< II Kronik 35 >

1 Potem obchodził Jozyjasz w Jeruzalemie święto przejścia Panu; i zabili baranka wielkanocnego czternastego dnia, miesiąca pierwszego.
Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
2 I postanowił kapłanów na urzędach ich, a potwierdził ich ku posługiwaniu w domu Pańskim.
Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
3 I rzekł Lewitom, którzy uczyli wszystkiego Izraela, i byli poświęceni Panu: Postawcie skrzynię świętą w domu, który zbudował Salomon, syn Dawidowy, król Izraelski; nie będzie więcej brzemieniem na ramionach waszych. Terazże służcie Panu, Bogu waszemu, i ludowi jego Izraelskiemu.
Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
4 A nagotujcie się według domów ojców waszych, i według podziałów waszych, jako je opisał Dawid, król Izraelski, i jako je opisał Salomon, syn jego;
Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
5 A stójcie w świątnicy według podziałów domów ojcowskich, braci waszych, którzy są z ludu, i według podziału domu ojcowskiego Lewitów.
“Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
6 A tak zabijcie baranka wielkanocnego, a poświęćcie się, i przygotujcie braci waszych, sprawując się według słowa Pańskiego, podanego przez Mojżesza.
Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
7 Tedy dał Jozyjasz pospólstwu baranków z trzód, i koziełków, to wszystko na ofiary święta przejścia według tego, ile się znalazło w liczbie, trzydzieści tysięcy, a wołów trzy tysiące; to wszystko z majętności królewskiej.
Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
8 Książęta też jego dobrowolnie ludowi, kapłanom, i Lewitom dawali na ofiarę; Helkijasz, i Zacharyjasz, i Jehijel, książęta domu Bożego, oddali kapłanom na ofiary święta przejścia dwa tysiące i sześć set drobnego bydła, i wołów trzysta.
Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
9 Nadto Kienanijasz, i Semejasz, i Natanael, bracia jego, i Chasabijasz, i Jehijel, i Josabad, przedniejsi z Lewitów, oddali innym Lewitom na ofiary święta przejścia pięć tysięcy drobnego bydła, i wołów pięć set.
Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
10 A tak wszystko zgotowawszy ku służbie, stanęli kapłani na miejscach swych, i Lewitowie w porządkach swych według rozkazania królewskiego.
Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
11 I bili baranki wielkanocne, a kapłani kropili krwią ich, a Lewitowie odzierali ze skór.
Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
12 I podzielili z nich na całopalenie, aby to dali pospólstwu według podziałów domów ojcowskich na ofiarę Panu, jako napisane w księgach Mojżeszowych; także też uczynili z strony wołów.
Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
13 I piekli baranki wielkanocne ogniem według zwyczaju; a inne rzeczy poświęcone warzyli w garncach, i w kotłach, i w panwiach, i rozdawali spieszno wszystkiemu pospólstwu.
Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
14 Potem też nagotowali sobie i kapłanom. Bo kapłani, synowie Aaronowi, około całopalenia i tłustości zabawieni byli aż do nocy; przetoż Lewitowie gotowali sobie i kapłanom, synom Aaronowym.
Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
15 Także i śpiewacy, synowie Asafowi, stali w porządku swym według rozkazania Dawida i Asafa, i Hemmana, i Jedytuna, widzącego królewskiego; odźwierni też stali u każdej bramy, bo się im nie godziło odchodzić od posług ich; przetoż bracia ich Lewito wie gotowali dla nich.
Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
16 A tak zgotowana jest wszystka służba Pańska dnia onego dla obchodzenia święta przejścia, i dla ofiarowania całopalenia na ołtarzu Pańskim według rozkazania króla Jozyjasza.
Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
17 I obchodzili synowie Izraelscy, ile się ich znalazło, święto przejścia onegoż czasu, i święto uroczyste przaśników przez siedm dni.
Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
18 A nie było obchodzone święto przejścia temu podobne w Izraelu ode dni Samuela proroka; ani żaden z królów Izraelskich obchodził takiego święta przejścia, jakie obchodził Jozyjasz i kapłani, i Lewitowie, i wszystek lud Judzki, i Izraelski, ile się go znalazło, i obywatele Jeruzalemscy.
Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
19 Ośmnastego roku królowania Jozyjaszowego to święto przejścia obchodzono.
Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
20 Po tem wszystkiem, gdy naprawił Jozyjasz dom Boży, wyciągnął Necho, król Egipski, aby walczył przeciw Karchemis nad rzeką Eufrates; a Jozyjasz też wyjechał przeciwko niemu.
Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
21 Ale on posłał do niego posłów swych, mówiąc: Cóż ja mam z tobą, królu Judzki? Nie przeciwkoć tobie dziś ciągnę, ale przeciwko domowi, który ze mną walczy; i rozkazał mi Bóg, abym się pospieszył. Przestań walczyć z Bogiem, który jest ze mną, aby cię nie zabił.
Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
22 Ale nie odwrócił Jozyjasz twarzy swej od niego; owszem odmienił szaty swe, aby z nim walczył; a nie przestał na słowach Necha, które wyszły z ust Bożych. A tak przyciągnął, aby się z nim potykał na polu Magieddo.
Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
23 I postrzelili strzelcy króla Jozyjasza. Tedy rzekł król do sług swoich: Wyprowadźcie mię z bitwy, bom jest bardzo zraniony.
Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
24 I przenieśli go słudzy jego z onego wozu, a włożyli go na drugi wóz, który miał, i odwieżli go do Jeruzalemu. Tamże umarł, i pochowano go w grobach ojców jego; a wszystek lud Judzki i Jeruzalemski płakał nad Jozyjaszem.
Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
25 Uczynił też i Jeremijasz narzekanie nad Jozyjaszem, które przypominają wszyscy śpiewacy, i śpiewaczki w lamentach swych o Jozyjaszu aż po dziś dzień, i wprowadzili to w zwyczaj w Izraelu; a zapisano te rzeczy w lamentach Jeremijaszowych.
Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
26 A inne sprawy Jozyjaszowe i dobroczynności jego według tego, jako napisane w zakonie Pańskim,
Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
27 I uczynki jego pierwsze i poślednie zapisane są w księgach królów Izraelskich i Judzkich.
zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.

< II Kronik 35 >