umarł na onemże miejscu, a wszyscy, którzy przychodzili do onego miejsca, gdzie poległ Asael i umarł, zastanawiali się.
Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
24 Wszakże gonili Joab i Abisaj Abnera; i zachodziło słońce, gdy przyszli do pagórka Amma, który jest przeciw Gia na drodze pustyni Gabaońskiej.
Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
25 Tedy się zebrali synowie Benjaminowi do Abnera, skupiwszy się w jeden huf, i stanęli na wierzchu jednego pagórka.
Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
26 I zawołał Abner na Joaba i rzekł: Izali się na wieki będzie srożył ten miecz? azaż nie wiesz, że na ostatku bywa gorzkość? i dokądże nie rzeczesz ludowi, aby się wrócił od pogoni braci swych?
Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
27 Tedy rzekł Joab: Jako żywy Bóg, byś ty był nie wyzywał, zarazby się był z poranku lud wrócił, każdy od pogoni braci swych.
Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
28 A tak zatrąbił Joab w trąbę i zastanowił się wszystek lud, a nie gonili dalej Izraela, ani się więcej potykali.
Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
29 Ale Abner i mężowie jego szli polem całą onę noc, a przeprawiwszy się przez Jordan, przeszli przez wszystko Betoron, aż przyszli do Mahanaim.
Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
30 A Joab wróciwszy się z pogoni za Abnerem, zebrał wszystek lud, i nie dostawało mu sług Dawidowych dziewiętnastu mężów, i Asaela.
Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
31 Ale słudzy Dawidowi pobili z Benjamińczyków, i z mężów Abnerowych trzy sta i sześćdziesiąt mężów, którzy tam pomarli.
Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
32 A wziąwszy Asaela, pogrzebli go w grobie ojca jego, który był w Betlehem; potem szli całą noc Joab i mężowie jego, a na świtaniu przyszli do Hebronu.
Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.

< II Samuela 2 >