< II Królewska 17 >

1 Roku dwunastego Achaza, króla Judzkiego, królował Ozeasz, syn Eli, w Samaryi nad Izraelem dziewięć lat.
Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
2 I czynił złe przed oczyma Pańskiemi, wszakże nie tak jak inni królowie Izraelscy, którzy byli przed nim.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
3 Przeciwko niemu wyciągnął Salmanasar, król Assyryjski; i stał się Ozeasz niewolnikiem jego, i dawał mu dań.
Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
4 A gdy obaczył król Assyryjski, iż się Ozeasz buntował przeciw niemu, a iż wyprawił posły do Sua, króla Egipskiego, i nie posyłał dani dorocznej królowi Assyryjskiemu, obległ go król Assyryjski, a związawszy podał go do więzienia.
Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
5 I ciągnął król Assyryjski przez wszystkę ziemię, aż przyciągnął do Samaryi, pod którą leżał przez trzy lata.
Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
6 A roku dziewiątego Ozeasza wziął król Assyryjski Samaryję, i przeniósł Izraela do Assyryi, a osadził je w Hala i w Habor nad rzeką Gozan i w miastach Medskich.
Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
7 A to się stało przeto, że grzeszyli synowie Izraelscy przeciw Panu, Bogu swemu, który je wywiódł z ziemi Egipskiej, aby nie byli pod mocą Faraona, króla Egipskiego; a bali się bogów cudzych,
Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
8 Chodząc w ustawach poganów, które był Pan wyrzucił przed obliczem synów Izraelskich, i w ustawach królów Izraelskich, które czynili.
ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
9 Obłudnie synowie Izraelscy postępowali, czyniąc co nie było rzeczą dobrą przed Panem, Bogiem swym, i pobudowali sobie wyżyny po wszystkich miastach swych, od wieży strażników aż do miasta obronnego;
Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
10 A nastawiali sobie słupów, i gajów na każdym pagórku wyniosłym, pod każdem drzewem gałęzistem,
Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
11 Paląc tam kadzidła po wszystkich górach, jako narody, które wypędził Pan przed obliczem ich; i czynili rzeczy co najgorsze, pobudzając Pana ku gniewu,
Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
12 A służyli brzydkim bałwanom, o którym im powiedział Pan, aby tego nie czynili.
Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
13 I oświadczał się Pan przeciwko Izraelowi, i przeciwko Judzie, przez wszystkie proroki, i przez wszystkie widzące, mówiąc: Nawróćcie się od dróg waszych złych, a strzeżcie rozkazania mego, i wyroków moich według wszystkiego zakonu, którym rozkazał ojcom waszym, a z którymem posłał do was proroki, sługi moje.
Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
14 Lecz nie byli posłuszni; ale zatwardzili kark swój według karku ojców swych, którzy nie wierzyli w Pana, Boga swego.
Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
15 I wzgardzili wyroki jego, i przymierze jego, które uczynił z ojcami ich, i oświadczenia jego, któremi się oświadczał przeciwko nim, a chodzili za próżnością, i stali się próżnymi, i naśladowali poganów, którzy byli około nich, o których im rozkazał Pan, aby nie czynili jako oni.
Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
16 I opuściwszy wszystkie rozkazania Pana, Boga swego, poczynili sobie lane bałwany, mianowicie dwóch cielców; poczynili też gaje, a kłaniali się wszystkiemu wojsku niebieskiemu, i służyli Baalowi.
Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
17 Przewodzili też syny i córki swe przez ogień, i bawili się wieszczbami i wróżkami, i zaprzedali się, aby czynili złe przed oczyma Pańskiemi, pobudzając go do gniewu.
Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
18 Przetoż się bardzo Pan rozgniewał na Izraela, a odrzucił je od oblicza swego, nic z nich nie zostawując, oprócz samego pokolenia Judy.
Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
19 Aleć i Juda nie strzegł przykazań Pana, Boga swego; lecz chodził w ustawach Izaelskich, których naczynili.
Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
20 Przetoż odrzucił Pan wszystko nasienie Izraelskie, i utrapił je, a podał je w rękę łupieżcom, aż je odrzucił od oblicza swego.
Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
21 Albowiem oderwał się Izrael od domu Dawidowego, a postanowili królem Jeroboama, syna Nabatowego; ale Jeroboam odwiódł Izraela od naśladowania Pana, a przywiódł je do grzeszenia grzechem wielkim.
Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
22 I chodzili synowie Izraelscy we wszystkich grzechach Jeroboamowych, które on czynił, a nie odstąpili od nich,
Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
23 A odrzucił Pan Izraela od oblicza swego, jako powiedział przez wszystkie sługi swe proroki; a tak przeniesiony jest Izrael z ziemi swej do Assyryi, aż do dnia tego.
mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
24 Potem przyprowadził król Assyryjski lud z Babilonu, i z Kuta, i z Awa, i z Emat, i z Sefarwaim, a osadził je w miastach Samaryi miasto synów Izraelskch; którzy posiadłszy Samaryję, mieszkali w miastach jej.
Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
25 A gdy tam oni mieszkać poczęli a nie bali się Pana, posłał Pan na nie lwy, którzy je zabijali.
Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
26 I powiedziano to królowi Assyryjskiemu, mówiąc: Narodowie, któreś przeniósł i osadził w miastach Samaryi, nie wiedzą obyczaju Boga onej ziemi; przetoż posłał na nie lwy, a oto je zabijają, dla tego, iż nie wiedzą obyczaju Boga onej ziemi.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
27 Tedy rozkazał król Assyryjski, mówiąc: Zawiedźcie tam jednego z kapłanów, któreście stamtąd przywiedli, aby poszedłszy mieszkał tam, i nauczał ich obyczaju Boga onej ziemi.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
28 Przyszedł tedy jeden z kapłanów, których było wzięto z Samryi, i mieszkał w Betel, a nauczał ich, jako się mieli bać Pana.
Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
29 Wszakże naczynili sobie każdy naród bogów swych, i postawili je w domu wyżyn, które byli pobudowali Samaryjczycy, każdy naród w miastach swych, w których mieszkali,
Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
30 Albowiem mężowie Babilońscy uczynili Sukkotbenot, a mężowie Kutscy uczynili Nergiel, a mężowie Ematscy uczynili Asyma.
Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
31 A Hewejczycy uczynili Nebahaz, i Tartak; a Sefarwaiczycy palili syny swe w ogniu Adramelechowi, i Anamelechowi, bogom Sefarwaimskim.
Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
32 A tak bali się Pana, naczyniwszy sobie z pośrodku siebie kapłanów na wyżynach, którzy im usługiwali w domach wyżyn.
Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
33 A choć się Pana bali, wszakże przecię bogom swoim służyli według zwyczajów onych narodów, skąd byli przeniesieni.
Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
34 Ci aż do dnia tego sprawują się według zwyczajów starych, nie boją się Pana, ani czynią według wyroków jego, i według ustaw jego, i według zakonu, i według rozkazania, które przykazał Pan synom Jakóbowym, którego przezwał Izraelem.
Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
35 Uczynił też był Pan z nimi przymierze, i rozkazał im, mówiąc: Nie bójcie się bogów cudzych, i nie kłaniajcie się im, ani im służcie, ani im ofiarujcie;
Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
36 Ale Pana, który was wywiódł z ziemi Egipskiej mocą wielką i ramieniem wyciągnionem, tego się bójcie, i jemu się kłaniajcie, i jemu ofiarujcie;
Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
37 Także ustaw, i sądów, i zakonu, i przykazań, które wam napisał, strzeżcie, czyniąc je po wszystkie dni, a nie bójcie się bogów cudzych.
Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
38 Więc przymierza, którem czynił z wami, nie zapominajcie, ani się bójcie bogów cudzych.
Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
39 Ale Pana, Boga waszego, się bójcie, a on was wybawi z ręki wszystkich nieprzyjaciół waszych;
Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
40 Lecz nie usłuchali, ale owszem według obyczaju swego dawnego czynili.
Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
41 A tak narodowie oni bali się Pana, wszakże przecię rytym bałwanom swoim służyli; a synowie ich, i synowie synów ich, według wszystkiego, co czynili ojcowie ich, tak i oni czynią, aż po dziś dzień.
Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.

< II Królewska 17 >