< II Jana 1 >
1 Starszy wybranej pani i dziatkom jej, które ja miłuję w prawdzie, a nie ja tylko, ale i wszyscy, którzy poznali prawdę,
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
2 Dla prawdy, która zostaje w nas i z nami będzie na wieki. (aiōn )
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn )
3 Niech będzie z wami łaska, miłosierdzie i pokój od Boga Ojca i od Pana Jezusa Chrystusa, Syna Ojcowego, w prawdzie i w miłości.
Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
4 Uradowałem się bardzo, żem znalazł niektóre z dziatek twoich chodzące w prawdzie, jakośmy przykazanie wzięli od Ojca.
Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
5 A teraz proszę cię, Pani! nie jako przykazanie nowe pisząc ci, ale któreśmy mieli od początku, abyśmy jedni drugich miłowali.
Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
6 A tać jest miłość, abyśmy chodzili według przykazań jego. A przykazanie to jest, jakoście słyszeli od początku, abyście w niem chodzili.
Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
7 Gdyż wiele zwodzicieli wyszło na świat, którzy nie wyznawają, że Jezus Chrystus przyszedł w ciele; ten jest zwodzicielem i antychrystem.
Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
8 Strzeżcie samych siebie, żebyśmy nie stracili tego, koło czegośmy pracowali, ale żebyśmy odpłatę zupełną wzięli.
Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
9 Wszelki, co przestępuje, a nie zostaje w nauce Chrystusowej, Boga nie ma; kto zostaje w nauce Chrystusowej, ten i Ojca, i Syna ma.
Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
10 Jeźli kto przychodzi do was, a tej nauki nie przynosi, nie przyjmujcie go w dom, ani go pozdrawiajcie.
Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
11 Albowiem kto takiego pozdrawia, uczestnikiem jest złych uczynków jego.
Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
12 Mając wam wiele pisać, nie chciałem przez papier i inkaust, ale mam nadzieję, że do was przyjdę i ustnie z wami mówić będę, aby radość nasza była zupełna.
Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
13 Pozdrawiają cię dziatki siostry twojej w Panu wybranej. Amen.
Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.