< II Kronik 7 >

1 A gdy dokończył Salomon modlitwy, tedy ogień zstąpił z nieba, i pożarł całopalenie i inne ofiary, a chwała Pańska napełniła on dom.
Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
2 I nie mogli kapłani wnijść do domu Pańskiego, przeto, że chwała Pańska napełniła dom Pański.
Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
3 I wszyscy synowie Izraelscy, widząc, gdy zstępował ogień, i chwała Pańska na dom, upadli twarzą swą na ziemię, na tło, a kłaniając się chwalili Pana, że dobry, że na wieki miłosierdzie jego.
Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
4 A król i wszystek lud sprawowali ofiary przed Panem.
Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
5 Tedy nabił król Salomon na ofiary wołów dwadzieścia i dwa tysiące, a owiec sto i dwadzieścia tysięcy, gdy poświęcali dom Boży król i wszystek lud.
Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
6 Ale kapłani stali w rzędach swych: Lewitowie także z instrumentami muzyki Pańskiej, które był sprawił Dawid król ku chwaleniu Pana, (że na wieki miłosierdzie jego) pieśnią Dawidową, którą im podał. Inni też kapłani trąbili przeciwko nim, a wszyscy Izraelczycy stali.
Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
7 Nadto poświęcił Salomon pośrodek sieni, która była przed domem Pańskim; bo tam ofiarował całopalenia, i tłustości spokojnych ofiar, przeto, że na ołtarzu miedzianym, który był sprawił Salomon, nie mogły się zmieścić całopalenia, i ofiary śniedne i tłustości.
Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
8 I obchodził Salomon onego czasu święto uroczyste przez siedm dni, i wszystek Izrael z nim, zgromadzenie bardzo wielkie, od wejścia do Emat aż do rzeki Egipskiej.
Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
9 (Potem uczynili dnia ósmego święto; albowiem poświęcenie ołtarza sprawowali przez siedm dni, i święto uroczyste obchodzili przez siedm dni.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
10 A dnia dwudziestego i trzeciego, miesiąca siódmego, rozpuścił lud do przybytków swoich, weselący się i cieszący się w sercu swem z dobrodziejstwa, które uczynił Pan Dawidowi i Salomonowi i Izraelowi, ludowi swemu.
Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
11 A tak dokończył Salomon domu Pańskiego, i domu królewskiego, a wszystko, co był umyślił w sercu swem, uczynić w domu Pańskim i w domu swym, wykonał szczęśliwie.
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
12 Potem ukazał się Pan Salomonowi w nocy, i rzekł do niego: Wysłuchałem modlitwę twoję, i obrałem to miejsce sobie za dom do ofiary.
Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
13 Jeźli zamknę niebo, żeby nie było deszczu, i jeźli rozkażę szarańczy, aby pożarła ziemię; jeźli też poślę powietrze na lud mój;
“Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
14 A jeźliby się upokorzył lud mój, nad którym wzywano imienia mego, a modliłby się, i szukałby twarzy mojej, odwróciwszy się od dróg swoich złych: tedy Ja wysłucham z nieba, i odpuszczę grzech ich, a uzdrowię ziemię ich.
ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
15 Oczy też moje otworzone będą, a uszy moje nakłonione ku modlitwie uczynionej na tem miejscu.
Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
16 Bom teraz obrał i poświęcił ten dom, aby tu przebywało imię moje aż na wieki; i będą tu oczy moje, i serce moje po wszystkie dni.
Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
17 A ty będzieszli chodził przede mną, jako chodził Dawid, ojciec twój, a będziesz się sprawował według wszystkiego, com ci przykazał, strzegąc ustaw moich i sądów moich:
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
18 Tedy utwierdzę stolicę królestwa twego, jakom uczynił umowę z Dawidem, ojcem twoim, mówiąc: Nie będzie odjęty z narodu twego mąż panujący nad Izraelem.
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
19 A jeźli się wy odwrócicie, a opuścicie ustawy moje, i przykazania moje, którem wam podał, a odszedłszy będziecie służyli bogom cudzym, i będziecie się im kłaniali:
“Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
20 Tedy ich wykorzenię z ziemi mojej, którąm im dał; a ten dom, którym poświęcił imieniowi memu, odrzucę od oblicza mego, i podam go na przypowieść, i na baśń między wszystkie narody.
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
21 Nadto i ten dom, który był sławny, każdemu mimo idącemu będzie na podziw, i rzecze: Przeczże tak uczynił Pan tej ziemi i temu domowi?
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
22 Tedy odpowiedzą: Przeto, iż opuścili Pana, Boga ojców swoich, który ich wywiódł z ziemi Egipskiej, a chwycili się bogów cudzych, i kłaniali się im, i służyli im, dlategoż przywiódł na nich to wszystko złe.
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”

< II Kronik 7 >