< II Królewska 16 >

1 Roku siedmnastego Facejasza, syna Romelijaszowego, królował Achaz, syn Joatama, króla Judzkiego.
Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Dwadzieścia lat było Achazowi, gdy królować począł, a szesnaście lat królował w Jeruzalemie; ale nie czynił, co dobrego jest przed oczyma Pana, Boga swego, jako Dawid, ojciec jego;
Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
3 Lecz chodził drogami królów Izraelskich. Nadto i syna swego dał przewieść przez ogień według obrzydliwości poganów, które był Pan wygnał przed obliczem synów Izraeliskich.
Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
4 Ofiarował też i kadził na wyżynach, i na pagórkach, i pod każdem drzewem gałęzistem.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
5 Tedy wyciągnął Rasyn, król Syryjski, i Facejasz, syn Romelijasza, król Izraelski, przeciwko Jeruzalemowi na wojnę, i oblegli Achaza; wszakże go dobyć nie mogli.
Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
6 Tegoż czasu Rasyn, król Syryjski, przywrócił zasię Elat do Syryi, a wykorzenił Żydy z Elat, ale Syryjczycy przyszedłszy do Elat, mieszkali tam aż do dnia tego.
Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
7 I posłał Achaz posły do Teglat Falasera króla Assyryjskiego, mówiąc: Sługa twój i syn twój jestem. Przyciągnij a wybaw mię z ręki króla Syryjskiego, i z ręki króla Izraelskiego, którzy powstali przeciwko mnie.
Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
8 Tedy wziąwszy Achaz srebro i złoto, które się znalazło w domu Pańskim i w skarbach domu królewskiego, posłał dar królowi Assyryjskiemu.
Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
9 Na co mu przyzwolił król Assyryjski; a przyciągnąwszy król Assyryjski pod Damaszek wziął go, i przeniósł obywatele jego do Chyr, a Rasyna zabił.
Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
10 Zatem jechał król Achaz przeciw Teglat Falaserowi, królowi Assyryjskiemu, do Damaszku; a ujrzawszy król Achaz ołtarz w Damaszku, posłał do Uryjasza kapłana wizerunek ołtarza onego i kształt jego, według wszystkiego jako był urobiony.
Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
11 I zbudował Uryjasz kapłan ołtarz według onego wszystkiego, jako był posłał król Achaz z Damaszku; tak uczynił Uryjasz kapłan pierwej, niżeli się wrócił król Achaz z Damaszku.
Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
12 A gdy się wrócił król z Damaszku, ujrzawszy ołtarz przystąpił do niego, i sprawował ofiary na nim.
Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
13 I zapalił całopalenie swoje, i ofiarę śniedną swoję, i ofiarował ofiarę mokrą swoję, i kropił krwią ofiar spokojnych swoich na ołtarzu.
Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
14 Ale ołtarz miedziany, który był przed Panem, przeniósł z przedniej strony domu, aby nie stał między ołtarzem jego, a między domem Pańskim; a postawił go po bok ołtarza ku północy.
Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
15 I rozkazał król Achaz Uryjaszowi kapłanowi, mówiąc: Na tym większym ołtarzu będziesz zapalał całopalenie poranne i ofiarę śniedną wieczorną, i całopalenie królewskie, i ofiarę śniedną jego, i całopalenie wszystkiego ludu ziemi, i ofiarę ich śniedną, i ofiary mokre ich, i wszelką krwią całopalenia, i wszelką krwią innych ofiar będziesz kropił na nim; ale ołtarz miedziany będzie mi na radzenie się Boga.
Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
16 I uczynił Uryjasz kapłan według wszystkiego, jako był rozkazał król Achaz.
Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
17 Nadto poodcinał król Achaz listwy podstawków, i pozbierał z nich wanny; do tego morze zdjął z wołów miedzianych, które były pod niem, a położył je na tle kamiennem.
Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
18 Zasłonę także sabatnią, którą było sprawiono w domu, i drzwi zewnętrzne, któremi król wchadzał, odjął od domu Pańskiego dla bojażni króla Assyryjskiego.
Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
19 A inne sprawy Achazowe, które czynił, zapisane są w kronikach o królach Judzkich.
Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 I zasnął Achaz z ojcami swymi, i pogrzebiony jest z ojcami swymi w mieście Dawidowem. A królował Ezechyjasz, syn jego miasto niego.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< II Królewska 16 >