< II Królewska 1 >

1 I odstąpił Moab od Izraela po śmierci Achabowej.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 A Ochozyjasz spadł przez kratę sali swej, którą miał w Samaryi, i rozniemógł się. I wyprawił posły, mówiąc im: Idźcie, poradźcie się Beelzebuba, boga Akkarońskiego, jeżeli powstanę z tej choroby.
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Ale Anioł Pański rzekł do Elijasza Tesbity: Wstań, idź przeciwko posłom króla Samaryi, i mów do nich: Izali niemasz Boga w Izraelu, iż się idziecie radzić Beelzebuba, boga Akkarońskiego?
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Przetoż tak mówi Pan: Z łoża, na któreś się położył, nie wstaniesz, ale pewnie umrzesz. I odszedł Elijasz.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 A gdy się posłowie wrócili do niego, rzekł do nich: Czemużeście się wrócili?
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 Odpowiedzieli mu: Mąż niektóry zaszedł nam drogę, i mówił do nas: Idźcie, wróćcie się do króla, który was posłał, i rzeczcie mu: Tak mówi Pan: Izaliż niemasz Boga w Izraelu, że się posyłasz radzić Beelzebuba, boga Akkarońskiego? Przetoż z łoża na któreś się położył, nie wstaniesz, ale pewnie umrzesz.
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 I rzekł do nich: Cóż za osoba była tego męża, który wam zaszedł drogę, i mówił do was te słowa?
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 I opowiedzieli mu: Mąż kosmaty, a pasem skórzanym przepasany na biodrach swych. I rzekł: Elijasz Tesbita jest.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Przetoż posłał do niego pięćdziesiątnika z pięćdziesięcioma jego, który poszedł do niego, (a oto siedział na wierzchu góry, ) i rzekł mu: Mężu Boży, król rozkazał, abyś zstąpił.
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 A odpowiadając Elijasz, rzekł pięćdziesiątnikowi: Jeźliżem jest mąż Boży, niech ogień zstąpi z nieba, a pożre ciebie i pięćdziesięciu twoich. Zstąpił tedy ogień z nieba, i pożarł go i pięćdziesięciu jego.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Znowu posłał do niego pięćdziesiątnika drugiego z pięćdziesięcioma jego, który mówił do niego, i rzekł: Mężu Boży, tak mówi król: Rychło zstąp.
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 I odpowiedział Elijasz, a rzekł mu: Jeźlim jest mąż Boży, niech zstąpi ogień z nieba, a pożre ciebie i pięćdziesiąt twoich. Tedy zstąpił ogień Boży z nieba, i pożarł go i pięćdziesięciu jego.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Tedy jeszcze posłał pięćdziesiątnika trzeciego z pięćdziesięcioma jego. Przetoż poszedł pięćdziesiątnik on trzeci, a przyszedłszy poklęknął na kolana swoje przed Elijaszem, a prosząc go pokornie, mówił do niego: Mężu Boży, proszę niech będzie droga dusza moja, i dusza tych sług twoich pięćdziesięciu w oczach twoich:
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Oto zstąpił ogień z nieba, i pożarł dwóch pięćdziesiątników pierwszych z pięćdziesięciu ich; ale teraz niech będzie droga dusza moja w oczach twoich.
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 I rzekł Anioł Pański do Elijasza: Zstąp z nim, nie bój się twarzy jego. Który wstawszy poszedł z nim do króla.
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 I rzekł mu: Tak mówi Pan: Przeto, żeś wyprawił posły radzić się Beelzebuba, boga Akkarońskiego, jakoby Boga nie było w Izraelu, abyś się pytał słowa jego, dlatego z łoża, na któremeś się położył, nie wstaniesz, ale pewnie umrzesz.
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 A tak umarł według słowa Pańskiego, które mówił Elijasz. I królował Joram miasto niego, roku wtórego Jorama, syna Jozafatowego, króla Judzkiego; albowiem on nie miał syna.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 A inne sprawy Ochozyjaszowe, które czynił, azaż nie są napisane w kronikach o królach Izraelskich?
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

< II Królewska 1 >