< II Królewska 20 >
1 W one dni zachorował Ezechyjasz aż na śmierć, i przyszedł do niego Izajasz prorok, syn Amosowy, i rzekł mu: Tak mówi Pan: Rozpraw dom twój; bo umrzesz, a nie będziesz żył.
Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
2 Tedy obrócił Ezechyjasz twarz swoję do ściany, i modlił się Panu, mówiąc:
Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
3 Proszę, o Panie! wspomnij teraz, żem chodził przed tobą w prwadzie, i w sercu całem, czyniąc to, co dobrego jest w oczach twoich. I płakał Ezechyjasz płaczem wielkiem.
“Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
4 Ale jeszcze Izajasz nie wyszedł był do pół sieni, gdy się słowo Pańskie stało do niego, mówiąc:
Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
5 Wróć się, a mów do Ezechyjasza, wodza ludu mego: Tak mówi Pan, Bóg Dawida, ojca twego: Wysłuchałem modlitwę twoję, a widziałem łzy twoje; oto Ja uzdrawiam cię, dnia trzeciego wnijdziesz do domu Pańskiego;
“Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
6 I przydam do dni twoich piętnaście lat, a z ręki króla Assyryjskiego wyrwę ciebie, i to miasto; i bronić będę tego miasta dla siebie, i dla Dawida, sługi mego.
Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
7 Przytem rzekł Izajasz: Przynieście bryłę fig suchych. Którą przyniósłszy włożyli na wrzód, i zgoił się.
Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
8 I rzekł Ezechyjasz do Izajasza: Jaki znak tego, że mię uzdrowi Pan, a iż pójdę dnia trzeciego do domu Pańskiego?
Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
9 Odpowiedział Izajasz: Toć będzie znakiem od Pana, iż uczyni Pan tę rzecz, którąć obiecał. Chceszże, żeby cień postąpił na dziesięć stopni, albo żeby się na wstecz nawrócił na dziesięć stopni?
Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
10 I rzekł Ezechyjasz: Snadniej może cień postąpić na dół na dziesięć stopni, tego nie chcę; ale niech się wróci cień na wstecz na dziesięć stopni.
Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
11 Tedy wołał Izajasz prorok do Pana; i nawrócił cień po onych stponiach, któremi był postąpił na zegarze słonecznym Achazowym, na wstecz na dziesięć stopni.
Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
12 Onegoż czasu posłał Berodach Baladan, syn Baladanowy, król Babiloński, list i dary do Ezechyjasza; bo zasłyszał, że był zaniemógł Ezechyjasz.
Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
13 I wysłuchał ich Ezechyjasz i okazał im wszystkie skarbnice klejnotów swoich, srebro, i złoto, i rzeczy wonne, i olejki najwyborniejsze, i dom rynsztunków swoich, i wszystko, co się znajdowało w skarbach jego; nie było nic czego by im nie pokazał Ezechyjasz w domu swym, i we wszystkiem państwie swojem.
Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
14 Przetoż przyszedł prorok Izajasz do króla Ezechyjasza, i rzekł mu: Coć powiedzieli ci mężowie, a skąd przyszli do ciebie? I odpowiedział Ezechyjasz: Z ziemi dalekiej przyszli z Babilonu.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
15 I rzekł: Cóż widzieli w domu twoim? Odpowiedział Ezechyjasz: Wszystko, cokolwiek jest w domu moim, widzieli: nie było nic, czegobym im nie pokazał w skarbach moich.
Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
16 Ale Izajasz rzekł do Ezechyjasza: Słuchaj słowa Pańskiego.
Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
17 Oto przyjdą dni, w które zabiorą wszystko do Babilonu, cokolwiek jest w domu twoim, i cokolwiek schowali ojcowie twoi aż do dnia tego; nie zostanie ci nic, mówi Pan.
Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
18 Ale i syny twoje, którzy wynijdą z ciebie, i które spłodzisz, pobiorą, i będą komornikami na dworze króla Babilońskiego.
Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
19 Tedy rzekł Ezechyjasz do Izajasza: Dobre jest słowo Pańskie, któreś mówił. Nadto rzekł: Zaiste dobre, jeźli tylko pokój i prawda będzie za dni moich.
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
20 Ale inne sprawy Ezechyjaszowe, i wszystka moc jego, i jako uczynił sadzawkę, i rury, którymi przywiódł wodę do miasta to zapisano w kronikach o królach Judzkich.
Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
21 I zasnął Ezechyjasz z ojcami swymi, a królował Manases, syn jego, miasto niego.
Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.