< I Samuela 31 >

1 A Filistynowie zwiedli bitwę z Izraelem; i uciekli mężowie Izraelscy przed Filistynami, a polegli zranieni na górze Gielboe.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 I gonili Filistynowie Saula i syny jego, i zabili Filistynowie Jonatana, i Abinadaba, i Melchisuego, syny Saulowe.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 A gdy się wzmagała bitwa przeciwko Saulowi, trafili nań strzelcy, mężowie strzelający z łuku, i zraniony jest bardzo od strzelców.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
4 I rzekł Saul do wyrostka swego, który nosił broń jego: Dobądź miecza twego, a przebij mię nim, by snać nie przyszli ci nieobrzezańcy, i nie przebili mię, a nie czynili igrzyska ze mnie. Ale nie chciał wyrostek jego, bo się bardzo bał. Przetoż Saul porwał miecz i upadł nań.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 A widząc wyrostek jego, iż umarł Saul, padł i on na miecz swój, i umarł z nim.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
6 Umarł tedy Saul, i trzej synowie jego, i wyrostek jego, co za nim broń nosił, i wszyscy mężowie jego dnia onego wespół.
Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
7 Co gdy ujrzeli mężowie Izraelscy, którzy za doliną, i za Jordanem mieszkali, iż uciekali mężowie Izraelscy, a iż umarł Saul, i synowie jego, odbieżawszy miast, pouciekali też, a przyszedłszy Filistynowie mieszkali w nich.
Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 A nazajutrz przyszli Filistynowie, aby odzierali pobite; i znaleźli Saula, i trzech synów jego leżących na górze Gielboe.
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
9 A uciąwszy głowę jego, zdarli z niego zbroję jego, i posłali po ziemi Filistyńskiej wszędzie, aby to opowiadano w kościele bałwanów ich, i między ludem.
Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 I położyli zbroję jego w kościele Astarot; ale ciało jego przybili na murze Betsan.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
11 Tedy usłyszawszy o tem obywatele Jabes Galaad, co uczynili Filistynowie Saulowi;
Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 Wstali wszyscy mężowie mocni, i szli przez onę całą noc, i wzięli ciało Saulowe, i ciała synów jego z muru Betsan, a przyszedłszy do Jabes spalili je tam.
anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
13 A wziąwszy kości ich, pogrzebli je pod drzewem w Jabes, i pościli siedm dni.
Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.

< I Samuela 31 >