< II Królewska 25 >

1 I stało się roku dziewiątego królowania jego, miesiąca dziesiątego, dnia dziesiątego tegoż miesiąca, że przyciągnął Nabuchodonozor, król Babiloński, on i wszystko wojsko jego przeciw Jeruzalemowi, i położył się obozem u niego, a porobił przeciwko niemu szańce w około.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 A tak oblężone było miasto aż do jedenastego roku króla Sedekijasza.
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 Tedy dnia dziewiątego czwartego miesiąca był wielki głód w mieście, a nie miał chleba lud ziemi.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 I przełamano mur miejski, a wszyscy ludzie rycerscy uciekli w nocy drogą, kędy idą do bramy, która jest między dwoma murami, które były podle ogrodu królewskiego; a Chaldejczycy leżeli około miasta, a król uszedł drogą do pustyni.
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 I goniło wojsko Chaldejskie króla, i pojmało go na polach Jerycho; a wszystko wojsko jego rozpierzchnęło się od niego.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 A tak pojmawszy króla przywiedli go do króla Babilońskiego do Rebli, kędy o nim uczynili sąd.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 A synów Sedekijaszowych pozabijali przed oczyma jego; potem Sedekijasza oślepiwszy związali go łańcuchami miedzianemi, i zawiedli go do Babilonu.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 Potem miesiąca piątego, siódmego dnia tegoż miesiąca, ( ten jest rok dziewiętnasty królowania Nabuchodonozora, króla Babilońskiego) przyciągnął Nabuzardan, hetman żołnierski, sługa króla Babilońskiego, do Jeruzalemu;
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 I spalił do Pański, i dom królewski, i wszystkie domy w Jeruzalemie, owa wszystko budowanie kosztowne popalił ogniem.
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 Mury także Jeruzalemskie w około rozwaliło wszystko wojsko Chaldejskie, które było z onym hetmanem żołnierskim.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 A ostatek ludu, który był został w mieście, i zbiegi, którzy byli zbiegli do króla Babilońskiego, i inne pospólstwo, przeniósł Nabuzardan, hetman żołnierski.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 Tylko z ubogich onej ziemi zostawił hetman żołnierski, aby byli winiarzami i oraczami.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 Nadto słupy miedziane, które były w domu Pańskim, i podstawki, i morze miedziane, które było w domu Pańskim, potłukli Chaldejczycy, i przenieśli wszystkę miedź do Babilonu.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 Kotły też i łopaty, i naczynia muzyczne, i misy i wszystko naczynie miedziane, którem usługiwano; pobrali.
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 I kadzielnice, i miednice, i co było złotego w złocie, i co było srebrnego w srebrze, pobrał hetman żołnierski.
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 Słupy dwa, morze jedno, i podstawki, które był sprawił Salomon w domu Pańskim, a nie było wagi miedzi onego wszystkiego naczynia.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 Ośmnaście łokci wzwyż było słupa jednego, a gałka na nim miedziana; a gałka miała na wzwyż trzy łokcie, a siatka i jabłka granatowe na gałce w około, wszystko miedziane. Takiż też był i drugi słup z siatką,
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 Wziął też hetman żołnierski Sarajego, kapłana przedniego, i Sofonijasza, kapłana wtórego, i trzech odźwiernych.
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 Wziął też z miasta dworzanina jednego, który był przełożony nad ludem, rycerskim, i pięć mężów z tych, którzy stawali przed królem, którzy byli znalezieni w mieście, i pisarza przedniego wojskowego, który spisywał lud onej ziemi, i sześćdziesiąt mężów ludu z onej ziemi, którzy się znależli w mieście.
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 Pojmawszy ich tedy Nabuzardan, hetman żołnierski, zawiódł ich do króla Babilońskiego do Ryblaty.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 I pobił ich król Babiloński, a pomordował ich w Ryblacie w ziemi Emat; a tak przeniesiony jest Juda z ziemi swojej.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 Ale nad ludem, który jeszcze był został w ziemi Judzkiej, którego był zostawił Nabuchodonozor, król Babiloński, przełożył Godolijasza, syna Ahykamowego, syna Safanowego.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 A gdy usłyszeli wszyscy hetmani wojska, sami i mężowie ich, że przełożył król Babiloński Godolijasza, tedy przyszli do Godolijasza do Masfy; mianowicie, Izmael, syn Natanijaszowy, i Johanan, syn Kareaszowy, i Serajasz, syn Tanhumeta Netofatczyk a, i Jezonijasz, syn Maachatowy sami i mężowie ich.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 Którym przysiągł Godolijasz, i mężom ich, i rzekł im: Nie bójcie się być poddanymi Chaldejczykom; zostańcie w ziemi, a służcie królowi Babilońskiemu, i będzie wam dobrze.
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 I stało się miesiąca siódmego, że przyszedł Izmael, syn Natanijasza, syna Elisamowego, z nasienia królewskiego, i dziesięć mężów z nim, i zabili Godolijasza, i umarł; także Żydów i Chaldejczyków, którzy z nim byli w Masfa.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 Tedy powstał wszystek lud od małego aż do wielkiego, i hetmani wojsk, a poszli do Egiptu; bo się bali Chaldejczyków.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 Stało się także trzydziestego i siódmego roku pojmania Joachyna, króla Judzkiego, dwunastego miesiąca dnia dwudziestego siódmego tegoż miesiąca, że wywyższył Ewilmerodach, król Babiloński, tegoż roku, gdy począł królować, głowę Joachyna, króla Judzkiego, uwolniwszy go z więzienia.
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 I rozmawiał z nim łaskawie, a wystawił stolicę jego nad stolicę innych królów, którzy z nim byli w Babilonie.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 Odmienił też odzienie jego, w którem był w więzieniu, i jadł chleb zawsze przed obliczem jego po wszystkie dni żywota swego.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 Obrok też jemu naznaczony ustawicznie mu dawano od króla, na każdy dzień po wszystkie dni żywota jego.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

< II Królewska 25 >