< II Królewska 12 >

1 Roku siódmego Jehu począł królować Joaz, a czterdzieści lat królował w Jeruzalemie; imię matki jego było Sebija z Beersaby.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 I czynił Joaz, co dobrego było w oczach Pańskich, po wszystkie dni swoje, których go uczył Jojada kapłan.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
3 Wszakże wyżyny nie były zniesione; jeszcze lud ofiarował i kadził na onych wyżynach.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
4 I rzekł Joaz do kapłanów: Wszystkie pieniądze poświęcone, które przychodzą do domu Pańskiego, pieniądze tych, którzy idą w liczbę, pieniądze każdego z osobna według szacunku jego, i wszystkie pieniądze, które ktokolwiek dobrowolnie znosi do domu Pańskiego,
Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
5 Te wezmą do siebie kapłani każdy od znajomego swego; a oni naprawią skazę domu Pańskiego wszędy, gdzieby się znalazła skaza.
Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
6 I stało się roku dwudziestego i trzeciego króla Joaza, gdy jeszcze nie poprawili byli kapłani skazy domu,
Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
7 Że wezwał król Joaz Jojady kapłana, i innych kapłanów, i mówił do nich: Przecz nie oprawujecie skazy domu? Przetoż teraz nie bierzcie pieniędzy od znajomych waszych, ale one na poprawę skazy domu oddawajcie.
Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
8 I zezwolili na to kapłani; żeby nie brali pieniędzy od ludu, i żeby nie poprawiali skazy domu.
Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
9 Przetoż wziąwszy Jojada kapłan skrzynię jednę, uczynił dziurę w wieku jej, a postawił ją przy ołtarzu po prawej stronie, kędy wchodzono do domu Pańskiego. I kładli w nię kapłani, którzy strzegli progu, wszystkie pieniądze, które wnoszono do domu Pańskiego.
Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
10 A gdy widzieli, że było wiele pieniędzy w skrzyni, tedy przychodził pisarz królewski, i kapłan najwyższy, którzy zliczywszy chowali one pieniądze, które się znajdowały w domu Pańskim.
Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
11 I dawali pieniądze gotowe w ręce rzemieślników, przełożonych nad robotą domu Pańskiego; a ci je wydawali na cieśle, i na robotniki, którzy poprawiali domu Pańskiego;
Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
12 I na murarze, i na te, co ciosali kamienie, i na kupowanie drzewa, i ciosanego kamienia, ku poprawie skazy domu Pańskiego, i na wszystek nakład ku poprawie domu onego.
amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
13 Wszakże nie sprawowano do domu Pańskiego kubków srebrnych, naczynia do muzyki, miednic, i trąb, żadnego naczynia złotego, i naczynia srebrnego, z pieniędzy, które przynoszono do domu Pańskiego;
Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
14 Ale rzemieślnikom przełożonym nad robotą dawali je, i poprawiali za nie domu Pańskiego.
Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
15 A nie słuchano liczby tych ludzi, którym dawano pieniądze w ręce ich, aby wydawali rzemieślnikom, ponieważ to oni wiernie odprawowali.
Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
16 Ale pieniądze za występek, i pieniądze za grzechy, nie były wnoszone do domu Pańskiego; kapłanom się dostawały.
Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
17 Tedy wyciągnął Hazael, król Syryjski, a walczył przeciwko Giet, i wziął je. Potem obrócił Hazael twarz swoję, aby ciągnął przeciwko Jeruzalemowi.
Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
18 Przetoż wziął Joaz, król Judzki, wszystkie rzeczy poświęcone, które byli poświęcili Jozafat i Joram, i Ochozyjasz, ojcowie jego, królowie Judzcy, i to, co był sam poświęcił, i wszystko złoto, które się znalazło w skarbach domu Pańskiego, i domu królewskiego, a posłał to do Hazaela, króla Syryjskiego, i odciągnął od Jeruzalemu.
Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
19 Ale insze sprawy Joazowe, i wszystko co czynił, azaż to nie jest napisane w kronikach o królach Judzkich?
Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 Potem powstawszy słudzy jego sprzysięgli się między sobą i zabili Joaza w Betmello, którędy chodzą do Selli;
Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
21 To jest, zabili go Josachar, syn Semaatowy, i Jozabad, syn Sommerowy; ci słudzy jego zabili go, i umarł. A pochowali go z ojcami jego w mieście Dawidowem, i królował Amazyjasz, syn jego, miasto niego.
Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< II Królewska 12 >