< II Królewska 14 >

1 Roku wtórego Joaza, syna Joachaza, króla Izraelskiego, począł królować Amazyjasz, syn Joaza, króla Judzkiego.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Dwadzieścia i pięć lat miał, gdy królować począł, a dwadzieścia i dziewięć lat królował w Jeruzalemie. Imię matki jego było Joadana z Jeruzalemu.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Ten czynił, co dobrego jest przed oczyma Pańskiemi, aczkolwiek nie tak jako Dawid, ojciec jego; według wszystkiego, co czynił Joaz, ojciec jego, postępował.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Wszakże wyżyny nie były zniesione; jeszcze lud ofiarował i kadził po wyżynach.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 A gdy zmocnione było królestwo w ręku jego, pobił sługi swe, którzy byli zabili króla, ojca jego.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Lecz synów onych morderców nie pobił, jako napisano w księgach zakonu Mojżeszowego, gdzie rozkazał Pan, mówiąc: Nie pomrą ojcowie za synów, ani synowie pomrą za ojców, ale każdy za grzech swój umrze.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Ten też poraził Edomczyków dziesięć tysięcy w dolinie solnej, i wziął mocą Selę, a nazwał imię jej Jokteel, aż do tego czasu.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Tedy posłał Amazyjasz posły do Joaza, syna Joachaza, syna Jehu, króla Izraelskiego, mówiąc: Pójdź, wejrzymy sobie w oczy.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 Posłał zasię Joaz, król Izraelski, do Amazyjasza, króla Judzkiego, mówiąc: Oset, który jest na Libanie, posłał do cedru Libańskiego, mówiąc: Daj córkę twoję synowi memu za żonę. Wtem przyszedł zwierz polny, który jest na Libanie, i podeptał on oset.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Żeś ty bardzo poraził Edomczyki, dlatego się podniosło serce twoje. Chlubże się, a siedź w domu twoim; i przeczże się masz wdawać w to złe, abyś upadł ty, i Juda z tobą?
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Ale nie usłuchał Amazyjasz. Przetoż wyciągnął Joaz, król Izraelski, a wejrzeli sobie w oczy, on i Amazyjasz, król Judzki, w Betsemes, które jest w Judztwie.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 I porażony jest Juda od ludu Izraelskiego, a uciekł każdy do przybytku swego.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 Lecz Amazyjasza, króla Judzkiego, syna Joaza, syna Ochozyjaszowego, pojmał Joaz, król Izraelski, w Betsemes, a przyciągnąwszy do Jeruzalemu, zburzył mur Jeruzalemski od bramy Efraim aż do bramy narożnej, na cztery sta łokci.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 I zabrał wszystko złoto i srebro i wszystkie naczynia, które się znalazły w domu Pańskim, i w skarbach domu królewskiego, i ludzie zastawne, i wrócił się do Samaryi.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 A inne sprawy Joazowe, które czynił, i moc jego, i jako walczył z Amazyjaszem, królem Judzkim, azaż tego nie zapisano w kronikach o królach Izraelskich?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 I zasnął Joaz z ojcami swymi, a pogrzebiony jest w Samaryi z królmi Izraelskimi, a królował Jeroboam, syn jego, miasto niego.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 I żył Amazyjasz, syn Joazowy, król Judzki, po śmierci Joaza, syn Joachaza, króla Izraelskiego, piętnaście lat.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 A inne sprawy Amazyjaszowe, azaż nie są opisane w kronikach o królach Judzkich?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Potem sprzysięgli się przeciwko niemu niektórzy w Jeruzalemie; ale uciekł do Lachys. Przetoż posławszy za nim do Lachys, zabili go tam.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Skąd przynieśli go na koniach, i pogrzebiony jest w Jeruzalemie z ojcami swymi, w mieście Dawidowem.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 A tak wziąwszy wszystek lud Judzki Azaryjasza, któremu było szesnaście lat, postanowili go królem na miejscu ojca jego Amazyjasza.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Ten pobudował Elat, i przywrócił je do Judy, gdy zasnął król z ojcami swymi.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 Roku piętnastego Amazyjasza, syna Joaza, króla Judzkiego, królował Jeroboam, syn Joaza, króla Izraelskiego, w Samaryi czterdzieści lat i rok.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 A czynił złe przed oczyma Pańskiemi, nie uchylając się od wszystkich grzechów Jeroboama, syn Nabatowego, który przywiódł do grzechu Izraela.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 Ten zasię przywrócił granice Izraelskie od wejścia do Emat aż do morza pustego, według słowa Pana, Boga Izraelskiego, które był wyrzekł przez sługę swego Jonasza, syna Amaty, proroka; który był z Gatefer.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 Albowiem widział Pan utrapienie Izraelskie, im dalej tem większe, tak, że i więzień, i opuszczony zniszczeni byli, a nie był, ktoby ratował Izraela.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 A nie rzekł był Pan, aby miał wygładzić imię Izraela, żeby nie zostało pod niebem: przetoż je wybawił przez rękę Jeroboama, syna Joazaowego.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 A inne sprawy Jeroboamowe, i wszystko co czynił, i moc jego, którą walczył, i którą przywrócił Damaszek i Emat Judzkie Izraelowi, azaż tego nie zapisano w kronikach o królach Izraelskich?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 I zasnął Jeroboam z ojcami swymi, z królmi Izraelskimi, a królował Zacharyjasz, syn jego, miasto niego.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< II Królewska 14 >