< II Kronik 18 >

1 I miał Jozafat bogactw i sławy bardzo wiele, a spowinowacił się z Achabem.
Tsono Yehosafati anali ndi chuma chambiri ndi ulemu, ndipo iye anachita mgwirizano wa ukwati ndi Ahabu.
2 I przyjechał po kilku latach do Achaba do Samaryi; i nabił Achab owiec i wołów wiele dla niego, i dla ludu, który był z nim, i namawiał go, aby ciągnął do Ramot Galaad.
Patapita zaka zina, iye anapita kukacheza kwa Ahabu mu Samariya. Ahabu anaphera iye pamodzi ndi anthu amene anali naye, nkhosa zambiri ndi ngʼombe ndipo anamuwumiriza kuti akathire nawo nkhondo Ramoti Giliyadi
3 I rzekł Achab, król Izraelski, do Jozafata, króla Judzkiego: Pociągnijże ze mną do Ramot Galaad? A on mu odpowiedział: Jako ja, tak i ty, a jako lud twój, tak lud mój, i będziemy z tobą na wojnie.
Ahabu mfumu ya Israeli anafunsa Yehosafati mfumu ya Yuda kuti, “Kodi mudzapita nane kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha kuti, “Ine ndili ngati inu nomwe, ndi anthu anga ngati anthu anu. Ife tikhala nanu limodzi pa nkhondoyi.”
4 Nadto rzekł Jozafat do króla Izraelskiego: Proszę, pytaj się dziś słowa Pańskiego.
Koma Yehosafati anatinso kwa mfumu ya Israeli, “Choyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
5 A tak zebrał król Izraelski proroków cztery sta mężów, i rzekł do nich: Mamże ciągnąć do Ramot Galaad na wojnę, czyli zaniechać? A oni odpowiedzieli: Ciągnij; bo je da Bóg w ręce królewskie.
Tsono mfumu ya Israeli inasonkhanitsa aneneri 400 ndipo inawafunsa kuti, “Kodi tipite kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Mulungu adzawupereka mʼdzanja la mfumu.”
6 Ale Jozafat rzekł: Niemaszże tu jeszcze którego proroka Pańskiego, żebyśmy się go pytali?
Koma Yehosafati anafunsanso kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wina wa Yehova amene ife tingafunsireko?”
7 I rzekł król Izraelski do Jozafata: Jest jeszcze mąż jeden, przez któregobyśmy się mogli radzić Pana, ale go ja nienawidzę; bo mi nie prorokuje nic dobrego, ale zawżdy złe; a tenci jest Micheasz, syn Jemlowy. I rzekł Jozafat: Niech tak nie mówi król.
Mfumu ya Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife kudzera mwa iye titha kufunsira kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa sandilosera zabwino koma zoyipa nthawi zonse. Iyeyu ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu isanene motero.”
8 Tedy zawołał król Izraelski niektórego komornika, i rzekł: Przywiedź tu rychło Micheasza, syna Jemlowego.
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa akuluakulu ake ndipo inati, “Kamutengeni Mikaya mwana wa Imula, abwere msanga.”
9 Międzytem król Izraelski, i Jozafat, król Judzki, siedzieli każdy z nich na stolicy swojej, ubrani w szaty królewskie, a siedzieli na placu u wrót bramy Samaryjskiej, a wszyscy prorocy prorokowali przed nimi.
Mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda, atavala mikanjo yawo yaufumu anali atakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopunthira tirigu pa khomo la chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
10 A Sedechyjasz, syn Chanaanowy, sprawił sobie rogi żelazne, i rzekł: Tak mówi Pan: Temi będziesz bódł Syryjczyków, aż ich wyniszczysz.
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana anapanga nyanga zachitsulo ndipo analengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi udzagunda Aaramu mpaka atawonongedwa!’”
11 Toż wszyscy prorocy prorokowali, mówiąc: Ciągnij do Ramot Galaad, a będzieć się szczęściło; albowiem je poda Pan, w ręce królewskie.
Aneneri ena onse amanenera chimodzimodzi kuti, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo kapambaneni, pakuti Mulungu adzamupereka mʼdzanja la mfumu.”
12 Tedy poseł, który chodził, aby przyzwał Micheasza, rzekł do niego, mówiąc: Oto słowa proroków jednemi usty dobrze tuszą królowi; niechże będzie, proszę, słowo twoje jako jednego z nich, a mów dobre rzeczy.
Wauthenga amene anapita kukayitana Mikaya anati kwa iye, “Taonani aneneri ena onse ngati munthu mmodzi akulosera za chipambano cha mfumu. Mawu anunso agwirizane ndi awo ndipo muyankhule zabwino.”
13 I rzekł Micheasz: Jako żyje Pan, że co mi kolwiek rozkaże Bóg mój, to mówić będę.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndidzanena zimene Mulungu wanga andiwuze.”
14 A gdy przyszedł do króla, rzekł król do niego: Micheaszu! mamyż ciągnąć na wojnę przeciw Ramot Galaad, czyli zaniechać? A on odpowiedział: Ciągnijcie, a poszczęści się wam, i będą podani w ręce wasze.
Iye atafika mfumu inamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite ku nkhondo kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Kathireni nkhondo ndipo kapambaneni, pakuti mzindawo udzaperekedwa mʼdzanja lanu.”
15 I rzekł król do niego: A wieleż cię razy mam przysięgą zobowiązywać, abyś mi nie mówił jedno prawdę w imieniu Pańskiem?
Mfumu inati kwa iye, “Kodi ndikuwuze kangati kuti ulumbire kuti usandiwuze chilichonse koma zoonadi mʼdzina la Yehova?”
16 Przetoż rzekł: Widziałem wszystek lud Izraelski rozproszony po górach jako owce, które nie mają pasterza; bo Pan rzekł: Nie mająci Pana; niech się wróci każdy do domu swego w pokoju.
Ndipo Mikaya anayankha kuti, “Ine ndinaona Aisraeli atabalalika mʼmapiri monga nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mu mtendere!’”
17 I rzekł król Izraelski do Jozafata: Izażem ci nie powiadał, że mi nic dobrego prorokować nie miał, ale złe?
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti sandinenera zabwino koma zoyipa zokhazokha?”
18 Ale on rzekł: Słuchajcież tedy słowa Pańskiego: Widziałem Pana siedzącego na stolicy jego, i wszystko wojsko niebieskie stojące po prawicy jego i po lewicy jego.
Mikaya anapitiriza ndi kunena kuti, “Imvani tsono mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu ndi gulu lonse lakumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi lamanzere.
19 I rzekł Pan: Kto zwiedzie Achaba, króla Izraelskiego, aby szedł, a poległ w Ramot Galaad? A gdy mówił jeden tak, a drugi mówił inaczej,
Ndipo Yehova anati, ‘Ndani amene adzamunyengerere Ahabu mfumu ya Israeli kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi ndi kukafera komweko?’ “Wina ananena zina, winanso ananena zina.”
20 Wystąpił duch, i stanął przed Panem, i rzekł: Ja go zwiodę. A Pan mu rzekł: Przez cóż?
Pomaliza mzimu wina unatuluka ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, “Ine ndikamunyengerera!” Yehova anafunsa kuti, “Ukagwiritsa ntchito njira yanji?”
21 I odpowiedział: Wynijdę, a będę kłamliwym duchem w ustach wszystkich proroków jego. I rzekł Pan: Zwiedziesz, i pewnie przemożesz: Idźże, a uczyń tak.
Mzimuwo unati, “Ine ndidzapita ndi kukhala mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri ake onse!” Yehova anati, “‘Iwe ukamunyengadi iyeyo. Pita kachite zimenezo.’
22 Przetoż teraz, oto dał Pan ducha kłamliwego w usta tych proroków twoich, gdyż Pan wyrzekł przeciwko tobie złe.
“Choncho Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anuwa. Yehova waneneratu kuti inu mukaona tsoka.”
23 Tedy przystąpiwszy Sedechijasz, syn Chanaanowy, uderzył Micheasza w policzek, mówiąc: A którąż drogą odszedł duch Pański odemnie, aby mówił z tobą?
Ndipo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi ndi kumenya khofi Mikaya. Zedekiya anafunsa kuti, “Kodi mzimu wochokera kwa Yehova unadzera njira iti pamene unachoka kwa ine kupita kwa iwe?”
24 I odpowiedział Micheasz: Oto ty ujrzysz dnia onego, kiedy wnijdziesz do najskrytszej komory, abyś się skrył.
Mikaya anayankha kuti, “Udzadziwa pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
25 I rzekł król Izraelski: Weźmijcie Micheasza, a odwiedźcie go do Amona, starosty miejskiego, i do Joaza, syna królewskiego.
Pamenepo mfumu ya Israeli inalamula kuti, “Tengani Mikaya ndipo mupite naye kwa Amoni, wolamulira mzindawo ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu,
26 I rzeczecie im: Tak mówi król: Wsadźcie tego do więzienia, a dawajcie mu jeść chleb utrapienia, i wodę ucisku, aż się wrócę w pokoju.
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyike munthu uyu mʼndende ndipo musamupatse kanthu kalikonse koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwera mwamtendere.’”
27 Ale odpowiedział Micheasz: Jeźliże się wrócisz w pokoju, tedy nie mówił Pan przez mię. Nadto rzekł: Słuchajcież wszyscy ludzie.
Mikaya anayankhula kuti, “Ngati inu mukabwera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo anawonjeza kuti, “Anthu nonsenu, mumve zimene ndanenazi.”
28 A tak ciągnął król Izraelski, i Jozafat, król Judzki, do Ramot Galaad.
Choncho mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
29 I rzekł król Izraelski do Jozafata: Odmienię się, a pójdę do bitwy: ale ty ubierzesz się w szaty swe. I odmienił się król Izraelski, a szli do bitwy.
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Ine ndipita ku nkhondo modzibisa koma iwe uvale mikanjo yaufumu.” Kotero mfumu ya Israeli inadzibisa ndipo inapita ku nkhondoko.
30 A król Syryjski rozkazał był hetmanom, którzy byli nad wozami jego, mówiąc: Nie potykajcie się ani z małym ani z wielkim, tylko z samym królem Izraelskim.
Tsono mfumu ya Aramu inalamulira olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu koma mfumu ya Israeli yokha.”
31 A gdy ujrzeli Jozafata hetmani, co byli nad wozami, rzekli: Król Izraelski jest. I obrócili się przeciw niemu, aby się z nim potykali; ale zawołał Jozafat, a Pan go ratował; i odwrócił ich Bóg od niego.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, iwo anaganiza kuti, “Mfumu ya Israeli ndi iyi.” Kotero anatembenuka kukamenyana naye koma Yehosafati anafuwula, ndipo Yehova anamuthandiza. Mulungu anawabweza mʼmbuyo,
32 Bo obaczywszy hetmani, co byli nad wozami, że nie ten był król Izraelski, odwrócili się od niego.
pakuti olamulira magaleta ataona kuti sanali mfumu ya Israeli, anasiya kumuthamangitsa.
33 Lecz niektóry mąż strzelił na niepewne z łuku, i postrzelił króla Izraelskiego, między nity i między pancerz; który rzekł woźnicy swemu: Nawróć, a wywieź mię z wojska; bom jest raniony.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndipo analasa mfumu ya Israeli pakati polumikizira malaya achitsulo. Mfumu inawuza oyendetsa galeta kuti, “Bwerera, undichotse pa nkhondo pano. Ndavulazidwa.”
34 I wzmogła się bitwa dnia onego, a król Izraelski stał na wozie przeciw Syryjczykom aż do wieczora: i umarł, gdy zachodziło słońce.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku lonse, ndipo mfumu ya Israeli inakhala tsonga mʼgaleta lake kuyangʼanana ndi Aaramu mpaka madzulo. Ndipo pamene dzuwa linkalowa inamwalira.

< II Kronik 18 >