< II Kronik 33 >

1 We dwunastym roku był Manases, gdy królować począł; a pięćdziesiąt i pięć lat królował w Jeruzalemie.
Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
2 Ten czynił złe przed oczyma Pańskiemi według obrzydłości onych narodów, które wygnał Pan przed obliczem synów Izraelskich.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
3 Albowiem znowu pobudował wyżyny, które był poburzył Ezechyjasz, ojciec jego; wystawił też i ołtarze Baalom, a nasadził gajów, i kłaniał się wszystkiemu wojsku niebieskiemu, a służył mu,
Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
4 Pobudował też ołtarze w domu Pańskim, o którym powiedział był Pan: W Jeruzalemie będzie imię moje na wieki.
Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
5 Nadto nabudował ołtarze wszystkiemu wojsku niebieskiemu we dwóch sieniach domu Pańskiego.
Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
6 I przewodził synów swych przez ogień w dolinie synów Hennomowych; nadto czasów przestrzegał, i bawił się wieszczbą i czarnoksięstwem, a ustawił czarnoksiężników i guślarzy, i bardzo wiele złego czynił przed oczyma Pańskiemi, draźniąc go.
Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
7 Postawił także bałwana rytego, którego był uczynił w domu Bożym, o którym był rzekł Bóg do Dawida i do Salomona, syna jego: W domu tym i w Jeruzalemie, którem obrał ze wszystkich pokoleń Izraelskich, położę imię moje na wieki;
Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
8 A nie dopuszczę się więcej ruszyć nodze Izraela z ziemi, którąm naznaczył ojcom waszym, by jedno strzegli i sprawowali się według wszystkiego, com i rozkazał, według wszystkiego zakonu, i ustaw, i sądów wydanych przez Mojżesza.
Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
9 Ale Manases zwiódł Judę i obywateli Jeruzalemskich, tak iż się gorzej sprawowali niż narody, które Pan wygładził przed obliczem synów Izraelskich.
Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
10 Bo choć mówił Pan do Manasesa, i do ludu jego, przecież oni nie słuchali.
Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
11 Przetoż Pan nawiódł na nich hetmanów wojska króla Assyryjskiego, którzy pojmawszy Manasesa w cierniu, i związawszy go dwoma łańcuchami, zawiedli go do Babilonu.
Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
12 Który będąc uciśniony, modlił się Panu, Bogu swemu, i upokorzył się bardzo przed obliczem Boga ojców swoich,
Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
13 I prosił go; a dał mu się uprosić, i wysłuchał modlitwę jego, a przywrócił go do Jeruzalemu na królestwo jego. Tedy poznał Manases, iż sam Pan jest Bogiem.
Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
14 Potem budował mur około miasta Dawidowego ku zachodniej stronie Gichonu potoku aż do wejścia do bramy rybnej, i otoczył murem Ofel, i wywiódł go bardzo wysoko; postanowił też hetmanów po wszystkich miastach obronnych w Judzie.
Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
15 Zniósł też bogów cudzych, i bałwana z domu Pańskiego, i wszystkie ołtarze, które był pobudował na górze domu Pańskiego, i w Jeruzalemie, i wyrzucił za miasto.
Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
16 Zatem naprawił ołtarz Pański, i sprawował na nim ofiary spokojne, i dziękczynienia, a przykazał Judzie, aby służyli Panu, Bogu Izraelskiemu.
Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
17 Wszakże jeszcze lud ofiarował na wyżynach, lecz tylko Panu, Bogu swemu.
Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
18 Ale inne sprawy Manasesowe, i modlitwa jego do Boga jego, i słowa widzących, którzy mawiali do niego w imię Pana, Boga Izraelskiego, są w księgach spraw królów Izraelskich.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
19 Modlitwa zaś jego, i jako jest wysłuchany, i każdy grzech jego, i przestępstwo jego, i miejsca, na których był pobudował wyżyny, i wystawił gaje święcone, i bałwany, przedtem niż się był upokorzył, zapisane w księgach Chozaja.
Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
20 Potem zasnął Manases z ojcami swymi, i pochowali go w domu jego; a Amon, syn jego, królował miasto niego.
Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 We dwudziestu i dwóch latach był Amon, gdy królować począł, a dwa lata królował w Jeruzalemie.
Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
22 I czynił złe przed oczyma Pańskiemi, jako czynił Manases, ojciec jego; albowiem wszystkim bałwanom, których był naczynił Manases, ojciec jego, ofiarował Amon, i służył im.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
23 A nie upokorzył się przed obliczem Pańskiem, jako się upokorzył Manases, ojciec jego; owszem ten Amon daleko więcej grzeszył.
Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
24 I sprzysięgli się przeciw niemu słudzy jego, i zabili go w domu jego.
Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
25 Ale lud onej ziemi pobił wszystkich, co się byli sprzysięgli przeciw królowi Amonowi; a postanowił lud ziemi królem Jozjasza, syna jego, miasto niego.
Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.

< II Kronik 33 >