< II Samuela 17 >

1 Nadto rzekł Achitofel do Absaloma: Niech proszę wybiorę dwanaście tysięcy mężów, a wstawszy będę gonił Dawida tej nocy;
Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
2 I przypadnę nań, pokąd jest spracowany i zemdlonych rąk, a strwożę go, i uciecze wszystek lud, który jest z nim, a zabiję króla samego.
Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
3 A tak przywrócę wszystek lud do ciebie; bo jakoby się wszyscy ku tobie nawrócili, gdy zabiję tego męża, którego ty szukasz, a wszystek się lud uspokoi.
ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
4 I spodobało się to Absalomowi, i wszystkim starszym Izraelskim.
Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
5 Jednak rzekł Absalom: Zawołaj rychło i Chusaja Arachity, abyśmy usłyszeli, co on też powie.
Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
6 A gdy przyszedł Chusaj do Absaloma, rzekł Absalom do niego, mówiąc: Tak powiedział Achitofel: Mamyli uczynić według rady jego, czyli nie? i ty powiedz.
Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
7 Tedy odpowiedział Chusaj Absalomowi: Niedobra jest rada, którą teraz dał Achitofel.
Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
8 Nadto rzekł Chusaj: Świadomyś ojca twego i mężów jego, iż są mężni, i serca zajuszonego, jako niedźwiedzica osierociała w polu; do tego ojciec twój jest mąż waleczny, i nie będzie nocował z ludem.
Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
9 A podobno i teraz się kryje w jakiej jaskini, albo na któremkolwiek miejscu. I stałoby się, jeźliżeby kto z twoich poległ na tym początku, żeby każdy, ktoby o tem usłyszał, rzekł: Stała się porażka w ludzie, który szedł za Absalomem.
Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
10 Tedy i najmężniejszy, którego serce jako serce lwie, bardzo osłabieje; bo wie wszystek Izrael, że mężnym jest ojciec twój, i mężni wszyscy, którzy są z nim.
Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
11 Aleć radzę, aby się do ciebie cale zebrał wszystek Izrael od Dan aż do Beerseba, jako piasek, który jest przy morzu w mnóstwie, a ty żebyś osobą swoją szedł na wojnę.
“Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
12 A tak pociągniemy przeciwko niemu, na któremkolwiek miejscu znaleziony będzie, i przypadniemy nań, jako pada rosa na ziemię, i nie zostanie z niego, to jest, z tych wszystkich mężów, którzy są z nim, ani jeden.
Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
13 A jeźliżby do którego miasta uszedł, tedy zniesie wszystek Izrael do onego miasta powrozy, a pociągniemy je aż do potoku, tak iż tam nie będzie znalezion ani kamyk.
Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
14 Tedy rzekł Absalom i wszyscy mężowie Izraelscy: Lepsza jest rada Chusajego Arachity, niż rada Achitofelowa. Albowiem Pan był postanowił, aby rozerwana była rada Achitofelowa, która była dobra, a tak aby przywiódł Pan złe na Absaloma.
Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
15 I oznajmił Chusaj Sadokowi i Abijatarowi, kapłanom: Tak a tak radził Achitofel Absalomowi, i starszym Izraelskim; alem ja tak a tak radził.
Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
16 Teraz tedy poślijcie co rychlej, a oznajmijcie Dawidowi, mówiąc: Nie zostawaj tej nocy w równinach puszczy; ale bez odwłoki przejdź, by snać nie był pożarty król, i wszystek lud, który jest z nim.
Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
17 A Jonatan i Achimmas stali u studni Rogiel: i poszła dziewka, a oznajmiła im, aby poszli, i donieśli to królowi Dawidowi; bo się nie śmieli ukazać, ani wnijść do miasta.
Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
18 Wszakże obaczył je niektóry sługa i powiedział Absalomowi. Przetoż poszedłszy obadwaj spieszno, weszli w dom niektórego męża w Bahurym, który miał studnię na dworze swym, i spuścili się do niej.
Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
19 A wziąwszy niewiasta płachtę, rozciągnęła ją na wierzchu studni, i nasypała na niej krup; a tak się tego nie dowiedziano.
Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
20 Bo gdy przyszli słudzy Absalomowi do onej niewiasty w dom, rzekli: Gdzie jest Achimaas i Jonatan? odpowiedziała im niewiasta: Przeszli przez rzekę; a poszukawszy ich, i nie znalazłszy, wrócili do Jeruzalemu.
Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
21 A gdy oni odeszli, tedy owi wystąpiwszy z studni poszli, i oznajmili królowi Dawidowi, mówiąc do niego: Wstańcie, przeprawcie się co rychlej przez wodę; albowiem tak radził przeciwko wam Achitofel.
Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
22 Przetoż wstawszy Dawid, i wszystek lud, który był z nim, przeprawili się przez Jordan, pierwej niż się rozedniało, a nie został i jeden, któryby się nie przeprawił przez Jordan.
Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
23 Tedy Achitofel widząc, iż się nie stało podług rady jego, osiodłał osła, a wstawszy jechał do domu swego, do miasta swego, a rozprawiwszy dom swój, powiesił się, i umarł, a pogrzebion jest w grobie ojca swego.
Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
24 A Dawid już był przyszedł do Mahanaim, gdy Absalom przeprawił się przez Jordan, on i wszyscy mężowie Izraelscy z nim.
Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
25 I przełożył Absalom Amazę, miasto Joaba, nad wojskiem. A ten Amaza był synem męża, którego imię było Itra, Izraelczyk, który był wszedł do Abigajli, córki Nahasowej, siostry Sarwii, matki Joabowej.
Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
26 I położył się obozem Izrael z Absalomem na ziemi Galaad.
Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
27 I stało się, gdy przyszedł Dawid do Mahanaim, że Soby syn Nahasowy z Rabby, synów Ammonowych, i Machir, syn Ammijelowy z Lodebaru, i Barsylaj Galaadczyk z Rogielim,
Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
28 Pościel, i miednice, i naczynia zduńskie, i pszenicę, i jęczmień, i mąki, i krupy, i boby, i soczewice, i prażma,
anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
29 I miodu, i masła, i owiec, i serów krowich przynieśli Dawidowi, i ludowi, który był z nim, aby jedli: bo mówili: Lud ten głodny jest, i spracowany, i pragnieniem zmorzony na puszczy.
uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”

< II Samuela 17 >