< II Królewska 8 >

1 Potem Elizeusz rzekł do onej niewiasty, której był syna wskrzesił, mówiąc: Wstań a idź, ty i dom twój, a bądź gościem, kędy będziesz mogła być; bo zawołał Pan głodu, i przyjdzie na ziemię przez siedm lat.
Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
2 Wstała tedy ona niewiasta, i uczyniła według słowa męża Bożego; a poszła ona i dom jej, i była gościem w ziemi Filistyńskiej przez siedm lat.
Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
3 I stało się po wyjściu siedmiu lat, że się wróciła ona niewiasta z ziemi Filistyńskiej, i poszła, aby wołała na króla o dom swój, i o rolę swoję.
Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
4 A na ten czas król rozmawiał z Giezym, sługą męża Bożego, mówiąc: Powiedz mi proszę wszystkie zacne sprawy, które czynił Elizeusz.
Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
5 A gdy on powiadał królowi, jako wskrzesił umarłego, oto niewiasta, której był wskrzesił syna, zawołała na króla o dom swój i o rolę swoję. I rzekł Giezy: Królu panie mój, tać to jest niewiasta, i ten syn jej, którego wskrzesił Elizeusz.
Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
6 I pytał król niewiasty, a ona mu powiedziała. I przydał jej król komornika jednego, mówiąc: Przywróć jej wszystko, co jej było, i wszystkie dochody z pola od onego dnia, którego opuściła ziemię, aż dotąd.
Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
7 Potem przyszedł Elizeusz do Damaszku, a Benadad, król Syryjski, chorował. I powiedziano mu, mówiąc: Przyszedł tu mąż Boży.
Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
8 I rzekł król do Hazaela: Weźmij w rękę swą upominek, a idź przeciwko mężowi Bożemu, i pytaj się Pana przezeń, mówiąc: Wstanęli z tej choroby?
inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
9 Przetoż szedł Hazael przeciwko niemu, a wziąwszy upominek w rękę swą, i ze wszystkich dóbr Damaskich brzemion na czterdzieści wielbłądów. I przyszedł, a stanął przed nim, mówiąc: Syn twój Benadad, król Syryjski, posłał mię do ciebie, mówiąc: Wstanęli z tej choroby?
Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
10 I odpowiedział mu Elizeusz: Idź, powiedz mu: Wprawdziebyści mógł żyć; wszakże okazał mi Pan, że pewnie umrzesz.
Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
11 Wtem pokazał mu, i stawił twarz swoję smutną, i płakał mąż Boży.
Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
12 Któremu rzekł Hazael: Czemuż pan mój płacze? I odpowiedział: Iż wiem, co uczynisz złego synom Izraelskim. Twierdze ich popalisz ogniem, a młodzieńce ich mieczem pomordujesz, i dzieci ich poroztrącasz, i brzemienne ich porozcinasz.
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
13 Tedy rzekł Hazael: Co? Izali sługa twój pies, żeby miał czynić tak wielką rzecz? I odpowiedział Elizeusz: Okazał mi Pan, że ty będziesz królem nad Syrią.
Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
14 I odszedł od Elizeusza, a przyszedł do pana swego, który rzekł do niego: Cóż ci powiedział Elizeusz? A on rzekł: Powiedział mi, żebyś pewnie mógł żyć.
Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
15 A nazajutrz wziął Hazael kołdrę i zamaczał ją w wodzie, i rozciągnął na twarzy jego. I umarł (Benadad), a Hazael królował miasto niego.
Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
16 A roku piątego Jorama, syna Achaba, króla Izraelskiego, i Jozafata króla Judzkiego, począł królować Joram, syn Jozafata, król Judzki.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
17 Trzydzieści i dwa lata miał, gdy królować począł, a ośm lat królował w Jeruzalemie.
Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
18 Ale chodził drogami królów Izraelskich, sprawując się jako dom Achabowy; bo córkę Achabową miał za żonę, i czynił złe przed oczyma Pańskiemi.
Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
19 Wszakże nie chciał Pan wytracić Judy, dla Dawida, sługi swego, jako mu był powiedział, iż mu miał dać pochodnię między synami jego, po wszystkie dni.
Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
20 Za dni jego odstąpił Edom, aby nie był pod mocą Judy; i postanowili nad sobą króla.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
21 Przetoż przyciągnął Joram do Seiru, i wszystkie wozy z nim; a wstawszy w nocy poraził Edomczyki, którzy go byli otoczyli, i hetmany wozów, tak iż lud uciekał do namiotów swoich.
Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
22 Wszakże odstąpił Edom, aby nie był pod mocą Judy, aż do dnia tego. Odstąpiło także i Lobne onegoż czasu.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
23 A inne sprawy Joramowe, i wszystko co czynił, izali nie jest napisane w kronikach o królach Judzkich?
Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
24 I zasnął Joram z ojcami swymi, a pogrzebiony jest z ojcami swymi w mieście Dawidowem; i królował Ochozyjasz, syn jego, miasto niego.
Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Roku dwunastego Jorama, syna Achaba, króla Izraelskiego, począł królować Ochozyjasz, syn Jorama, króla Judzkiego.
Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
26 We dwudziestu i dwóch latach był Ochozyjasz, gdy królować począł, a rok jeden królował w Jeruzalemie; a imię matki jego było Atalija, córka Amrego, króla Izraelskiego.
Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
27 Ten chodził drogą domu Achabowego, i czynił złe przed oczyma Pańskiemi, jako i dom Achabowy; bo był zięciem domu Achabowego.
Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
28 Przetoż wychadzał z Joramem, synem Achabowym, na wojnę przeciw Hazaelowi, królowi Syryjskiemu, do Ramot Galaadskiego; ale porazili Syryjczycy Jorama.
Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
29 A tak wrócił się król Joram, aby się leczył w Jezreelu na rany, które mu byli zadali Syryjczycy w Ramacie, gdy walczył z Hazaelem, królem Syryjskim. A Ochozyjasz, syn Jorama, króla Judzkiego, przyjechał nawiedzać Jorama, syna Achabowego, do Jezreela; bo tam chorował.
Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

< II Królewska 8 >