< I Samuela 8 >

1 I stało się, gdy się zstarzał Samuel, że postanowił syny swe sędziami nad Izraelem.
Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
2 A było imię syna jego pierworodnego Joel, a imię drugiego syna jego Abija; ci byli sędziami w Beerseba.
Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
3 Ale nie chodzili synowie jego drogami jego; lecz udali się za łakomstwem, i brali dary, a wywracali sąd.
Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
4 Przetoż zebrali się wszyscy starsi Izraelscy, i przyszli do Samuela do Ramaty,
Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
5 I rzekli mu: Otoś się ty zstarzał, a synowie twoi nie chodzą drogami twojemi; przetoż postanów nam króla, aby nas sądził, jako je wszystkie narody mają.
Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
6 Ale się nie podobała ta rzecz Samuelowi, że mówili: Daj nam króla, aby nas sądził; przetoż modlił się Samuel Panu.
Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
7 Tedy rzekł Pan do Samuela: Usłuchaj głosu ludu tego we wszystkiem, coć powiedzą; albowiem nie tobą wzgardzili, ale mną wzgardzili, iżbym nie królował nad nimi.
Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
8 A według wszystkich spraw, które czynili od onego dnia, któregom je wywiódł z Egiptu, aż do dnia tego, gdy mię opuścili i służyli bogom obcym, tak też czynią i tobie.
Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
9 Przetoż teraz usłuchaj głosu ich, a wszakże oświadcz się jako najpilniej przed nimi, i oznajmij im prawo króla, który nad nimi ma królować.
Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
10 A tak Samuel odniósł wszystkie słowa Pańskie do ludu, który go prosił o króla,
Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
11 I mówił: Toć będzie prawo króla, który królować ma nad wami: Syny wasze brać będzie a osadzi nimi wozy swoje, i poczyni je jezdnymi, a będą biegać przed wozem jego;
Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
12 Poczyni też sobie z nich pułkowniki nad tysiącami, i rotmistrze nad pięćdziesięcioma; poczyni z nich oracze ról swoich, i żeńce żniwa swego, i te, którzyby robili rynsztunki wojenne, i potrzeby do wozów jego.
Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
13 Córki też wasze pobierze, by gotowały rzeczy wonne, i były kucharkami i piekarkami.
Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
14 Pola też wasze, i winnice wasze, i oliwnice wasze co najlepsze pobierze, a rozda sługom swoim.
Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
15 Przytem z zasiewków waszych, i z winnic waszych będzie brał dziesięciny, i rozda je komornikom swoim, i sługom swoim.
Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
16 Także sługi wasze, i dziewki wasze, i młodzieńce wasze co najgrzeczniejsze będzie brał, i osły wasze pobierze, i obróci do roboty swojej.
Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
17 Z bydła waszego dziesięcinę będzie brał, a wy będziecie niewolnikami jego.
Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
18 I będziecie wołać dnia onego dla króla waszego, którego sobie obierzecie, a nie wysłucha was Pan dnia onego.
Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
19 Ale nie chciał lud usłuchać głosu Samuelowego; owszem mówili: Nic z tego; ale król niech będzie nad nami,
Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
20 Abyśmy byli i my, jako i wszystkie narody; będzie nas sądził król nasz, a wychodząc przed nami, będzie odprawował wojny nasze.
Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
21 A wysłuchwaszy Samuel wszystkich słów ludu, odniósł je do uszu Pańskich.
Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
22 I rzekł Pan do Samuela: Usłuchaj głosu ich, a postanów nad nimi króla. Przetoż rzekł Samuel do mężów Izraelskich: Idźcie każdy do miasta swego.
Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

< I Samuela 8 >