< II Kronik 31 >
1 A gdy się to wszystko odprawiło, wyszedł wszystek lud Izraelski, który się znajdował w miastach Judzkich, i połamali słupy, a wyrąbali gaje, i poburzyli wyżyny i ołtarze po wszystkim Judzie i Benjaminie, i w Efraimie, i w Manasesie, aż do szczę tu; a potem się wrócili wszyscy synowie Izraelscy, każdy do osiadłości swojej, i do miasta swego.
Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
2 I postanowił Ezechyjasz porządki kapłanów i Lewitów według rozdziałów ich, każdego według powinności urzędu jego, kapłanów i Lewitów do całopalenia i ofiar spokojnych, aby służyli i wysławiali i chwalili Pana w bramach obozu jego.
Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
3 Także dział z królewskiej majętności ku sprawowaniu całopalenia rano i w wieczór, także całopalenia w sabaty, i na nowiu miesiąca, i w uroczyste święta, jako napisane w zakonie Pańskim.
Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
4 Rozkazał też ludowi mieszkającemu w Jeruzalemie, aby oddawali dział kapłanom i Lewitom, aby byli tem pilniejszymi w zakonie Pańskim.
Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
5 A gdy się ta rzecz rozgłosiła, znieśli synowie Izraelscy wiele pierwocin zboża, moszczu i oliwy, i owocu palmowego, i wszystkich urodzajów polnych, i dziesięciny ze wszystkiego bardzo wiele przynosili.
Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
6 Nadto synowie Izraelscy i Judzcy, którzy mieszkali w miastach Judzkich, i oni dziesięcinę z wołów i z owiec, i dziesięcinę z rzeczy świętych, poświęconych Panu, Bogu ich, zniósłszy składli na gromady.
Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
7 Trzeciego miesiąca poczęli zakładać te gromady, a miesiąca siódmego dokonali.
Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
8 Tedy przyszedłszy Ezechyjasz z książętami, obaczył one gromady, i błogosławili Panu i ludowi jego Izraelskiemu.
Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
9 Zatem wywiadywał się Ezechyjasz od kapłanów i Lewitów o onych gromadach.
Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
10 Któremu odpowiedział Azaryjasz kapłan najwyższy z domu Sadokowego, mówiąc: Jako poczęto te ofiary znaszać do domu Pańskiego, jedliśmy, i byliśmy nasyceni, a jeszcze zostało bardzo wiele: bo Pan błogosławił ludowi swemu, i tej wielkości, która jeszcze została.
ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
11 I rozkazał Ezechyjasz, aby sprawiono szpichlerze przy domu Pańskim. I sprawiono je.
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
12 A zniesiono tam wiernie ofiary podnoszenia, i dziesięciny, i rzeczy poświęcone; a nad nimi był przełożonym Kienanijasz Lewita, i Symchy, brat jego wtóry.
Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
13 Jehijel także, i Azaryjasz, i Nahat, i Asael, i Jerymot, i Josabad, i Elijel, i Ismachyjasz, i Machat, i Benajasz, byli szafarzami przy ręce Kienanijasza, i Symchy, brata jego, z rozkazania Ezechyjasza króla, i Azaryjasza, przedniejszego w domu Bożym.
Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
14 Kore też, syn Jemny, Lewita, odźwierny bramy na wschód słońca, był nad rzeczami dobrowolnie ofiarowanemi Bogu, aby rozdzielał ofiary Panu i rzeczy najświętsze.
Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
15 A byli mu na pomoc Eden, i Minjamin, i Jesua, i Semejasz, Amaryjasz, i Sechanijasz po miastach kapłańskich, mężowie wierni, aby rozdawali braciom swym działy, tak wielkiemu jako i małemu:
Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
16 Tak z narodu ich mężczyźnie we trzech latach i wyżej, jako każdemu wchodzącemu do domu Pańskiego, do powinności każdodziennej, według urzędów ich, i według usług ich, i według podziałów ich;
Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
17 I tym, którzy byli policzeni w narodzie kapłańskim według domów ojców ich, i Lewitom od tego, który miał dwadzieścia lat i wyżej, według posług i podziałów ich;
Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
18 I narodowi ich, wszystkim dziatkom ich, i żonom ich, i synom ich, i córkom ich, owa wszystkiemu zgromadzeniu; bo się oni wiernie poświęcili na urząd świętobliwością.
Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
19 Synom także Aaronowym, kapłanom, na polach przedmiejskich miast ich, po wszystkich miastach, ci mężowie, którzy z imienia mianowani są, oddawali działy, każdemu mężczyźnie z kapłanów, i każdemu urodzonemu z Lewitów.
Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
20 I uczynił tak Ezechyjasz po wszystkiem Judztwie; i czynił, co było dobrego i prawego i prawdziwego przed obliczem Pana Boga swego.
Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
21 I w każdej sprawie, którą zaczął około usługi domu Bożego, i w zakonie i w przykazaniu, szukając Boga swego, wszystko czynił z całego serca swego, i szczęściło mu się.
Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.