< II Samuela 12 >

1 Przetoż posłał Pan Natana do Dawida; który przyszedłszy do niego, rzekł mu: Dwaj mężowie byli w jednem mieście, jeden bogaty a drugi ubogi.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 Bogaty miał owiec i wołów bardzo wiele;
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 A ubogi nie miał jedno owieczkę jednę małą, którą był kupił, i chował ją, aż urosła przy nim, także i przy dziatkach jego; z bochna jego jadała, i z kubka jego pijała, i na łonie jego sypiała, a była mu jako córka.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 A gdy przyszedł gość do onego męża bogatego, żałował wziąć z owiec swoich albo z wołów swoich, aby nagotował ucztę gościowi, który był do niego przyszedł: ale wziął owieczkę męża onego ubogiego, i nagotował ją mężowi, który był do niego przyszedł.
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Tedy zapaliwszy się gniewem Dawid na onegoż męża bardzo, rzekł do Natana: Jako żywy Pan, że godzien śmierci jest mąż, który to uczynił;
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 Owcę tę nagrodzi czworako, przeto iż to uczynił, a nie żałował go.
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 I rzekł Natan do Dawida: Tyś jest tym mężem. Tak ci mówi Pan, Bóg Izraelski: Jam cię pomazał, abyś był królem nad Izraelem, i Jam cię wyrwał z rąk Saulowych;
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 A podałem ci dom pana twego i żony pana twego na łono twoje; nadto oddałem ci dom Izraelski i Judzki, a byłoliby to mało, przydałbym ci był daleko więcej.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Czemużeś znieważył słowo Pańskie, czyniąc to złe przed oczyma jego? Uryjasza Hetejczyka zabiłeś mieczem, a żonę jego wziąłeś sobie za żonę, a samegoś zabił mieczem synów Ammonowych.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Przetoż teraz nie odejdzie miecz z domu twego aż na wieki, dlatego, iżeś mię znieważył, a wziąłeś żonę Uryjasza Hetejczyka, abyć była za żonę.
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 Tak mówi Pan: Oto, Ja wzbudzę przeciwko tobie złe z domu twego, a pobrawszy żony twe przed oczyma twemi, dam je bliźniemu twemu, a bądzie jawnie spał z żonami twojemi.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 A chociażeś to ty uczynił potajemnie, Ja jednak uczynię to przed wszystkim Izraelem, i przed słońcem.
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 Tedy rzekł Dawid do Natana: Zgrzeszyłem Panu. Zaś rzekł Natan do Dawida: Pan też przeniósł grzech twój, nie umrzesz.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 Wszakże iżeś dał przyczynę, aby urągali nieprzyjaciele Pańscy dla tej sprawy, przetoż syn, któryć się urodził, pewnie umrze.
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 Potem odszedł Natan do domu swego. Wtem zaraził Pan dziecię, które była urodziła żona Uryjaszowa Dawidowi, i zwątpiono o niem.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 Tedy się modlił Dawid Bogu za dziecięciem i pościł, a wszedłszy do pokoju, leżał przez noc na ziemi.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 I przyszli starsi domu jego do niego aby go podnieśli z ziemi; ale niechciał, i nie jadł z nimi chleba.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 I stało się dnia siódmego, że umarło dziecię. A obawiali się słudzy Dawidowi, oznajmić mu, iż umarło dziecię, bo mówili: Oto, póki jeszcze dziecię było żywę, mówiliśmy z nim, a nie słuchał głosu naszego; cóż gdy mu powiemy: Umarło dziecię, dopier oż się będzie trapił.
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 A widząc Dawid, że słudzy jego szeptali z sobą, porozumiał Dawid, iż umarło dziecię. I rzekł Dawid do sług swoich: Albo umarło dziecię? A oni odpowiedzieli: Umarło.
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 Tedy wstawszy Dawid z ziemi, umył się, i namazał się, i odmienił szaty swoje, a wszedłszy do domu Pańskiego, modlił się; potem wróciwszy się do domu swego, kazał sobie dać jeść, i położono przedeń chleb, i jadł.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 I rzekli słudzy jego do niego: Cóż to jest, coś uczynił? Dla dzicięcia, póki jeszcze żyło, pościłeś i płakałeś, a gdy umarło dziecię, wstałeś i jadłeś chleb?
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 A on rzekł: Póki jeszcze dziecię żyło, pościłem i płakałem; bom mówił: Któż wie, nie zmiłujeli się Pan nademną, że będzie żywe dziecię.
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 Ale teraz, gdy już umarło, przeczżebym miał pościć? Izali je mogę jeszcze nazad wrócić? Ja pójdę do niego, ale się ono nie wróci do mnie.
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 I cieszył Dawid Betsabeę, żonę swą, a wszedłszy do niej, spał z nią. I porodziła syna, i nazwał imię jego Salomon, a Pan go miłował.
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 Przetoż posłał Natana proroka, i nazwał imię jego Jedydyja, dla Pana.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 Potem walczył Joab przeciw Rabbie synów Ammonowych, i wziął miasto królewskie
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 A posławszy Joab posły do Dawida, rzekł: Walczyłem przeciw Rabbie i wziąłam miasto wód.
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 Przetoż teraz zbierz ostatek ludu, a połóż się obozem przeciwko miastu, i weźmij je, bym ja snać nie wziął miasta tego, a przypisanoby zwycięstwo imieniowi memu.
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 A tak zebrał Dawid wszystek lud, i ciągnął przeciw Rabbie, i dobywał go, a wziął je.
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 Wziął też koronę króla ich z głowy jego, która ważyła talent złota, a kamień drogi był na niej; i włożono ją na głowę Dawidowę, a łupów z miasta wyniósł bardzo wiele.
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 Lud też, który był w mieście, wywiódłszy, podał pod piły, i pod brony żelazne, i pod siekiery żelazne, i wegnał je w piec cegielny. A tak uczynił wszystkim miastom synów Ammonowych; i wrócił się Dawid, i wszystek lud jego do Jeruzalem.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< II Samuela 12 >